1 Samueli 6 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 6:1-21

Bokosi la Chipangano Libwerera ku Israeli

1Bokosi la Yehova linakhala mʼdziko la Afilisti kwa miyezi isanu ndi iwiri. 2Tsono Afilisti anayitana ansembe ndi amawula ndipo anati, “Tichite nalo chiyani Bokosi la Yehova? Tiwuzeni momwe tidzalitumizira ku malo ake.”

3Iwo anayankha kuti, “Ngati mufuna kubweza Bokosi la Mulungu wa Israeli, musalitumize wopanda kanthu, koma muyesetse kulitumiza pamodzi ndi nsembe yopepesera machimo. Mukatero mudzachiritsidwa, ndipo mudzadziwa chifukwa chiyani chilango cha Yehova sichikukuchokani.”

4Afilisti anafunsanso kuti “Kodi ife tipereke nsembe yanji yopepesera machimo?”

Iwo anayankha kuti, “Mupereke zifanizo zagolide za zithupsa zisanu ndi zamakoswe asanu malingana ndi chiwerengero cha akalonga a Afilisti popeza mliri womwewo wagwera inu ndi akalonga anu. 5Mupange zifanizo za zithupsa zisanu ndi za makoswe asanu amene akuwononga dziko lanu ndipo mupereke ulemu kwa Israeli. Mwina adzaleka kuzunza inu, milungu yanu ndi dziko lanu. 6Nʼchifukwa chiyani mukuwumitsa mitima monga anachita Aigupto ndi Farao? Mulungu atawalanga anthu a ku Igupto aja kodi suja anawalola Aisraeli kuti azipita ndipo anapitadi?

7“Tsopano konzani galeta latsopano limodzi ndiponso ngʼombe ziwiri zazikazi zamkaka zimene sizinavalepo goli. Muzimangirire ngʼombezo ku ngoloyo, koma ana awo muwachotse ndi kuwasiya kwanu. 8Mutenge Bokosi la Yehova ndi kuliyika pa galetapo ndipo pambali pake pakhale Bokosi, mʼmene muyikemonso zinthu zagolide zomwe mukutumiza kwa Iye monga nsembe yopepesera machimo. Kenaka, mulisiye lizipita. 9Koma muziliyangʼana. Ngati lilondola njira yopita kwawo kwa Bokosilo mpaka ku Beti-Semesi ndiye kuti amene watichita zoyipa zazikulu zoterezi ndi Mulungu wa Israeli. Koma ngati silitero, ife tidzadziwa kuti sanali Mulungu wa Israeli amene watizunza koma kuti zinangochitika mwatsoka.”

10Anthu aja anachitadi zimenezi. Anatenga ngʼombe zamkaka ziwiri nazimanga ku galeta lija. Koma ana awo anawatsekera mʼkhola. 11Tsono anayika Bokosi la Yehova pa galeta pamodzi ndi bokosi limene munali makoswe agolide ndi zifanizo zawo za zithupsa. 12Ngʼombe zija zinapita molunjika kutsata msewu wopita ku Beti Semesi zikulira njira yonse. Sizinakhotere kumanja kapena kumanzere. Akalonga a Afilisti anazitsatira mpaka mʼmalire a Beti-Semesi.

13Nthawi imeneyi anthu a ku Beti-Semesi amakolola tirigu mʼchigwa ndipo pamene anayangʼana ndi kuona Bokosi la Chipangano likubwera anakondwa. 14Galeta lija linafika ku munda wa Yoswa ku Beti-Semesi ndipo linayima. Kumeneko kunali mwala waukulu. Tsono anthu anawaza nkhuni galetalo, ndipo anapha ngʼombe zija ndi kuzipereka ngati nsembe zopsereza kwa Yehova. 15Alevi nʼkuti atatsitsa Bokosi la Yehova, pamodzi ndi bokosi mmene munali zinthu zagolide, ndipo anawayika pa mwala uja waukulu. Tsiku limenelo anthu a ku Beti-Semesi anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa Yehova. 16Atsogoleri asanu a Afilisti ataona izi anabwerera ku Ekroni tsiku lomwelo.

