1 Mbiri 22 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 22:1-19

1Ndipo Davide anati, “Nyumba ya Yehova Mulungu idzakhala pano, ndiponso guwa lansembe zopsereza za Israeli.”

Kukonzekera Kumanga Nyumba ya Mulungu

2Choncho Davide analamula kuti asonkhanitse alendo onse amene amakhala mu Israeli ndipo kuchokera pakati pawo anasankha amisiri a miyala kuti aseme miyala yomangira nyumba ya Mulungu. 3Ndipo anapereka zitsulo zambiri zopangira misomali ya zitseko za pa zipata ndi zolumikiza zake. Anaperekanso mkuwa wochuluka wokanika kuwuyeza. 4Iye anaperekanso mitengo yambiri ya mkungudza, yosawerengeka, pakuti anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo anabweretsa yambiri kwa Davide.

5Davide anati, “Mwana wanga Solomoni ndi wamngʼono ndipo sadziwa zambiri. Koma nyumba yomwe timangire Yehova iyenera kukhala yaulemerero, yotchuka ndi yokongola pamaso pa anthu a mitundu yonse. Choncho ndikonzekeratu zambiri.” Motero Davide anayikonzekera kwambiri asanamwalire.

6Tsono iye anayitana Solomoni mwana wake ndipo anamulamula kuti adzamangire nyumba Yehova Mulungu wa Israeli. 7Davide anati kwa Solomoni, “Mwana wanga, ine ndinali ndi maganizo oti ndimangire nyumba Dzina la Yehova Mulungu wanga. 8Koma Yehova anandiyankhula kuti, ‘Iwe wapha anthu ambiri ndiponso wachita nkhondo zambiri. Sumangira dzina langa nyumba chifukwa wapha anthu ambiri pa dziko lapansi pamaso panga. 9Koma udzabala mwana wamwamuna amene adzakhala munthu wamtendere ndi wabata ndipo ndidzamupatsa mpumulo kuchokera kwa adani ake onse a mbali zonse. Dzina lake adzatchedwa Solomoni ndipo Ine ndidzapereka mtendere ndi bata kwa Israeli pa nthawi ya ulamuliro wake. 10Iye ndiye adzandimangire nyumba. Adzakhala mwana wanga ndipo Ine ndidzakhala abambo ake. Ndipo ndidzakhazikitsa mpando wake waufumu mʼdziko la Israeli mpaka muyaya.’ ”

11“Tsopano mwana wanga, Yehova akhale nawe ndipo upambane ndi kumanga Nyumba ya Yehova Mulungu wako, monga momwe Iye ananenera kuti udzatero. 12Yehova akupatse nzeru ndi kumvetsetsa pamene Iye adzakuyika kukhala wolamulira Israeli, kuti udzasunge malamulo a Yehova Mulungu wako. 13Ndipo udzapambana ngati udzamvera mosamala malangizo ndi malamulo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kudzera mwa Mose. Khala wamphamvu ndi wolimba mtima. Usachite mantha kapena kutaya mtima.

14“Ine movutikira kwambiri ndapereka ku Nyumba ya Mulungu matani 3,400 agolide, matani 34,000 asiliva, ndiponso mkuwa ndi chitsulo, matabwa ndi miyala. Ndipo iwe utha kuwonjezerapo pa zimenezi. 15Iwe uli ndi antchito ambiri: osema miyala, amisiri a miyala, ndi amisiri a matabwa, komanso anthu ambiri aluso la ntchito zosiyanasiyana, 16zagolide ndi zasiliva, zamkuwa, zazitsulo, amisiri osawerengeka. Tsopano yamba ntchito, ndipo Yehova akhale nawe.”

