1 Samueli 24 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 24:1-22

Davide Amusiya Sauli Wosamupha

1Sauli atabwera kuchokera kumene amathamangitsa Afilisti anamva kuti, “Davide ali mʼchipululu cha Eni Gedi.” 2Tsono Sauli anatenga asilikali 3,000 odziwa kumenya bwino nkhondo kuchokera pakati pa Aisraeli onse ndipo anapita kukafunafuna Davide ndi anthu ake ku Matanthwe a Mbalale.

3Iye anafika ku makola a nkhosa amene anali mʼmbali mwa njira. Kumeneko kunali phanga, ndipo Sauli analowa mʼphangamo kuti akadzithandize. Davide ndi anthu ake ankabisala mʼkati mwenimweni mwa phangalo. 4Tsono anthu a Davide anamuwuza kuti, “Tsiku lija lafika limene Yehova anakuwuzani kuti, ‘Ndidzapereka mdani wanu mʼmanja mwanu, ndi kumuchita chimene chidzakukomereni.’ ” Koma Davide anapita mwakachetechete ndi kukadula msonga ya mkanjo wa Sauli.

5Atachita izi, Davide anatsutsika mu mtima chifukwa anadula msonga ya mkanjo wa Sauli. 6Tsono anawuza anthu ake kuti, “Yehova asalole kuti ndimuchite choyipa mbuye wanga, wodzozedwa wa Yehova. Ndisamupweteke pakuti ndi wodzozedwa wa Yehova.” 7Choncho Davide anabweza mitima ya anthu ake ndi mawu amenewa, ndipo sanawalole kuti aphe Sauli. Pambuyo pake Sauli anatuluka mʼphangamo ndipo anachoka.

8Kenaka Davide anatuluka mʼphanga muja ndipo anayitana Sauli, “Mbuye wanga!” Sauli atayangʼana mʼmbuyo, Davide anawerama ndi kugunditsa nkhope yake pansi. 9Anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumamvera mawu a anthu kuti, ‘Davide wakukonzerani chiwembu?’ 10Lero lino inu mwadzionera nokha kuti Yehova anakuperekani mʼmanja mwanga mʼphanga muja. Ena anandiwuza kuti ndikupheni, koma ndakusiyani. Ndinati, ‘Sindidzapha mbuye wanga pakuti ndiye wodzozedwa wa Yehova.’ 11Tsono abambo anga, onanitu kansalu ka mkanjo wanu kali mʼdzanja langali! Popeza kuti ndinatha kudula msonga ya mkanjo wanu koma osakuphani, pamenepo mudziwe kuti ine ndilibe maganizo woti ndikuchiteni choyipa kapena kukuwukirani. Sindinakulakwireni ngakhale kuti inu mukufuna moyo wanga kuti mundiphe. 12Yehova aweruze pakati pa inu ndi ine, akulangeni chifukwa cha zoyipa zimene mukundichitazi, koma dzanja langa silidzakukhudzani. 13Paja anthu akale anati, ‘Munthu woyipa, ntchito zakenso ndi zoyipa.’ Kotero dzanja langa silidzakukhudzani.

14“Kodi mfumu ya Israeli yadzalondola yani. Inu mukuthamangitsa yani? Galu wakufa kodi? Nsabwe kodi? 15Nʼchifukwa chake Yehova agamule, inde aweruze pakati pa inu ndi ine ndi kupeza wolakwa. Yehova anditeteze ndi kundipulumutsa mʼdzanja lanu.”

