1 Mafumu 3 – CCL & NUB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 3:1-28

Solomoni Apempha Nzeru

1Solomoni anachita ubale ndi Farao mfumu ya ku Igupto ndipo anakwatira mwana wake wamkazi. Mkaziyo anabwera naye mu Mzinda wa Davide mpaka anatsiriza kumanga nyumba yaufumu ndi Nyumba ya Yehova ndiponso khoma lozungulira Yerusalemu. 2Koma anthu ankaperekabe nsembe ku malo achipembedzo osiyanasiyana chifukwa chakuti mpaka pa nthawi imeneyo Dzina la Yehova anali asanalimangire nyumba. 3Solomoni anaonetsa chikondi chake pa Yehova poyenda motsatira malamulo a abambo ake Davide, kupatula kuti ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo osiyanasiyana achipembedzo.

4Mfumu inapita ku Gibiyoni kukapereka nsembe popeza kumeneko ndiye kunali malo oposa malo ofunika kwambiri pachipembedzo. Kumeneko Solomoni anapereka nsembe zopsereza 1,000 pa guwa lansembe. 5Ku Gibiyoniko Yehova anaonekera kwa Solomoni mʼmaloto usiku, ndipo Mulungu anati, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”

6Solomoni anayankha kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa kapolo wanu, abambo anga Davide, chifukwa anali wokhulupirika pamaso panu, wolungama mtima ndiponso wa mtima wangwiro. Inu mukupitirizabe kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa iye ndipo mwamupatsa mwana kuti akhale pa mpando wake waufumu lero lino.

7“Tsopano Inu Yehova Mulungu wanga, mtumiki wanune mwandiyika kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo anga Davide. Komatu ndine mwana wamngʼono ndipo sindidziwa kagwiridwe kake ka ntchito yangayi. 8Mtumiki wanu ali pakati pa anthu amene munawasankha, mtundu waukulu, anthu ochuluka kwambiri osatheka kuwawerenga. 9Choncho mupatseni mtumiki wanu nzeru zolamulira anthu anu ndi kuti azitha kusiyanitsa pakati pa chabwino ndi choyipa. Pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”

10Ambuye anakondwera kuti Solomoni anapempha zimenezi. 11Tsono Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza wapempha zinthu zimenezi osati moyo wautali kapena chuma chako kapena imfa ya adani ako koma nzeru zolamulira anthu mwachilungamo, 12Ine ndidzakuchitira zimene wapempha. Ndidzakupatsa mtima wanzeru ndi wozindikira zinthu, kotero kuti sipanakhalepo wina wofanana nawe ndipo sipadzapezekanso wina wonga iwe pambuyo pako. 13Kuwonjeza apo, ndidzakupatsa zimene sunazipemphe: chuma ndi ulemu, kotero kuti pa masiku onse a moyo wako sipadzakhala mfumu yofanana nawe. 14Ndipo ngati udzayenda mʼnjira zanga ndi kumvera malamulo anga ndiponso malangizo anga monga abambo ako Davide anachitira, ndidzakupatsa moyo wautali.” 15Kotero Solomoni anadzuka ndipo anazindikira kuti anali maloto.

Iye anabwerera ku Yerusalemu nakayimirira patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Ambuye ndipo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Kenaka anakonzera phwando atumiki ake onse.

Kuweruza Kolungama

16Nthawi ina amayi awiri adama anabwera kwa mfumu ndipo anayima pamaso pake. 17Mmodzi mwa amayiwo anati, “Mbuye wanga, mayi uyu ndi ine timakhala nyumba imodzi. Ine ndinabala mwana tili limodzi ndi mnzangayu. 18Tsiku lachitatu ine nditabala mwana, mnzangayunso anabereka mwana wake. Tinalipo awiriwiri mʼnyumbamo ndipo munalibe wina aliyense.

19“Nthawi ya usiku mwana wa mnzangayu anafa chifukwa anamugonera. 20Tsono iyeyu anadzuka pakati pa usiku, natenga mwana wanga ku mimba kwanga pamene ine mdzakazi wanu ndinali mʼtulo. Anamuyika mwanayo ku mimba kwake ndi kuyika mwana wake wakufayo ku mimba kwanga. 21Mmawa nditadzuka kuti ndiyamwitse mwana wanga ndinapeza kuti ndi wakufa! Koma kutacha nditamuyangʼanitsitsa ndinaona kuti si mwana amene ine ndinabala.”

22Koma mayi winayo anati, “Ayi! Mwana wamoyoyu ndi wanga, mwana wakufayu ndi wako.”

Koma mayi woyambayo analimbikira kuti. “Ayi! Mwana wakufayu ndi wako; wamoyoyu ndi wanga.” Motero akaziwa anatsutsana pamaso pa mfumu.

23Pamenepo mfumu inati, “Wina akuti, ‘Mwana wanga ndi wamoyoyu ndipo mwana wako ndi wakufayu,’ pamene winanso akuti, ‘Ayi! Mwana wako ndi wakufayu wanga ndi wamoyoyu.’ ”

24Pamenepo mfumu inati, “Patseni lupanga.” Ndipo anabwera nalo lupanga kwa mfumu. 25Tsono mfumu inagamula kuti, “Muduleni pakati mwana wamoyoyu ndipo wina mumupatse gawo limodzi, gawo linalo mumupatse winayo.”