17Tsono Davide analamula atsogoleri onse a Israeli kuti athandize Solomoni mwana wake. 18Iye anawawuza kuti, “Kodi Yehova Mulungu, sali nanu? Ndipo Iye siwakupatsani mpumulo mbali zonse? Pakuti Iyeyo wapereka eni nthaka kwa inu ndipo dziko lili pa ulamuliro wa Yehova ndi anthu ake. 19Tsono perekani mtima wanu ndi moyo wanu kufunafuna Yehova Mulungu wanu. Yambani kumanga malo opatulika a Yehova Mulungu, kuti mubweretse Bokosi la Chipangano la Yehova ndi zinthu zopatulika za Mulungu mʼNyumba ya Mulungu imene idzamangidwa chifukwa cha dzina la Yehova.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

1 Летопись 22:1-19

1И Давуд сказал:

– Здесь будет дом Вечного Бога и жертвенник для всесожжений Исраила.

Подготовка к строительству храма

2Давуд приказал собрать всех живущих в Исраиле чужеземцев и назначил из них каменотёсов, чтобы они тесали камень для строительства храма Аллаха. 3Он заготовил много железа, чтобы делать гвозди для дверей в воротах и скобы, и бронзы больше, чем можно было взвесить. 4Ещё он заготовил столько кедровых брёвен, что их невозможно было пересчитать, ведь сидоняне и тиряне поставили их Давуду в избытке. 5Давуд сказал:

– Мой сын Сулейман ещё молод и неопытен, а дом, который следует построить Вечному, должен быть великолепен, славен и знаменит во всех землях. Поэтому я приготовлю для него всё необходимое.

И до своей смерти Давуд успел заготовить для храма много строительного материала. 6Он призвал своего сына Сулеймана и повелел ему построить дом для Вечного, Бога Исраила. 7Давуд сказал Сулейману:

– Сын, я думал построить дом для поклонения Вечному, моему Богу, 8но ко мне было слово Вечного: «Ты пролил много крови и вёл большие войны. Ты не построишь дом для поклонения Мне, потому что ты пролил предо Мной на землю много крови. 9Но у тебя родится сын, который будет мирным человеком, и Я дам ему покой от всех окружающих его врагов. Поэтому его будут звать Сулейман («мир»), и в дни его царствования Я дам Исраилу мир и спокойствие. 10Он и построит дом для поклонения Мне. Он будет Мне сыном, а Я буду ему Отцом. Я упрочу престол его царства над Исраилом навеки».

11Итак, сын, пусть Вечный будет с тобой, чтобы тебе сопутствовал успех и ты построил дом Вечному, твоему Богу, как Он и говорил о тебе. 12Пусть Вечный даст тебе разум и понимание, когда Он поставит тебя властвовать над Исраилом, чтобы тебе соблюдать Закон Вечного, твоего Бога. 13Тебе будет сопутствовать успех, если ты будешь внимателен к тому, чтобы исполнять установления и законы, которые Вечный дал Мусе для Исраила. Будь твёрд и мужествен. Не бойся, не падай духом.

14Я приложил много труда, заготовив для дома Вечного три тысячи шестьсот тонн золота и тридцать шесть тысяч тонн22:14 Букв.: «сто тысяч… миллион талантов». серебра, а бронзы и железа больше, чем можно взвесить, а также дерево и камень. Ты же прибавь к этому ещё. 15У тебя много мастеров: каменотёсов, каменщиков и плотников, а также людей, искусных в работе 16с золотом и серебром, бронзой и железом, – ремесленников без счёта. Итак, начинай работу, и пусть Вечный будет с тобой.

17Давуд велел всем старейшинам Исраила помогать его сыну Сулейману. 18Он сказал им:

– Разве Вечный, ваш Бог, не с вами? Разве Он не даровал вам покой со всех сторон? Ведь Он отдал мне обитателей этой земли, и земля подвластна Вечному и Его народу. 19Посвятите же свой разум и сердце тому, чтобы искать Вечного, вашего Бога; начните строить святилище Вечному Богу, чтобы вы могли внести сундук соглашения с Вечным и все остальные священные предметы в храм, который будет выстроен для поклонения Вечному.