1 Mbiri 12 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 12:1-40

Ankhondo Amene Anali ndi Davide, Sauli Asanafe

1Nawa anthu amene anabwera kwa Davide ali ku Zikilagi pamene iye anathamangitsidwa ndi Sauli mwana wa Kisi (iwowo anali mʼgulu la asilikali amene ankamuthandiza pa nkhondo. 2Iwo anali ndi mauta ndipo amadziwa kuponya mivi komanso miyala, ndipo amatha kuponyera dzanja lamanja kapena lamanzere. Iwo anali abale ake a Sauli ochokera ku fuko la Benjamini.

3Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri ndi Yowasi ana a Semaya wa ku Gibeya; Yezieli ndi Peleti ana a Azimaveti; Beraka, Yehu wa ku Anatoti, 4ndi Isimaiya wa ku Gibiyoni, munthu wamphamvu mʼgulu la anthu makumi atatu aja, yemwenso anali mtsogoleri wawo; Yeremiya, Yahazieli, Yohanani, Yozabadi wa ku Gederi, 5Eluzai, Yerimoti, Bealiya, Semariya ndi Sefatiya Mharufi; 6Elikana, Isiya, Azareli, Yowezeri ndi Yasobeamu a ku banja la Kora; 7ndi Yowela ndi Zebadiya ana a Yerohamu wa ku Gedori.

8Asilikali ena a fuko la Gadi anathawira kwa Davide ku linga lake ku chipululu. Iwo anali asilikali olimba mtima, okonzekera nkhondo ndipo amadziwa kugwiritsa ntchito chishango ndi mkondo. Iwowo anali woopsa ngati mikango ndipo anali aliwiro ngati ngoma zamʼmapiri.

9Mtsogoleri wawo anali Ezeri,

wotsatana naye anali Obadiya, wachitatu anali Eliabu,

10wachinayi anali Misimana, Yeremiya anali wachisanu,

11wachisanu ndi chimodzi anali Atai, Elieli anali wachisanu ndi chiwiri,

12wachisanu ndi chitatu anali Yohanani, Elizabadi anali wachisanu ndi chinayi,

13wakhumi anali Yeremiya ndipo Makibanai anali wa 11.

14Anthu a fuko la Gadi amenewa anali atsogoleri; angʼonoangʼono amalamulira anthu 100 pamene akuluakulu amalamulira anthu 1,000. 15Awa ndi amene anawoloka Yorodani mwezi woyamba pamene mtsinje unali utasefukira mbali zonse, ndipo anathamangitsa aliyense amene amakhala mʼchigwa, mbali ya kumadzulo ndi kummawa.

16Anthu ena a fuko la Benjamini ndi ena ochokera ku Yuda anabweranso kwa Davide pamene anali ku linga lake. 17Davide anapita kukakumana nawo ndipo anati, “Ngati mwabwera kwa ine mwamtendere, kuti mundithandize, ndakonzeka kugwirizana nanu. Koma ngati mwabwera kudzandipereka kwa adani anga, ngakhale kuti sindinalakwe, Mulungu wa makolo anthu aone izi ndipo akuweruzeni.”

18Kenaka Mzimu anabwera pa Amasai, mtsogoleri wa anthu makumi atatu aja ndipo anati:

“Inu Davide, ife ndife anu!

Tili nanu limodzi, inu mwana wa Yese!

Kupambana, Kupambana kwa inu,

ndiponso kupambana kukhale kwa iwo amene akukuthandizani

pakuti Mulungu wanu adzakuthandizani.”

Kotero Davide anawalandira ndipo anawayika kukhala atsogoleri a magulu ake a ankhondo.

19Anthu ena a fuko la Manase anathawira kwa Davide pamene anapita ndi Afilisti kukamenyana ndi Sauli. (Iye ndi anthu ake sanathandize Afilisti chifukwa, atsogoleri awo atakambirana, anamubweza Davide. Iwo anati, “Ife tidzawonongedwa ngati uyu adzabwerera kwa mbuye wake Sauli).” 20Davide atapita ku Zikilagi, anthu a fuko la Manase amene anathawira kwa iye anali awa: Adina, Yozabadi, Yediaeli, Mikayeli, Yozabadi, Elihu ndi Ziletai; atsogoleri a magulu a anthu 1,000 a ku Manase. 21Iwowa anathandiza Davide kulimbana ndi magulu achifwamba, pakuti onsewa anali asilikali olimba mtima ndipo anali atsogoleri mʼgulu lake la ankhondo. 22Tsiku ndi tsiku anthu amabwera kudzathandiza Davide, mpaka anakhala ndi gulu lalikulu la ankhondo, ngati gulu la ankhondo a Mulungu.

