1 Timoteyo 2 – CCL & PEV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Timoteyo 2:1-15

Malangizo Achipembedzo

1Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika. 2Mupempherere mafumu ndi onse aulamuliro, kuti tikhale moyo wamtendere ndi bata, woopa Mulungu ndi oyera mtima. 3Izi ndi zabwino ndipo zimakondweretsa Mulungu Mpulumutsi wathu, 4amene amafuna kuti anthu onse apulumutsidwe ndipo kuti adziwe choonadi. 5Pakuti pali Mulungu mmodzi yekha ndi Mʼkhalapakati mmodzi yekha pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja Khristu Yesu. 6Iyeyu anadzipereka kukhala dipo lowombolera anthu onse. Umenewu ndi umboni umene waperekedwa mu nthawi yake yoyenera. 7Nʼchifukwa chake anandisankha kukhala mlaliki ndiponso mtumwi wophunzitsa anthu a mitundu ina mawu achikhulupiriro choona. Sindikunama ayi, ndikunena zoona.

8Choncho ndikufuna kuti paliponse popemphera, amuna azikweza manja awo kwa Mulungu mopanda mkwiyo kapena kukangana.

9Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali. 10Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.

11Amayi azikhala chete pophunzitsidwa ndi mtima ogonjera kwathunthu. 12Ine sindikulola kuti amayi aziphunzitsa kapena kulamulira amuna; koma akhale chete. 13Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa kenaka Hava. 14Ndipo Adamu si amene ananyengedwa koma mkazi ndiye amene ananyengedwa nachimwa. 15Ndipo mkazi adzapulumutsidwa pobereka mwana ngati apitiriza kukhala mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkuyera mtima pamodzi ndi kudzichepetsa konse.

La Parola è Vita

1 Timoteo 2:1-15

Come e per che cosa si deve pregare

1Mi raccomando, dunque, prima di ogni altra cosa, che si facciano domande, preghiere, intercessioni e ringraziamenti per tutti gli uomini.

2Pregate per i re e per tutti quelli che sono al potere e che hanno grandi responsabilità, affinché si possa vivere tutti in pace una vita serena e dedicata al Signore. 3Questa è una cosa buona che piace a Dio, nostro Salvatore. 4Egli vuole che tutti gli uomini siano salvati e comprendano la verità fino in fondo. 5Cʼè un unico Dio, Egli sta da una parte, mentre tutti gli uomini sono dalla parte opposta, e cʼè un solo mediatore che può riunire gli uomini a Dio: Gesù Cristo uomo, 6che ha dato la vita come prezzo di riscatto per tutti noi.

Questo è il messaggio che, al momento opportuno, Dio ha dato al mondo. 7Per questo io sono stato scelto come araldo e apostolo di Dio, per insegnare questa verità ai pagani e indicar loro come possono essere salvati per mezzo della fede. È la pura verità. 8Io voglio dunque che in qualsiasi luogo, gli uomini preghino, alzando al cielo mani pure, senza collera, né discussioni. 9-10Così pure voglio che le donne si vestano in modo decoroso, con pudore e modestia. Le donne cristiane devono essere notate per la loro bontà e gentilezza, come si conviene a donne che dicono di amare Dio, non per il modo in cui si acconciano i capelli, né per i gioielli o i vestiti eleganti. 11Devono ascoltare e imparare in silenzio e con umiltà.

12Non permetto a nessuna donna dʼinsegnare, né di comandare al marito; le donne devono starsene tranquille. 13Perché? Perché Dio creò per primo Adamo e poi Eva. 14E non fu Adamo a lasciarsi ingannare da Satana, ma Eva, che si rese colpevole di peccato. 15Perciò Dio mandò alle donne i dolori del parto. Tuttavia salverà la loro anima, a condizione che perseverino nella fede, nellʼamore e nella sottomissione a Dio.