1 Samueli 31 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 31:1-13

Imfa ya Sauli ndi Ana Ake

1Tsono Afilisti anachitanso nkhondo ndi Aisraeli ndipo Aisraeli anathawa Afilistiwo, kotero kuti ambiri anaphedwa pa phiri la Gilibowa. 2Afilisti anapanikiza kwambiri Sauli ndi ana ake, ndipo anapha Yonatani, Abinadabu ndi Maliki-Suwa. 3Nkhondo inakula kwambiri mozungulira Sauli ndipo pamene anthu amauta anamupeza, anamuvulaza kwambiri.

4Tsono Sauli anawuza mnyamata wake wonyamula zida zake kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuopa kuti anthu osachita mdulidwewa angabwere kudzandizunza ine.”

Koma mnyamata wonyamula zida uja anachita mantha kwambiri ndipo sanathe kutero. Choncho Sauli anatenga lupanga lake lomwe nagwerapo. 5Mnyamata wonyamula zida zake uja ataona kuti Sauli wafa, nayenso anadzigwetsera pa lupanga lake nafa naye limodzi. 6Motero Sauli ndi ana ake atatu, wonyamula zida zake pamodzi ndi anthu ake onse anafera limodzi pa tsikulo.

7Pamene Aisraeli amene anali tsidya lina la chigwa ndi amene anali tsidya la chigwa cha Yorodani anaona kuti gulu la ankhondo la Aisraeli lathawa komanso kuti Sauli ndi ana ake aphedwa, nawonso anathawa kusiya mizinda yawo. Ndipo Afilisti anabwera kudzakhalamo.

8Mmawa mwake, Afilisti atabwera kudzatenga zinthu za anthu ophedwa anapeza Sauli ndi ana ake atatu atafa pa phiri la Gilibowa. 9Iwo anadula mutu wake ndi kumuvula zida zake zankhondo. Ndipo anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Afilisti kukafalitsa nkhani yabwinoyi kwa mafano awo ndi kwa anthu awo. 10Iwo anayika zida zake zankhondo mʼnyumba yopembedzera Asitoreti, ndipo thupi lake analikhomera pa khoma la mzinda wa Beti-Sani.

11Pamene anthu a ku Yabesi Giliyadi anamva zimene Afilisti anachitira Sauli, 12anthu awo onse olimba mtima anayenda usiku wonse kupita ku Beti-Sani. Anakachotsa mtembo wa Sauli ndi mitembo ya ana ake pa khoma la mzinda wa Beti-Sani, ndipo anabwera nayo ku Yabesi kumene anayitentha ndi moto. 13Pambuyo pake anatenga mafupa awo ndi kuwakwirira pansi pa mtengo wabwemba ku Yabesi, ndipo anasala kudya masiku asanu ndi awiri.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

1 Царств 31:1-13

Гибель Шаула и его сыновей

(1 Лет. 10:1-12)

1Филистимляне воевали с Исраилом, и исраильтяне бежали от них и падали сражёнными на горе Гильбоа. 2Филистимляне нагнали Шаула и его сыновей и убили Ионафана, Авинадава и Малик-Шуа. 3Вокруг Шаула разгорелась жестокая битва. Лучники нашли его и тяжело ранили.

4Шаул сказал своему оруженосцу:

– Обнажи свой меч и заколи меня, иначе эти необрезанные придут, заколют меня и станут глумиться надо мной.

Но оруженосец не решился сделать это, потому что очень испугался. Тогда Шаул взял свой собственный меч и бросился на него. 5Когда оруженосец увидел, что Шаул мёртв, он тоже бросился на свой меч и умер вместе с ним. 6Так Шаул, три его сына, оруженосец и все его люди погибли в тот день.

7Увидев, что исраильское войско разбежалось, а Шаул и его сыновья погибли, исраильтяне, которые жили на другой стороне долины и за Иорданом, оставили свои города и тоже бежали. А филистимляне пришли и заняли их.

8На следующий день, когда филистимляне пришли грабить мёртвых, они нашли Шаула и трёх его сыновей, павших на горе Гильбоа. 9Они отсекли ему голову, сняли с него оружие и послали вестников по всей филистимской земле, чтобы возвестить об этом в капище своих идолов и народу. 10Они положили его оружие в храме Астарты и повесили его тело на стене Бет-Шеана.

11Когда жители Иавеша Галаадского услышали о том, что филистимляне сделали с Шаулом, 12то все их храбрые воины отправились в путь, шли всю ночь и, придя в Бет-Шеан, сняли тела Шаула и его сыновей со стены. Они пришли в Иавеш и сожгли их там. 13Потом они взяли их кости, похоронили под тамариском в Иавеше и постились семь дней.