1 Mbiri 26 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 26:1-32

Alonda a pa Zipata

1Magulu a alonda a pa zipata:

Kuchokera ku banja la Kora: Meselemiya mwana wa Kore, mmodzi mwa ana a Asafu.

2Meselemiya anali ndi ana awa:

woyamba Zekariya,

wachiwiri Yediaeli,

wachitatu Zebadiya,

wachinayi Yatinieli,

3wachisanu Elamu,

wachisanu ndi chimodzi Yehohanani,

ndipo wachisanu ndi chiwiri Elihunai.

4Obedi-Edomu analinso ndi ana awa:

woyamba Semaya,

wachiwiri Yehozabadi,

wachitatu Yowa,

wachinayi Sakara,

wachisanu Netaneli,

5wachisanu ndi chimodzi Amieli,

wachisanu ndi chiwiri Isakara

ndipo wachisanu ndi chitatu Peuletayi.

(Pakuti Mulungu anadalitsa Obedi-Edomu).

6Mwana wake Semaya analinso ndi ana amene anali atsogoleri mʼbanja la abambo awo chifukwa anali anthu amphamvu. 7Ana a Semaya anali: Otini, Refaeli, Obedi ndi Elizabadi; abale ake, Elihu ndi Semakiya, analinso anthu amphamvu. 8Onsewa anali adzukulu a Obedi-Edomu. Iwo ndi ana awo ndiponso abale awo anali anthu aluso ndi amphamvu pogwira ntchito. Zidzukulu zonse za Obedi-Edomu zinalipo 62.

9Meselemiya anali ndi ana ndi abale ake amene anali aluso ndipo onse analipo 18.

10Hosa Mmerari anali ndi ana awa: woyamba anali Simiri (ngakhale kuti iye sanali woyamba kubadwa, abambo ake anamusankha kuti akhale mtsogoleri), 11wachiwiri Hilikiya, wachitatu Tebaliya ndipo wachinayi Zekariya. Ana ndi abale onse a Hosa analipo 13.

12Magulu amenewa a alonda a pa zipata, motsogozedwa ndi atsogoleri awo, anali ndi ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova, monga momwe amachitira abale awo. 13Iwo anachita maere mwa mabanja awo aangʼono ndi aakulu omwe kuti apeze mlonda pa chipata chilichonse.

14Maere a chipata chakummwa anagwera Selemiya. Maere anachitikanso chifukwa cha mwana wake Zekariya, phungu wanzeru ndipo maere a chipata chakumpoto anagwera iye. 15Maere a chipata chakummwera anagwera Obedi-Edomu, ndipo maere a nyumba yosungiramo katundu anagwera ana ake. 16Maere a chipata chakumadzulo ndi chipata cha Saleketi ku msewu wa ku mtunda anagwera Supimu ndi Hosa.

Mlonda ankayangʼanana ndi mlonda mnzake: 17Mbali ya kummawa kunkakhala Alevi 6 pa tsiku, kumpoto anayi pa tsiku, kummwera anayi pa tsiku ndipo awiri ankakhala pa nyumba yosungiramo katundu. 18Ndipo ku bwalo cha kumadzulo, anayi amakhala mu msewu ndi awiri pabwalo penipeni.

19Awa anali magulu a alonda a pa zipata amene anali zidzukulu za Kora ndi Merari.

Asungichuma ndi Akuluakulu Ena

20Abale awo Alevi, motsogozedwa ndi Ahiya, anali oyangʼanira chuma cha nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Mulungu.

21Adzukulu a Ladani, mmodzi mwa ana a Geresoni, amene anali atsogoleri a mabanja a Ageresoni, anali awa: Yehieli, 22ana a Yehieli, Zetamu ndi mʼbale wake Yoweli. Iwo amayangʼanira chuma cha ku Nyumba ya Mulungu wa Yehova.

23Kuchokera ku banja la Amramu, banja la Aizihara, banja la Ahebroni ndi banja la Auzieli:

24Subaeli, chidzukulu cha Geresomu, mwana wa Mose, anali mkulu woyangʼanira chuma. 25Abale ake obadwa mwa Eliezara, anali Rekabiya mwana wake, Yesaya mwana wake, Yoramu mwana wake, Zikiri mwana wake ndi Selomiti mwana wake. 26Selomiti ndi abale ake amayangʼanira zinthu zonse zoperekedwa kwa Mulungu ndi mfumu Davide, atsogoleri a mabanja amene anali olamulira ankhondo 1,000, olamulira ankhondo 100, ndi olamulira ankhondo ena. 27Zina zofunkha ku nkhondo anazipereka kuti zikhale zokonzera Nyumba ya Yehova. 28Ndipo zonse zimene zinaperekedwa ndi Mlosi Samueli, Sauli mwana wa Kisi, Abineri mwana wa Neri ndiponso Yowabu mwana wa Zeruya ndi zinthu zonse zimene zinkaperekedwa zimasungidwa ndi Selomiti ndi abale ake.

29Kuchokera ku banja la Izihari: Kenaniya ndi ana ake anapatsidwa ntchito kutali ndi Nyumba ya Mulungu ngati akuluakulu ndi oweruza Israeli.