26Mayi amene mwana wake anali moyo anagwidwa ndi chisoni chifukwa cha mwana wakeyo ndipo anawuza mfumu kuti, “Chonde mbuye wanga, mupatseni mnzangayu mwana wamoyoyu! Musamuphe!”

Koma winayo anati, “Ayi, asandipatse ine kapena iwe. Muduleni pakati!”

27Choncho mfumu inagamula kuti, “Perekani mwana wamoyoyu kwa mayi woyambayu. Musamuphe, iyeyu ndiye mayi wake wa mwanayu.”

28Pamene Aisraeli onse anamva za chigamulo chimene mfumu inapereka, anaopa mfumuyo kwambiri, chifukwa anaona kuti mfumu inali ndi nzeru zochokera kwa Mulungu zoweruzira mwachilungamo.

Swedish Contemporary Bible

1 Kungaboken 3:1-28

1Salomo ingick en allians med farao, kungen i Egypten, och gifte sig med hans dotter. Han tog henne med sig till Davids stad, där hon bodde tills han hade byggt färdigt sitt palats, Herrens hus och muren runt Jerusalem.

2Folket offrade på höjderna eftersom något tempel åt Herrens namn ännu inte var byggt.

Salomo ber om vishet

(2 Krön 1:3-12)

3Salomo visade sin kärlek till Herren genom att följa de stadgar han fått av sin far David, bortsett från att han fortsatte att offra på höjderna och tända rökelse där. 4Den främsta offerplatsen fanns i Givon och dit gick kungen och bar fram 1 000 brännoffer på altaret där.

5I Givon uppenbarade sig Herren för Salomo en natt i en dröm och sa: ”Be mig om vad du vill, så ska du få det!”

6Salomo svarade: ”Du har visat stor nåd mot din tjänare David, min far, därför att han var trogen mot dig och rättfärdig och uppriktig i sitt hjärta. Du har fortsatt att visa samma stora nåd genom att ge honom en son som nu sitter på hans tron. 7Herre min Gud, nu har du gjort mig till kung efter min far David, men jag är ju oerfaren som ett barn och vet oftast inte hur jag ska handla. 8Du har satt mig, din tjänare, över ditt utvalda folk, en nation så stor att man inte kan räkna dem. 9Ge mig, din tjänare, nu ett lydigt hjärta och ett sådant förstånd att jag kan regera på rätt sätt över ditt folk och förstå skillnaden mellan rätt och orätt! För vem kan styra ditt folk som är så stort?”

10Herren var mycket nöjd med och glad över att Salomo bad om detta. 11Gud svarade honom: ”Därför att du bad om detta och inte om ett långt liv, rikedom för egen del eller dina fienders undergång, utan bad om förmåga att urskilja vad som är rätt, 12ja, därför ska jag ge dig vad du har bett om. Jag ska ge dig större vishet än någon annan någonsin haft eller kommer att få. 13Jag ska dessutom ge dig vad du inte bad om, nämligen ära och rikedom. Ingen i hela världen ska under din livstid bli din like bland kungar, 14och om du vandrar på mina vägar och lyder mina lagar som din far David gjorde, så ska jag låta dig få leva länge.”

15Sedan vaknade Salomo och förstod att det varit en dröm.

Han återvände till Jerusalem och ställde sig framför Herrens förbundsark. Där bar han fram brännoffer och gemenskapsoffer, och sedan inbjöd han hela hovet till en fest.

Salomo visar prov på sin vishet

16Två prostituerade kvinnor kom till kungen och trädde fram inför honom.

17”Hör, min herre, vi bor båda i samma hus”, började en av dem. ”Jag fick ett barn och hon var också där i huset. 18Tredje dagen efter att mitt barn fötts fick den här kvinnan också ett barn. Vi var ensamma och det var inga andra i huset. 19Men hennes barn dog när hon i sömnen råkade lägga sig på det. 20Då gick hon upp mitt i natten när jag, din tjänarinna, sov, tog min son som låg bredvid mig till sig och lade det döda barnet i mina armar. 21På morgonen när jag skulle ge mitt barn mat, upptäckte jag att det var dött, men när jag såg närmare på det på morgonen, såg jag att det inte var det barn jag fött.”

22Den andra kvinnan sa: ”Det var visst hennes egen son och barnet som lever är mitt!” Men den första stod på sig: ”Nej, det döda barnet är ditt och det som lever är mitt!” På det sättet grälade de alltså inför kungen.

23Då sa kungen: ”Den ena säger att det levande barnet är hennes och att det döda barnet tillhör den andra. Den andra säger att det levande barnet är hennes och det döda den andras. 24Ge mig nu ett svärd!” Man hämtade ett svärd till kungen. 25”Hugg det levande barnet i två delar och låt de båda kvinnorna få var sin del”, sa kungen.

26Barnets mor som fylldes av kärlek till sin son, utropade då: ”Nej, min herre! Ge henne barnet i stället! Döda det inte!” ”Nej, varken du eller jag ska ha honom”, sa den andra kvinnan. ”Dela honom mitt itu!”

27Då befallde kungen: ”Ge den levande pojken till den första kvinnan! Hon är hans mor.”

28Över hela Israel fick man höra talas om den dom kung Salomo avkunnade och alla visade honom vördnad, för de insåg vilken vishet Gud hade gett honom.