1 Timoteyo 5 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Timoteyo 5:1-25

Malangizo kwa Amayi Amasiye, Akulu Ampingo ndi Akapolo

1Usadzudzule munthu wachikulire mokalipa, koma umuchenjeze ngati abambo ako. Achinyamata uwatenge ngati abale ako. 2Amayi achikulire uwatenge ngati amayi ako ndipo amayi achitsikana uwatenge ngati alongo ako, nʼkuyera mtima konse.

3Uziwachitira ulemu akazi amasiye amene ali okhaokha. 4Koma ngati mkazi wamasiye ali ndi ana ndi zidzukulu, anawo ayambe aphunzira kukwaniritsa udindo wawo pa banja lawo moopa Mulungu, potero akubweza zabwino kwa makolo awo ndi agogo awo. Pakuti zimenezi ndiye zimakondweretsa Mulungu. 5Mkazi wamasiye amene ali yekha ndi wopanda womuthandiza, ameneyo wayika chiyembekezo chake pa Mulungu, ndipo amapemphera kosalekeza usana ndi usiku kuti Mulungu azimuthandiza. 6Koma mkazi wamasiye amene amangokhalira kuchita zosangalatsa moyo wake, wafa kale ngakhale akanali ndi moyo. 7Pereka malangizo amenewa kwa anthu kuti akhale opanda zolakwa. 8Ngati wina sasamalira abale ake, makamaka a mʼbanja mwake mwenimweni, ameneyo wakana chikhulupiriro ndipo ndi woyipa kuposa wosakhulupirira.

9Mayi wamasiye aliyense amene sanakwanitse zaka 60 zakubadwa, asakhale mʼgulu la akazi amasiye. Akhale woti anakwatiwapo ndi mwamuna wake mmodzi yekha. 10Akhale mayi woti amadziwika bwino pa ntchito zake zabwino monga kulera ana, kusamalira alendo, kusambitsa mapazi a anthu a Mulungu, kuthandiza amene ali pa mavuto ndi kudzipereka pa ntchito zonse zabwino.

11Akazi amasiye achitsikana, usawayike mʼgulu limeneli. Pakuti zilakolako zawo zikayamba kuwavutitsa nʼkuwalekanitsa ndi Khristu, amafuna kukwatiwanso. 12Zikatero amadziweruza okha chifukwa aphwanya lonjezo lawo loyamba. 13Komanso amakhala ndi chizolowezi cha ulesi ndi kumangoyenda khomo ndi khomo. Ndipo sikungokhala aulesi kokha komanso kuchita miseche, kududukira za eni ake, kumangokamba zinthu zosayenera kukamba. 14Kotero, ndikulangiza akazi amasiye achitsikana kuti akwatiwe, akhale ndi ana, asamalire makomo awo ndipo asamupatse mdani mpata wonyoza 15Akazi amasiye ena apatuka kale nʼkumatsatira Satana.

16Ngati mayi aliyense wokhulupirira ali ndi akazi amasiye amene akuwasamalira, apitirizebe kuwasamalira ndipo asalemetse mpingo, kuti mpingo uthandize akazi amasiye amene ali okhaokha.

17Akulu ampingo amene amayangʼanira bwino zochitika za mu mpingo, ndi oyenera ulemu wowirikiza, makamaka amene ntchito yawo ndi kulalikira ndi kuphunzitsa. 18Pakuti Mawu a Mulungu amati, “Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu,” ndi “Wantchito ngoyenera kulandira malipiro ake.” 19Usamamvere mawu oneneza akulu ampingo pokhapokha patakhala mboni ziwiri kapena zitatu. 20Akulu ampingo amene akuchimwa, uwadzudzule poyera kuti ena aphunzirepo.

21Ndikukulamulira pamaso pa Mulungu, pamaso pa Yesu Khristu ndi pamaso pa angelo osankhika, kuti usunge malangizowa mosachotsera ndipo usachite kalikonse mokondera.

22Usafulumire kusanjika manja munthu, ndipo usavomerezane ndi anthu ena pa machimo. Usunge bwino kuyera mtima kwako.

23Uleke kumangomwa madzi okha, koma uzimwako vinyo pangʼono chifukwa cha vuto lako la mʼmimba ndi kudwala kwako kwa pafupipafupi.

24Anthu ena machimo awo amaonekeratu poyera, amakafika pa mpando wachiweruzo eni akewo asanakafike. Machimo a anthu ena amabwera mʼmbuyo mwawo. 25Momwemonso, ntchito zabwino zimaonekera poyera, ndipo ngakhale zipande kutero, sizingatheke kubisika.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

提摩太前書 5:1-25

信徒的責任

1不要斥責年長的,要像對待父親一樣勸他們;對待青年男子要情同手足; 2對待年長的婦女要情同母親;對待青年女子要心思純正,視她們如姊妹。

3要敬重和幫助那些真正有需要的寡婦。 4如果寡婦有兒孫,就要叫她們的兒孫在家中學習盡孝道,奉養她們,以報答養育之恩,這是上帝所悅納的。 5真正有需要、無依無靠的寡婦仰賴上帝的幫助,晝夜不住地禱告祈求。 6但貪圖享受的寡婦雖然活著,卻已經死了。 7你當教導眾人這些事,好叫他們無可指責。 8誰不照顧自己的親屬,尤其是不照顧自己的家人,就是違背真道,比不信的人還壞。

9列入名冊的寡婦必須年滿六十歲,在婚姻上從一而終, 10並且在善事上有好名聲,如教養兒女、接待外人、服侍聖徒、救助困苦、竭力做各種善事。

11不要把年輕的寡婦列入名冊,因為當她們情慾衝動,無法持守對基督的委身時,就想再嫁, 12以致違背了起初的誓言而受審判。 13況且,她們不僅懶散成性,四處串門,還說長道短,好管閒事,搬弄是非。 14所以,我建議年輕的寡婦再嫁,生兒育女,料理家務,不要給仇敵毀謗的機會, 15因為有些人已經偏離正道,去追隨撒旦了。 16女信徒的家裡若有寡婦,就應該自己照顧她們,免得加重教會的負擔,這樣教會才能照顧那些真正無依無靠的寡婦。

17那些善於管理教會的長老,尤其是那些辛勤傳道和教導人的,理當得到加倍的尊敬和報酬。 18因為聖經上說:「牛在踩穀時,不可籠住牠的嘴。」又說:「做工的得報酬是應該的。」 19若有人向你控告長老,必須有兩三個證人,否則不要受理。 20那些一直犯罪的人,你要當眾責備他們,以警戒眾人。

21我在上帝和主耶穌基督以及蒙揀選的眾天使面前吩咐你:要遵行這些話,不要有成見,不要偏心; 22為人行按手禮,不要操之過急。不要沾染別人的罪,要潔身自好。

23你的胃不好,經常生病,不要只喝水,要稍微喝一點酒。

24有些人的罪很明顯,自招審判,有些人的罪日後才暴露出來。 25同樣,有些善行很明顯,不明顯的也不會被長久埋沒。