1 Samueli 8 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 8:1-22

Aisraeli Apempha kuti Akhale ndi Mfumu

1Samueli atakalamba anasankha ana ake kuti akhale oweruza Aisraeli. 2Mwana wake woyamba anali Yoweli, wachiwiri anali Abiya, ndipo ankaweruza ku Beeriseba. 3Koma ana akewo sanatengere makhalidwe ake abwino. Iwo ankapotokera ku zoyipa namatsata phindu mwachinyengo. Ankalandira ziphuphu ndi kumaweruza mwachinyengo.

4Tsono akuluakulu onse a Israeli anasonkhana pamodzi ndipo anabwera kwa Samueli ku Rama. 5Iwo anati kwa iye “Taonani, inu mwakula tsopano ndipo ana anu sakutsata makhalidwe anu abwino. Tsono mutipatse mfumu kuti izitilamulira, monga momwe ikuchitira mitundu ina yonseyi.”

6Koma mawu oti, “Mutipatse mfumu kuti izitilamulira,” sanakondweretse Samueli. Choncho anapemphera kwa Yehova. 7Yehova anamuyankha nati, “Mvera zonse zimene anthuwa akukuwuza. Si ndiwe amene akumukana, koma akukana Ine kuti ndikhale mfumu yawo. 8Kuyambira tsiku limene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mpaka lero zochita zawo zakhala zondikana Ine nʼkumatumikira milungu ina. Tsopano akukukananso iwe. 9Tsono amvere zimene akunena, koma uwachenjeze kwambiri ndipo uwawuzitse za khalidwe la mfumu imene idzawalamulire.”

10Samueli anawawuza anthu amene amamupempha mfumu aja mawu onse a Yehova. 11Iye anati, “Zimene mfumu imene idzakulamulireniyo idzachite ndi izi: Izidzatenga ana anu aamuna kuti akhale ankhondo ake; ena pa magaleta ake, ena pa akavalo ake ndipo ena othamanga patsogolo pa magaleta akewo. 12Ena adzawayika kukhala olamulira asilikali 1,000, ena olamulira asilikali makumi asanu, ndi ena otipula minda yake, ndi kukolola ndiponso ena adzakhala osula zida zankhondo ndi zida za magaleta ake. 13Iyo idzatenga ana anu akazi kuti akhale oyenga mafuta onunkhira, ophika chakudya ndi kupanga buledi. 14Idzatenga minda yanu yabwino ya mpesa ndi ya mitengo ya olivi ndipo adzayipereka kwa antchito ake. 15Idzatenga gawo lakhumi la tirigu wanu ndi mphesa zanu ndi kupereka kwa nduna zake ndi akapitawo ake. 16Mfumuyo idzatenga antchito anu aamuna ndi aakazi. Idzatenganso ngʼombe zanu zabwino ndi abulu anu nʼkumazingwiritsa ntchito. 17Iyo idzatenga gawo lakhumi la zoweta zanu, ndipo inu eni mudzakhala akapolo ake. 18Nthawi imeneyo ikadzafika inu mudzalira momvetsa chisoni chifukwa cha mfumu imene mwadzisankhira, koma Yehova sadzakuyankhani.”

19Koma anthu anakana kumumvera Samueli. Iwo anati, “Ayi! Ife tikufuna mfumu yotilamulira. 20Kotero ifenso tidzakhala ngati mayiko ena. Mfumu yathu idzatiweruza ndiponso idzatuluka nafe kutitsogolera kukamenya nkhondo.”

21Samueli atamva zonse zimene anthuwo ananena, iye anakazifotokozanso kwa Yehova. 22Yehova anamuyankha nati, “Amvere zimene akunena ndipo apatse mfumu.”

Ndipo Samueli anati kwa Aisraeli aja, “Bwererani aliyense kwawo.”

King James Version

1 Samuel 8:1-22

1And it came to pass, when Samuel was old, that he made his sons judges over Israel. 2Now the name of his firstborn was Joel; and the name of his second, Abiah: they were judges in Beer-sheba. 3And his sons walked not in his ways, but turned aside after lucre, and took bribes, and perverted judgment.

4Then all the elders of Israel gathered themselves together, and came to Samuel unto Ramah, 5And said unto him, Behold, thou art old, and thy sons walk not in thy ways: now make us a king to judge us like all the nations.

6¶ But the thing displeased Samuel, when they said, Give us a king to judge us. And Samuel prayed unto the LORD.8.6 displeased: Heb. was evil in the eyes of 7And the LORD said unto Samuel, Hearken unto the voice of the people in all that they say unto thee: for they have not rejected thee, but they have rejected me, that I should not reign over them. 8According to all the works which they have done since the day that I brought them up out of Egypt even unto this day, wherewith they have forsaken me, and served other gods, so do they also unto thee. 9Now therefore hearken unto their voice: howbeit yet protest solemnly unto them, and shew them the manner of the king that shall reign over them.8.9 hearken…: or, obey8.9 howbeit…: or, notwithstanding when thou hast solemnly protested against them then thou shalt

10¶ And Samuel told all the words of the LORD unto the people that asked of him a king. 11And he said, This will be the manner of the king that shall reign over you: He will take your sons, and appoint them for himself, for his chariots, and to be his horsemen; and some shall run before his chariots. 12And he will appoint him captains over thousands, and captains over fifties; and will set them to ear his ground, and to reap his harvest, and to make his instruments of war, and instruments of his chariots. 13And he will take your daughters to be confectionaries, and to be cooks, and to be bakers. 14And he will take your fields, and your vineyards, and your oliveyards, even the best of them, and give them to his servants. 15And he will take the tenth of your seed, and of your vineyards, and give to his officers, and to his servants.8.15 officers: Heb. eunuchs 16And he will take your menservants, and your maidservants, and your goodliest young men, and your asses, and put them to his work. 17He will take the tenth of your sheep: and ye shall be his servants. 18And ye shall cry out in that day because of your king which ye shall have chosen you; and the LORD will not hear you in that day.

19¶ Nevertheless the people refused to obey the voice of Samuel; and they said, Nay; but we will have a king over us; 20That we also may be like all the nations; and that our king may judge us, and go out before us, and fight our battles. 21And Samuel heard all the words of the people, and he rehearsed them in the ears of the LORD. 22And the LORD said to Samuel, Hearken unto their voice, and make them a king. And Samuel said unto the men of Israel, Go ye every man unto his city.