17Zifanizo zagolide za zithupsa zimene Afilisti anatumiza ngati nsembe zopepesera machimo kwa Yehova zinkayimirira mizinda isanu iyi motere: chimodzi cha ku Asidodi, china cha ku Gaza ndi zina za ku Asikeloni, Gati ndi Ekroni. 18Ndipo chiwerengero cha zifanizo za makoswe chinali chofanana ndi chiwerengero cha mizinda ya akalonga asanu a Afilisti. Mizindayi inali yotetezedwa bwino ndi ina yapamtetete. Mwala waukulu umene anayikapo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼmunda mwa Yoswa ku Beti-Semesi uli ngati mboni mpaka lero.

19Yehova anakantha amuna a ku Beti-Semesi 70 chifukwa anasuzumira mʼBokosi la Chipangano cha Yehova. Ndipo anzawo analira chifukwa Yehova anawalanga kwambiri. 20Tsono anthu a ku Beti-Semesi anafunsa, “Ndani angathe kuyima pamaso pa Yehova Mulungu Woyera? Bokosi la Chipanganoli lipita kuti likachoka pano?”

21Tsono iwo anatumiza a mithenga kwa anthu a ku Kiriati-Yearimu kuti, “Afilisti atibwezera Bokosi la Yehova. Bwerani kuno mudzalitenge, mupite nalo kwanuko.”

Thai New Contemporary Bible

1ซามูเอล 6:1-21

หีบพันธสัญญากลับสู่อิสราเอล

1หีบพันธสัญญาขององค์พระผู้เป็นเจ้าอยู่ในดินแดนฟีลิสเตียเป็นเวลาเจ็ดเดือน 2ชาวฟีลิสเตียเชิญบรรดาปุโรหิตและโหรของตนมาถามว่า “เราควรทำอย่างไรกับหีบพันธสัญญาขององค์พระผู้เป็นเจ้า? จงบอกเราเถิดว่าเราจะส่งหีบกลับคืนที่เดิมได้อย่างไร?”

3คนเหล่านั้นตอบว่า “ถ้าจะส่งหีบพันธสัญญาของพระเจ้าแห่งอิสราเอลคืน อย่าส่งไปแต่หีบ แต่ต้องส่งคืนไปพร้อมเครื่องบูชาลบความผิดเพื่อถวายแด่พระองค์ด้วย แล้วพวกท่านจะได้หายโรคและท่านจะรู้ว่าทำไมพระองค์ยังลงโทษพวกท่านอยู่”

4ชาวฟีลิสเตียถามว่า “เราจะส่งอะไรไปเป็นเครื่องบูชาลบความผิด?”

พวกเขาตอบว่า “ส่งฝีทองคำห้าลูกและหนูทองคำห้าตัวตามจำนวนเจ้านายทั้งห้า เพราะทั้งท่านและเจ้านายล้วนถูกภัยพิบัติเล่นงาน 5จงทำแบบจำลองฝีและหนูที่มาทำลายบ้านเมืองและถวายเกียรติแด่พระเจ้าแห่งอิสราเอลเถิด บางทีพระองค์อาจจะทรงยั้งพระหัตถ์จากท่านกับบรรดาพระและดินแดนของท่าน 6จะดื้อดึงแข็งขืนอย่างฟาโรห์กับชาวอียิปต์ไปทำไม? เมื่อพระเจ้าทรงจัดการกับพวกเขาอย่างหนัก พวกเขาก็ยอมปล่อยชนอิสราเอลออกมาไม่ใช่หรือ?

7“บัดนี้จงต่อเกวียนเล่มใหม่เทียมด้วยแม่วัวสองตัวที่เพิ่งจะตกลูกและไม่เคยเทียมแอกมาก่อน ส่วนลูกของมันแยกไปขังไว้ที่คอก 8จงวางหีบพันธสัญญาขององค์พระผู้เป็นเจ้าบนเกวียน และบรรจุเครื่องทองคำที่ท่านถวายเป็นเครื่องบูชาลบความผิดไว้ในกล่องข้างๆ แล้วปล่อยแม่วัวไปตามใจของมัน 9แต่จงคอยดูอยู่ หากมันข้ามพรมแดนมุ่งไปยังเบธเชเมช แสดงว่าพระองค์นี่แหละทรงนำภัยพิบัติยิ่งใหญ่นี้มาเหนือเรา แต่หากไม่เป็นเช่นนั้น เราก็จะได้รู้ว่าภัยพิบัตินี้เป็นเพียงเหตุบังเอิญ ไม่ใช่พระองค์ที่ทรงลงโทษเรา”