Enanso Abwera kwa Davide ku Hebroni

23Nachi chiwerengero cha magulu a anthu ankhondo amene anabwera kwa Davide ku Hebroni kudzapereka ufumu wa Sauli kwa iye, monga momwe ananenera Yehova:

24Anthu a fuko la Yuda onyamula chishango ndi mkondo analipo 6,800;

25Anthu a fuko la Simeoni, asilikali okonzekera nkhondo analipo 7,100;

26Anthu a fuko la Levi analipo 4,600, 27mtsogoleri Yehoyada wa banja la Aaroni anabweranso ndi anthu 3,700, 28ndi Zadoki, mnyamata wankhondo wolimba mtima, anabwera ndi akuluakulu 22 ochokera mʼbanja lake;

29Anthu a fuko la Benjamini, abale ake a Sauli analipo 3,000 ndipo ambiri anali ndi Sauli ku nyumba yake pa nthawiyi;

30Anthu a fuko la Efereimu, asilikali olimba mtima, otchuka pa mabanja awo analipo 20,800;

31Anthu a fuko latheka la Manase amene anawayitana kuti adzakhazikitse nawo ufumu wa Davide analipo 18,000;

32Anthu a fuko la Isakara amene ankazindikira nthawi ndipo amadziwa zimene Israeli ankayenera kuchita, analipo atsogoleri 200 pamodzi ndi abale awo onse amene amawatsogolera.

33Anthu a fuko la Zebuloni, analipo 5,000. Iwowa anali asilikali odziwa bwino nkhondo, okhala ndi zida za mtundu uliwonse, okonzekera kudzathandiza Davide ndi mtima umodzi.

34Anthu a fuko la Nafutali, analipo atsogoleri 1,000 pamodzi ndi anthu 37,000 onyamula zishango ndi mikondo;

35Anthu a fuko la Dani, okonzekera nkhondo analipo 28,600.

36Anthu a fuko la Aseri, asilikali odziwa bwino nkhondo, okonzekeradi nkhondo analipo 40,000;

37Ndipo kuchokera kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase, amene anali ndi zida za mtundu uliwonse analipo 120,000.

38Onsewa anali anthu odziwa kumenya nkhondo amene anadzipereka ku magulu awo. Iwo anabwera ku Hebroni ali otsimikiza kudzamuyika Davide kukhala mfumu ya Aisraeli. Aisraeli ena onse anali ndi mtima umodzinso womuyika Davide kukhala mfumu. 39Anthuwa anakhala ndi Davide masiku atatu akudya ndi kumwa pakuti mabanja awo anawapatsa zakudya. 40Komanso anthu oyandikana nawo ochokera ku Isakara, Zebuloni ndi Nafutali anabweretsa zakudya pa abulu, ngamira, nyulu ndi ngʼombe. Panali ufa wambiri, makeke ankhuyu, ntchintchi za mphesa, vinyo, mafuta, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi, popeza munali chimwemwe mu Israeli.

