2 Akorinto 9 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Akorinto 9:1-15

1Nʼkosafunika kuti ndikulembereni za utumiki othandiza anthu a Mulungu. 2Popeza ndikudziwa mtima wanu wofuna kuthandiza, ndipo ndakhala ndikuwawuza monyadira a ku Makedoniya za chimenechi. Ndimawawuza kuti inu a ku Akaya munakonzeka kale chaka chatha kuti mupereke. Ndipo changu chanu chapatsa chidwi ambiri mwa iwo kuti nawonso achitepo kanthu. 3Koma ndikutumiza abalewo kuti kukunyadirani kwathu pa zimenezi kutsimikizike kuti si kwachabe ndi kuti mukhale okonzeka monga ndinanenera. 4Pakuti nditabwera kumeneko ndi abale ena a ku Makedoniya, ndikukupezani kuti simunakonzeke, tingadzachite manyazi chifukwa chokudalirani. Koma amene angadzachite manyazi kwambiri ndi inuyo. 5Choncho ndinaganiza kuti nʼkofunika kupempha abale kuti adzakuchezereni ineyo ndisanafike, ndikuti adzatsirize kukonzekera mphatso zomwe munalonjeza kupereka mowolowamanja. Motero mphatsoyo idzakhala yokonzeratu, ndipo idzakhala mphatso yoperekedwa mowolowamanja, osati mokakamizidwa.

Kupereka Mowolowamanja

6Takumbukirani mawu awa: Amene adzala pangʼono, adzakololanso pangʼono, ndipo amene adzala zochuluka, adzakololanso zochuluka. 7Munthu aliyense apereke chimene watsimikiza mu mtima mwake kuti apereka, osati monyinyirika kapena mokakamizidwa, pakuti Mulungu amakonda wopereka mokondwera. 8Ndipo Mulungu akhoza kukudalitsani kwambiri, kuti inuyo nthawi zonse mukhale ndi zinthu zokukwanirani, ndiponso ndi zina zochuluka kuti muthandize pa ntchito zonse zabwino. 9Paja analemba kuti,

“Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka,

chilungamo chake chimanka mpaka muyaya.”

10Tsono Mulungu amene amapereka mbewu kwa wofesa, ndiponso chakudya kuti adye, adzaperekanso mbewu mʼnkhokwe zanu ndi kuzichulukitsa. Iye adzachulukitsanso zipatso za chilungamo chanu. 11Adzakulemeretsani pa zonse kuti mukhale owolowamanja pa nthawi zonse. Ndipo kuwolowamanja kwanu kudzera mwa ife, kudzakhala kuthokoza kwa Mulungu.

12Ntchito imene mukugwirayi siyongothandiza kokha anthu a Mulungu kupeza zosowa, komanso ikuthandiza kuti anthu ambiri ayamike Mulungu. 13Chifukwa cha ntchito imene mwawatsimikizira nokha, anthu ena onse adzayamika Mulungu chifukwa cha kumvera kwanu kumene kumaonekera pamene mukuvomereza Uthenga Wabwino wa Khristu, ndiponso chifukwa chowagawira mowolowamanja iwowo pamodzi ndi wina aliyense. 14Ndipo iwowo adzakupemphererani mwachikondi chifukwa cha chisomo choposa chimene Ambuye wakupatsani. 15Tiyamike Mulungu chifukwa cha mphatso zake zosaneneka!

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

2 Коринфянам 9:1-15

Аллах вознаграждает щедрость

1Мне нет нужды писать вам о помощи святому народу Аллаха в Иерусалиме. 2Я знаю ваше горячее желание помочь, и я даже хвалил вас перед македонцами. Я говорил им о том, что вы в Ахаии готовы были к такому пожертвованию ещё в прошлом году, и ваше рвение побудило и их к действиям. 3Однако я посылаю к вам братьев, чтобы в этом случае наша похвала о вас не была пустой и чтобы вы оказались готовы, как я и говорил вам. 4Ведь если македонцы придут со мной и найдут, что вы, о ком мы говорили с такой уверенностью, не готовы, то нам будет стыдно, не говоря уже о вас. 5Поэтому я посчитал необходимым убедить братьев посетить вас заранее, чтобы завершить сбор пожертвований, как вы сами обещали. Тогда и будет видно, что вы делаете это не по принуждению, а добровольно.

6Помните: кто скупо сеет, тот скупо и жнёт, и кто сеет щедро, тот щедро и жнёт. 7Каждый пусть даёт столько, сколько ему подсказывает сердце, не с огорчением и не по принуждению, потому что Аллах любит того, кто жертвует с радостью. 8Аллах может обеспечить вас всем, что нужно, чтобы у вас всегда было всего в достатке и с лихвой хватало ещё на любое доброе дело, 9как написано:

«Он щедро раздал своё имущество бедным,

и праведность его не забудется вовек!»9:9 Заб. 111:9.

10И Тот, Кто даёт семя сеятелю, Кто даёт людям хлеб в пищу, умножит посеянное вами и увеличит жатву вашей праведности9:10 Ср. Ис. 55:10; Ос. 10:12.. 11Вы станете так богаты всем, что всегда сможете щедро помогать людям, и за ваш щедрый дар, переданный через нас, они будут благодарить Аллаха.

12Ваше служение не только помогает нуждам святого народа Аллаха, но и вызывает всё большую и большую благодарность Аллаху. 13И, видя это ваше служение милосердия, люди будут славить Аллаха за вас, потому что вы верны Радостной Вести об аль-Масихе, которую вы исповедуете, и делитесь с ними и со всеми тем, что имеете сами. 14Они будут молиться о вас и будут тянуться к вам благодаря безмерной благодати, которая дана вам Аллахом. 15Благодарность Аллаху за Его неописуемый дар!