10พวกเขาจึงทำตามนั้น เขาเทียมแม่วัวสองตัวเข้ากับเกวียน ส่วนลูกของมันแยกไว้ที่คอก 11จากนั้นวางหีบพันธสัญญาขององค์พระผู้เป็นเจ้าและกล่องบรรจุหนูทองคำกับฝีจำลองบนเกวียน 12แม่วัวมุ่งหน้าไปตามถนนตรงไปยังเบธเชเมช เดินพลางร้องพลางตลอดทาง ไม่หันซ้ายหันขวาเลย บรรดาเจ้านายของฟีลิสเตียก็ติดตามไปจนถึงพรมแดนเบธเชเมช

13ชาวเมืองเบธเชเมชกำลังเกี่ยวข้าวสาลีอยู่ในหุบเขา และเมื่อเห็นหีบพันธสัญญาก็ดีใจมาก 14เกวียนแล่นเข้ามาในทุ่งนาของโยชูวาแห่งเบธเชเมช และมาหยุดอยู่ข้างก้อนหินใหญ่ ชาวเมืองจึงผ่าไม้เกวียนทำฟืน แล้วฆ่าแม่วัวถวายเป็นเครื่องเผาบูชาแด่องค์พระผู้เป็นเจ้า 15คนเลวีช่วยกันยกหีบพันธสัญญาขององค์พระผู้เป็นเจ้าและกล่องบรรจุเครื่องทองออกจากเกวียนแล้ววางไว้บนก้อนหินใหญ่นั้น ในวันนั้นชาวเมืองเบธเชเมชพากันนำเครื่องเผาบูชาและเครื่องบูชาอื่นๆ มาถวายแด่องค์พระผู้เป็นเจ้า 16เจ้านายทั้งห้าของฟีลิสเตียมองเห็นเหตุการณ์ทั้งหมดนี้ จากนั้นก็กลับไปเอโครนในวันเดียวกัน

17ฝีทองคำทั้งห้าซึ่งชาวฟีลิสเตียส่งมาเพื่อเป็นเครื่องบูชาลบความผิดถวายแด่องค์พระผู้เป็นเจ้านั้น แต่ละอันสำหรับแต่ละเมืองคือ อัชโดด กาซา อัชเคโลน กัท และเอโครน 18และจำนวนหนูทองคำห้าตัวเท่ากับจำนวนเมืองของเจ้านายฟีลิสเตียทั้งห้า ซึ่งเป็นเมืองป้อมปราการและมีหมู่บ้านโดยรอบ ก้อนหินใหญ่ซึ่ง6:18 สำเนาต้นฉบับภาษาฮีบรูส่วนใหญ่ว่าหมู่บ้านโดยรอบ ไกลไปถึงอาแบลใหญ่ที่ซึ่งพวกเขาวางหีบพันธสัญญาขององค์พระผู้เป็นเจ้านั้นยังคงตั้งอยู่ที่ทุ่งนาของโยชูวาแห่งเบธเชเมชจนถึงทุกวันนี้

19แต่พระเจ้าทรงประหารชาวเมืองเบธเชเมชเจ็ดสิบคน6:19 สำเนาต้นฉบับภาษาฮีบรูส่วนใหญ่และฉบับ LXX. ว่าห้าหมื่นเจ็ดสิบคนซึ่งมองเข้าไปในหีบพันธสัญญาขององค์พระผู้เป็นเจ้าชาวเมืองพากันโศกเศร้าที่องค์พระผู้เป็นเจ้าทรงลงโทษพวกเขาอย่างหนัก 20พวกเขาร้องว่า “ใครหนอจะสามารถยืนอยู่ต่อหน้าพระยาห์เวห์พระเจ้าผู้บริสุทธิ์องค์นี้ได้? เราจะส่งหีบพันธสัญญาไปที่ไหนได้บ้าง?”

21ฉะนั้นเขาจึงส่งผู้สื่อสารไปแจ้งชาวเมืองคีริยาทเยอาริมว่า “ชาวฟีลิสเตียได้ส่งหีบพันธสัญญาขององค์พระผู้เป็นเจ้าคืนมาให้แล้ว โปรดมารับไปไว้ในดินแดนของท่านเถิด”