30Kuchokera ku banja la Ahebroni: Hasabiya ndi abale ake, anthu anzeru 1,700. Iwo ankayangʼanira ntchito zonse za Yehova ndi ntchito yonse ya mfumu cha kumadzulo kwa Yorodani. 31Pa banja la Ahebroni, Yeriya anali mtsogoleri monga mwa mbiri ya mibado ya mabanja awo. Mʼchaka cha 40 cha ufumu wa Davide, panachitika kafukufuku ndipo ena mwa anthu aluso a banja la Hebroni anapezeka kuti anali ku Yazeri ku Giliyadi. 32Yeriya anali ndi abale 2,700 amene anali aluso ndiponso atsogoleri a mabanja. Mfumu Davide anawayika iwowa kuti aziyangʼanira fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase pa zinthu zonse za Mulungu ndi za mfumu.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

1 Летопись 26:1-32

Распределение привратников

1Вот распределение привратников:

из корахитов: Мешелемия, сын Коре, один из сыновей Асафа.

2У Мешелемии были сыновья:

первенец Закария,

второй сын – Иедиаил,

третий – Зевадия,

четвёртый – Иатниил,

3пятый – Елам,

шестой – Иоханан

и седьмой – Элиегоенай.

4У Овид-Эдома тоже были сыновья:

первенец Шемая,

второй сын – Иехозавад,

третий – Иоах,

четвёртый – Сахар,

пятый – Нетанил,

5шестой – Аммиил,

седьмой – Иссахар

и восьмой – Пеуллетай.

(Так Аллах благословил Овид-Эдома.)

6У Шемаи, сына Овид-Эдома, тоже родились сыновья, которые были вождями своего клана, потому что были очень способными людьми. 7Сыновья Шемаи: Отни, Рефаил, Овид и Элзавад; его родственники Элиху и Семахия тоже были очень способными людьми. 8Все они были потомками Овид-Эдома. Они сами, их сыновья и родственники были очень способными людьми, прилежными в работе. Всего их было у Овид-Эдома шестьдесят два человека.

9У Мешелемии было восемнадцать сыновей и родственников, которые также были способными людьми.

10У мераритянина Хосы были сыновья: первый Шимри (хотя он и не был первенцем, его отец сделал его главным), 11второй – Хилкия, третий – Тевалия и четвёртый – Закария. Сыновей и родственников Хосы было тринадцать человек.

12Эти привратники через своих начальников имели обязанности в служении в храме Вечного, как и их родственники. 13Они бросали жребии по своим кланам на каждые ворота – молодой наравне со старым.

14Восточные ворота выпали по жребию Мешелемии. Затем был брошен жребий для его сына Закарии, мудрого советчика, и ему выпали Северные ворота. 15Южные ворота выпали по жребию Овид-Эдому, а кладовые – его сыновьям. 16Западные ворота и ворота Шаллехет на верхней дороге выпали по жребию Шуппиму и Хосе. Одна стража стояла напротив другой: 17шестеро левитов каждый день стояли на восточной стороне, четверо на северной, четверо на южной и по двое у кладовых. 18Что же до западной колоннады, то четверо стояли там у дороги и двое – внутри самой колоннады.

19Так были распределены привратники, потомки Кораха и Мерари.

Распределение хранителей сокровищницы

20Их собратьям-левитам26:20 Или: «Что до левитов, Ахии были вверены…» были вверены сокровищницы дома Аллаха и сокровищницы для посвящённых вещей.

21Потомки Ливни26:21 Букв.: «Ладан» – другое имя Ливни (см. 6:17)., которые были гершонитами по линии Ливни и главами семейств, происходивших от гершонита Ливни: Иехиил. 22Сыновья Иехиила: Зетам и его брат Иоиль. Им были вверены сокровищницы храма Вечного.

23Из амрамитов, ицхаритов, хевронитов и узиилитов:

24Шевуил, потомок сына Мусы Гершома, был главным смотрителем за сокровищницами. 25Его родственники через Элиезера: сын Элиезера Рехавия, отец Иешаи, отца Иорама, отца Зихри, отца Шеломота. 26Шеломоту и его родственникам были вверены все сокровищницы для вещей, посвящённых Вечному царём Давудом, главами семейств, которые были тысячниками, сотниками и военачальниками. 27Часть добычи, взятой в сражении, они посвящали на поддержание храма Вечного. 28Всё, что было посвящено провидцем Шемуилом, царём Шаулом, сыном Киша, начальником войска Шаула Авнером, сыном Нера, и начальником войска Давуда Иоавом, сыном Церуи, и все прочие посвящённые вещи были доверены Шеломоту и его родственникам.

Прочие распределения

29Хенании из рода ицхаритов и его сыновьям были определены обязанности за пределами храма – они были сановниками и судьями над Исраилом.

30Хашавия из рода хевронитов и его родственники – тысяча семьсот способных людей – отвечали в Исраиле, к западу от Иордана, за всю работу в служении Вечному и на царской службе. 31Вождём у хевронитов был Иерия. (В сороковой год правления Давуда родословные записи хевронитян были исследованы и в Иазере Галаадском нашлись очень способные люди из хевронитян.) 32У Иерии было две тысячи семьсот сородичей, очень способных людей, глав семейств, и царь Давуд поставил их над родами Рувима, Гада и половиной рода Манассы во всяком деле Аллаха и во всех делах царя.