2 Akorinto 2 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Akorinto 2:1-17

1Kotero ndinatsimikiza maganizo anga kuti ndisachitenso ulendo wina owawa wobwera kwanuko. 2Pakuti ngati ndikumvetsani chisoni, kodi angandisangalatse ndani, kupatula inuyo amene ndakumvetsani chisoni? 3Nʼchifukwa chake ndinakulemberani monga ndinachitiramo kuti nditabwera kwanuko ndisadzamve chisoni ndi anthu oyenera kundisangalatsa. Ndinali ndi chikhulupiriro ndi inu nonse kuti inuyo mukakhala ndi chimwemwe poona kuti inenso ndili ndi chimwemwe. 4Pakuti ndinakulemberani kalata ija ndili wopsinjika ndi wowawidwa mtima kwambiri ndi kutuluka misozi yambiri, osati pofuna kukumvetsani chisoni koma kuti ndikudziwitseni kuti ndimakukondani kwambiri.

Za Kukhululukira Wolakwa

5Koma ngati wina wamvetsa chisoni, sanamvetse chisoni ine ndekha, koma koposa mosawonjezera wakhumudwitsa nonsenu, kunenatu mosawonjezera. 6Chilango chimene ambiri a inu mwamupatsa munthu ameneyu nʼchokwanira. 7Mʼmalo mwake tsono, muyenera kumukhululukira ndi kumulimbikitsa mtima kuti asamve chisoni choposa muyeso, angataye mtima. 8Choncho ndikukupemphani kuti mutsimikizire chikondi chanu pa iye. 9Cholinga china chimene ndinakulemberani kalata ija chinali chofuna kukuonani ngati mudzandimvera pa zonse. 10Aliyense amene mumukhululukire, inenso ndimukhululukira. Ndipo ndikakhululukira, ngati pali kanthu koti ndikhululukire, ndiye kuti ndakhululuka chifukwa cha inu pamaso pa Khristu, 11kupewa kuti Satana angapezere mpata pa ife, pajatu timadziwa machenjerero ake.

Atumiki a Pangano Latsopano

12Tsono nditafika ku Trowa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Khristu, nʼkupeza kuti Ambuye anditsekulira khomo, 13ndinasowa mtendere mu mtima mwanga, chifukwa sindinapezeko mʼbale wanga Tito. Choncho ndinatsanzikana ndi anthu kumeneko nʼkupita ku Makedoniya.

14Koma tithokoze Mulungu amene amatitsogolera nthawi zonse monga ogwidwa ku nkhondo a Khristu pa chipambano chake. Tsono amatigwiritsa ntchito yofalitsa ponseponse nzeru zodziwira Khristu ngati fungo labwino. 15Pakuti kwa Mulungu ndife fungo labwino la Khristu pakati pa iwo amene akupulumutsidwa ndi amene akuwonongeka. 16Kwa amene akuwonongeka ndife fungo la imfa, limawapha. Ndipo kwa amene akupulumuka ndife fungo lamoyo, limawapatsa moyo. Ndani angayithe ntchito yotereyi? 17Kusiyana ndi ena ambiri, ife sitilalikira Mawu a Mulungu kuti tipeza phindu. Mʼmalo mwake, ife mwa Khristu timayankhula pamaso pa Mulungu moona mtima, monga anthu otumidwa ndi Mulungu.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

2 Коринфянам 2:1-17

1Поэтому я решил больше не приходить к вам только для того, чтобы вас огорчать. 2Если я буду вас огорчать, то кто же сможет тогда порадовать меня? Кто, как не вы, которых я огорчаю? 3Я написал вам то послание2:3 Хотя некоторые верят, что здесь говорится о «Первом послании Павлуса верующим в Коринфе», большинство толкователей считает, что речь идёт о каком-то другом послании, которое было утрачено и до нас не дошло. для того, чтобы, придя к вам, не оказаться огорчённым теми, о ком я хотел бы радоваться, и я уверен, что моя радость – это наша общая радость. 4Мне очень нелегко было писать вам так; я писал со слезами и с болью в сердце. Но моей целью было не огорчить вас, а дать вам знать, как сильно я вас люблю.

Прощение грешника

5Тот, кто доставил мне печаль, огорчил не только меня, а отчасти, чтобы не сказать больше, и всех вас. 6Для этого человека достаточно того наказания, которое он уже получил от большинства из вас. 7А теперь простите его и успокойте, чтобы ему не быть подавленным невыносимой печалью. 8Умоляю вас, подтвердите свою любовь к нему.

9Я писал вам также для того, чтобы проверить вас, будете ли вы послушны во всём. 10А кого вы прощаете, того и я прощаю. А кого я прощаю, если ему действительно есть что прощать, того я прощаю ради вас перед Масехом, 11чтобы сатана не смог нас перехитрить, а намерения сатаны мы прекрасно знаем.

Переживания в Троаде

12Когда я пришёл в Троаду возвещать Радостную Весть о Масехе, то Повелитель открыл мне дверь для служения. 13Но я не мог успокоиться, потому что не нашёл там моего брата по вере Тита. Поэтому я попрощался с верующими из Троады и отправился в Македонию2:13 Павлус планировал встретиться в Троаде с Титом, который должен был прийти туда из Коринфа (см. 8:6). Но не дождавшись его, Павлус пошёл ему навстречу..

Победа через Масеха

14Я благодарен Всевышнему, Который всегда ведёт нас, находящихся в единении с Масехом, в Своей триумфальной процессии и повсюду распространяет через нас благоухание познания о Нём. 15Потому что мы для Всевышнего благовоние, возжигаемое Масехом, среди тех, кто принимает спасение2:15 Спасение – от пламени ада (см. Иуда 1:23), от гнева Всевышнего и Его судов (см. Рим. 5:9), от суетной жизни (см. 1 Пет. 1:18), от греха (см. Мат. 1:21) и от дьявола (см. 2 Тим. 2:26)., и тех, кто идёт к погибели. 16Для одних мы – запах смертоносный, для других – живительное благоухание. И кто способен на такое служение?! 17При этом мы не торгуем вразнос словом Всевышнего, как это делают многие. Будучи в единении с Масехом, мы говорим искренне перед Всевышним как люди, посланные Всевышним.