16Davide atatsiriza kuyankhula mawu awa, Sauli anafunsa kuti, “Kodi mawu amenewa ndi akodi mwana wanga Davide?” Sauli anayamba kulira mokweza. 17Anawuza Davide kuti, “Ndiwe wolungama kuposa ine. Iwe wandikomera mtima pamene ine ndakuchitira zoyipa. 18Iweyo lero lino wandifotokozera zabwino zimene wandichitira. Yehova anandipereka mʼdzanja lako koma iwe sunandiphe. 19Kodi munthu atapeza mdani wake angamulole kuti apite wosamuvulaza? Motero Yehova akuchitire iwe zabwino chifukwa cha zimene wandichitira lerozi. 20Ona tsono, Ine ndikudziwa kuti udzakhala mfumu ndithu ndipo ufumu wa Israeli udzakhazikika mʼmanja mwako. 21Tsopano undilonjeze molumbira lero mʼdzina la Yehova kuti sudzapha zidzukulu zanga ine nditamwalira kapena kufuta dzina langa pa banja la makolo anga.”

22Choncho Davide analumbira pamaso pa Sauli. Pambuyo pake Sauli anabwerera kwawo, koma Davide ndi anthu ake anapitanso ku phanga kuja.

New International Reader’s Version

1 Samuel 24:1-22

David Doesn’t Kill Saul When He Has the Chance

1Saul returned from chasing the Philistines. Then he was told, “David is in the Desert of En Gedi.” 2So Saul took 3,000 of the best soldiers from the whole nation of Israel. He started out to look for David and his men. He planned to look near the Rocky Cliffs of the Wild Goats.

3He came to some sheep pens along the way. A cave was there. Saul went in to go to the toilet. David and his men were far back in the cave. 4David’s men said, “This is the day the Lord told you about. He said to you, ‘I will hand your enemy over to you. Then you can deal with him as you want to.’ ” So David came up close to Saul without being seen. He cut off a corner of Saul’s robe.

5Later, David felt sorry that he had cut off a corner of Saul’s robe. 6He said to his men, “May the Lord keep me from doing a thing like that again to my master. He is the Lord’s anointed king. So I promise that I will never lay my hand on him. The Lord has anointed him.” 7David said that to correct his men. He wanted them to know that they should never suggest harming the king. He didn’t allow them to attack Saul. So Saul left the cave and went on his way.

8Then David went out of the cave. He called out to Saul, “King Saul! My master!” When Saul looked behind him, David bowed down. He lay down flat with his face toward the ground. 9He said to Saul, “Why do you listen when men say, ‘David is trying to harm you’? 10This day you have seen with your own eyes how the Lord handed you over to me in the cave. Some of my men begged me to kill you. But I didn’t. I said, ‘I will never lay my hand on my master. He is the Lord’s anointed king.’ 11Look, my father! Look at this piece of your robe in my hand! I cut off the corner of your robe. But I didn’t kill you. See, there is nothing in my hand that shows I am guilty of doing anything wrong. I haven’t turned against you. I haven’t done anything to harm you. But you are hunting me down. You want to kill me. 12May the Lord judge between you and me. And may the Lord pay you back because of the wrong things you have done to me. But I won’t do anything to hurt you. 13People say, ‘Evil acts come from those who do evil.’ So I won’t do anything to hurt you.

14“King Saul, who are you trying to catch? Who do you think you are chasing? I’m nothing but a dead dog or a flea! 15May the Lord be our judge. May he decide between us. May he consider my case and stand up for me. May he show that I’m not guilty of doing anything wrong. May he save me from you.”

16When David finished speaking, Saul asked him a question. He said, “My son David, is that your voice?” And Saul wept out loud. 17“You are a better person than I am,” he said. “You have treated me well. But I’ve treated you badly. 18You have just now told me about the good things you did to me. The Lord handed me over to you. But you didn’t kill me. 19Suppose a man finds his enemy. He doesn’t let him get away without harming him. May the Lord reward you with many good things. May he do it because of the way you treated me today. 20I know for sure that you will be king. I know that the kingdom of Israel will be made secure under your control. 21Now make a promise in the name of the Lord. Promise me that you won’t kill the children of my family. Also promise me that you won’t wipe out my name from my family line.”

22So David made that promise to Saul. Then Saul returned home. But David and his men went up to his usual place of safety.