1 Timoteyo 2 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Timoteyo 2:1-15

Malangizo Achipembedzo

1Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika. 2Mupempherere mafumu ndi onse aulamuliro, kuti tikhale moyo wamtendere ndi bata, woopa Mulungu ndi oyera mtima. 3Izi ndi zabwino ndipo zimakondweretsa Mulungu Mpulumutsi wathu, 4amene amafuna kuti anthu onse apulumutsidwe ndipo kuti adziwe choonadi. 5Pakuti pali Mulungu mmodzi yekha ndi Mʼkhalapakati mmodzi yekha pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja Khristu Yesu. 6Iyeyu anadzipereka kukhala dipo lowombolera anthu onse. Umenewu ndi umboni umene waperekedwa mu nthawi yake yoyenera. 7Nʼchifukwa chake anandisankha kukhala mlaliki ndiponso mtumwi wophunzitsa anthu a mitundu ina mawu achikhulupiriro choona. Sindikunama ayi, ndikunena zoona.

8Choncho ndikufuna kuti paliponse popemphera, amuna azikweza manja awo kwa Mulungu mopanda mkwiyo kapena kukangana.

9Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali. 10Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.

11Amayi azikhala chete pophunzitsidwa ndi mtima ogonjera kwathunthu. 12Ine sindikulola kuti amayi aziphunzitsa kapena kulamulira amuna; koma akhale chete. 13Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa kenaka Hava. 14Ndipo Adamu si amene ananyengedwa koma mkazi ndiye amene ananyengedwa nachimwa. 15Ndipo mkazi adzapulumutsidwa pobereka mwana ngati apitiriza kukhala mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkuyera mtima pamodzi ndi kudzichepetsa konse.

Korean Living Bible

디모데전서 2:1-15

기도의 향기

1나는 무엇보다도 먼저 이것을 권합니다. 그대는 모든 사람을 위하여 하나님 께 열심히 기도하며 감사하시오.

2왕들과 높은 자리에 있는 모든 사람들을 위해서도 그렇게 하시오. 그것은 안정되고 평온한 가운데서 경건하고 거룩한 생활을 하기 위한 것입니다.

3이런 생활은 아름다운 것이며 우리 구주 하나님을 기쁘게 해 드리는 일입니다.

4하나님께서는 모든 사람이 다 구원받고 진리를 알게 되기를 원하십니다.

5하나님은 한 분뿐이시며 하나님과 사람 사이의 중재자도 한 분뿐이시니 그분이 바로 사람이신 그리스도 예수님이십니다.

6그리스도 예수님은 모든 사람을 구원하시려고 자신을 바치셨습니다. 이것은 하나님께서 때가 되어 약속을 이루신 증거입니다.

7나는 이 그리스도를 전하기 위해 전도자와 사도로 임명을 받았으며 믿음과 진리 안에서 이방인의 스승이 되었습니다. 이것은 거짓말이 아닌 사실입니다.

8그러므로 남자들은 화를 내거나 다투지 말고 어디서나 거룩한 손을 들어 기도하기 바랍니다.

9여자들도 머리를 지나치게 꾸미거나 귀금속과 비싼 옷으로 단장하지 말고 정숙하고 단정한 몸가짐을 하십시오.

10하나님을 섬기는 여자는 마땅히 선한 행실로 자기를 꾸며야 합니다.

11여자는 일체 순종하며 조용히 배우도록 하십시오.

12나는 여자가 가르치거나 남자를 지배하는 것을 허락하지 않습니다. 다만 여자는 조용히 해야 합니다.

13이것은 아담이 먼저 창조된 다음에 이브가 창조되었으며

14아담이 속은 것이 아니라 여자가 속아서 죄에 빠졌기 때문입니다.

15그러나 만일 여자들이 절제함으로 계속 믿음과 사랑과 거룩함으로 살면 2:15 또는 ‘해산함으로’아이를 낳고 구원을 받을 것입니다.