King James Version

1 Chronicles 12:1-40

1Now these are they that came to David to Ziklag, while he yet kept himself close because of Saul the son of Kish: and they were among the mighty men, helpers of the war.12.1 while…: Heb. being yet shut up 2They were armed with bows, and could use both the right hand and the left in hurling stones and shooting arrows out of a bow, even of Saul’s brethren of Benjamin. 3The chief was Ahiezer, then Joash, the sons of Shemaah the Gibeathite; and Jeziel, and Pelet, the sons of Azmaveth; and Berachah, and Jehu the Antothite,12.3 Shemaah: or, Hasmaah 4And Ismaiah the Gibeonite, a mighty man among the thirty, and over the thirty; and Jeremiah, and Jahaziel, and Johanan, and Josabad the Gederathite, 5Eluzai, and Jerimoth, and Bealiah, and Shemariah, and Shephatiah the Haruphite, 6Elkanah, and Jesiah, and Azareel, and Joezer, and Jashobeam, the Korhites, 7And Joelah, and Zebadiah, the sons of Jeroham of Gedor. 8And of the Gadites there separated themselves unto David into the hold to the wilderness men of might, and men of war fit for the battle, that could handle shield and buckler, whose faces were like the faces of lions, and were as swift as the roes upon the mountains;12.8 of war: Heb. of the host12.8 as swift…: Heb. as the roes upon the mountains to make haste 9Ezer the first, Obadiah the second, Eliab the third, 10Mishmannah the fourth, Jeremiah the fifth, 11Attai the sixth, Eliel the seventh, 12Johanan the eighth, Elzabad the ninth, 13Jeremiah the tenth, Machbanai the eleventh. 14These were of the sons of Gad, captains of the host: one of the least was over an hundred, and the greatest over a thousand.12.14 one…: or, one that was least could resist an hundred, and the greatest a thousand 15These are they that went over Jordan in the first month, when it had overflown all his banks; and they put to flight all them of the valleys, both toward the east, and toward the west.12.15 overflown: Heb. filled over 16And there came of the children of Benjamin and Judah to the hold unto David. 17And David went out to meet them, and answered and said unto them, If ye be come peaceably unto me to help me, mine heart shall be knit unto you: but if ye be come to betray me to mine enemies, seeing there is no wrong in mine hands, the God of our fathers look thereon, and rebuke it.12.17 to meet…: Heb. before them12.17 be knit: Heb. be one12.17 wrong: or, violence 18Then the spirit came upon Amasai, who was chief of the captains, and he said, Thine are we, David, and on thy side, thou son of Jesse: peace, peace be unto thee, and peace be to thine helpers; for thy God helpeth thee. Then David received them, and made them captains of the band.12.18 came…: Heb. clothed 19And there fell some of Manasseh to David, when he came with the Philistines against Saul to battle: but they helped them not: for the lords of the Philistines upon advisement sent him away, saying, He will fall to his master Saul to the jeopardy of our heads.12.19 to the…: Heb. on our heads 20As he went to Ziklag, there fell to him of Manasseh, Adnah, and Jozabad, and Jediael, and Michael, and Jozabad, and Elihu, and Zilthai, captains of the thousands that were of Manasseh. 21And they helped David against the band of the rovers: for they were all mighty men of valour, and were captains in the host.12.21 against…: or, with a band 22For at that time day by day there came to David to help him, until it was a great host, like the host of God.

23¶ And these are the numbers of the bands that were ready armed to the war, and came to David to Hebron, to turn the kingdom of Saul to him, according to the word of the LORD.12.23 bands: or, captains, or, men: Heb. heads 24The children of Judah that bare shield and spear were six thousand and eight hundred, ready armed to the war.12.24 armed: or, prepared 25Of the children of Simeon, mighty men of valour for the war, seven thousand and one hundred. 26Of the children of Levi four thousand and six hundred. 27And Jehoiada was the leader of the Aaronites, and with him were three thousand and seven hundred; 28And Zadok, a young man mighty of valour, and of his father’s house twenty and two captains. 29And of the children of Benjamin, the kindred of Saul, three thousand: for hitherto the greatest part of them had kept the ward of the house of Saul.12.29 kindred: Heb. brethren12.29 the greatest…: Heb. a multitude of them 30And of the children of Ephraim twenty thousand and eight hundred, mighty men of valour, famous throughout the house of their fathers.12.30 famous: Heb. men of names 31And of the half tribe of Manasseh eighteen thousand, which were expressed by name, to come and make David king. 32And of the children of Issachar, which were men that had understanding of the times, to know what Israel ought to do; the heads of them were two hundred; and all their brethren were at their commandment. 33Of Zebulun, such as went forth to battle, expert in war, with all instruments of war, fifty thousand, which could keep rank: they were not of double heart.12.33 expert…: or, rangers of battle, or, ranged in battle12.33 keep…: or, set the battle in array12.33 not…: Heb. without a heart and a heart 34And of Naphtali a thousand captains, and with them with shield and spear thirty and seven thousand. 35And of the Danites expert in war twenty and eight thousand and six hundred. 36And of Asher, such as went forth to battle, expert in war, forty thousand.12.36 expert: or, keeping their rank 37And on the other side of Jordan, of the Reubenites, and the Gadites, and of the half tribe of Manasseh, with all manner of instruments of war for the battle, an hundred and twenty thousand. 38All these men of war, that could keep rank, came with a perfect heart to Hebron, to make David king over all Israel: and all the rest also of Israel were of one heart to make David king. 39And there they were with David three days, eating and drinking: for their brethren had prepared for them. 40Moreover they that were nigh them, even unto Issachar and Zebulun and Naphtali, brought bread on asses, and on camels, and on mules, and on oxen, and meat, meal, cakes of figs, and bunches of raisins, and wine, and oil, and oxen, and sheep abundantly: for there was joy in Israel.12.40 meat…: or, victual of meal