1 Mafumu 3 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 3:1-28

Solomoni Apempha Nzeru

1Solomoni anachita ubale ndi Farao mfumu ya ku Igupto ndipo anakwatira mwana wake wamkazi. Mkaziyo anabwera naye mu Mzinda wa Davide mpaka anatsiriza kumanga nyumba yaufumu ndi Nyumba ya Yehova ndiponso khoma lozungulira Yerusalemu. 2Koma anthu ankaperekabe nsembe ku malo achipembedzo osiyanasiyana chifukwa chakuti mpaka pa nthawi imeneyo Dzina la Yehova anali asanalimangire nyumba. 3Solomoni anaonetsa chikondi chake pa Yehova poyenda motsatira malamulo a abambo ake Davide, kupatula kuti ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo osiyanasiyana achipembedzo.

4Mfumu inapita ku Gibiyoni kukapereka nsembe popeza kumeneko ndiye kunali malo oposa malo ofunika kwambiri pachipembedzo. Kumeneko Solomoni anapereka nsembe zopsereza 1,000 pa guwa lansembe. 5Ku Gibiyoniko Yehova anaonekera kwa Solomoni mʼmaloto usiku, ndipo Mulungu anati, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”

6Solomoni anayankha kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa kapolo wanu, abambo anga Davide, chifukwa anali wokhulupirika pamaso panu, wolungama mtima ndiponso wa mtima wangwiro. Inu mukupitirizabe kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa iye ndipo mwamupatsa mwana kuti akhale pa mpando wake waufumu lero lino.

7“Tsopano Inu Yehova Mulungu wanga, mtumiki wanune mwandiyika kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo anga Davide. Komatu ndine mwana wamngʼono ndipo sindidziwa kagwiridwe kake ka ntchito yangayi. 8Mtumiki wanu ali pakati pa anthu amene munawasankha, mtundu waukulu, anthu ochuluka kwambiri osatheka kuwawerenga. 9Choncho mupatseni mtumiki wanu nzeru zolamulira anthu anu ndi kuti azitha kusiyanitsa pakati pa chabwino ndi choyipa. Pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”

10Ambuye anakondwera kuti Solomoni anapempha zimenezi. 11Tsono Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza wapempha zinthu zimenezi osati moyo wautali kapena chuma chako kapena imfa ya adani ako koma nzeru zolamulira anthu mwachilungamo, 12Ine ndidzakuchitira zimene wapempha. Ndidzakupatsa mtima wanzeru ndi wozindikira zinthu, kotero kuti sipanakhalepo wina wofanana nawe ndipo sipadzapezekanso wina wonga iwe pambuyo pako. 13Kuwonjeza apo, ndidzakupatsa zimene sunazipemphe: chuma ndi ulemu, kotero kuti pa masiku onse a moyo wako sipadzakhala mfumu yofanana nawe. 14Ndipo ngati udzayenda mʼnjira zanga ndi kumvera malamulo anga ndiponso malangizo anga monga abambo ako Davide anachitira, ndidzakupatsa moyo wautali.” 15Kotero Solomoni anadzuka ndipo anazindikira kuti anali maloto.

Iye anabwerera ku Yerusalemu nakayimirira patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Ambuye ndipo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Kenaka anakonzera phwando atumiki ake onse.

Kuweruza Kolungama

16Nthawi ina amayi awiri adama anabwera kwa mfumu ndipo anayima pamaso pake. 17Mmodzi mwa amayiwo anati, “Mbuye wanga, mayi uyu ndi ine timakhala nyumba imodzi. Ine ndinabala mwana tili limodzi ndi mnzangayu. 18Tsiku lachitatu ine nditabala mwana, mnzangayunso anabereka mwana wake. Tinalipo awiriwiri mʼnyumbamo ndipo munalibe wina aliyense.

19“Nthawi ya usiku mwana wa mnzangayu anafa chifukwa anamugonera. 20Tsono iyeyu anadzuka pakati pa usiku, natenga mwana wanga ku mimba kwanga pamene ine mdzakazi wanu ndinali mʼtulo. Anamuyika mwanayo ku mimba kwake ndi kuyika mwana wake wakufayo ku mimba kwanga. 21Mmawa nditadzuka kuti ndiyamwitse mwana wanga ndinapeza kuti ndi wakufa! Koma kutacha nditamuyangʼanitsitsa ndinaona kuti si mwana amene ine ndinabala.”

22Koma mayi winayo anati, “Ayi! Mwana wamoyoyu ndi wanga, mwana wakufayu ndi wako.”

Koma mayi woyambayo analimbikira kuti. “Ayi! Mwana wakufayu ndi wako; wamoyoyu ndi wanga.” Motero akaziwa anatsutsana pamaso pa mfumu.

23Pamenepo mfumu inati, “Wina akuti, ‘Mwana wanga ndi wamoyoyu ndipo mwana wako ndi wakufayu,’ pamene winanso akuti, ‘Ayi! Mwana wako ndi wakufayu wanga ndi wamoyoyu.’ ”

24Pamenepo mfumu inati, “Patseni lupanga.” Ndipo anabwera nalo lupanga kwa mfumu. 25Tsono mfumu inagamula kuti, “Muduleni pakati mwana wamoyoyu ndipo wina mumupatse gawo limodzi, gawo linalo mumupatse winayo.”

26Mayi amene mwana wake anali moyo anagwidwa ndi chisoni chifukwa cha mwana wakeyo ndipo anawuza mfumu kuti, “Chonde mbuye wanga, mupatseni mnzangayu mwana wamoyoyu! Musamuphe!”

Koma winayo anati, “Ayi, asandipatse ine kapena iwe. Muduleni pakati!”

27Choncho mfumu inagamula kuti, “Perekani mwana wamoyoyu kwa mayi woyambayu. Musamuphe, iyeyu ndiye mayi wake wa mwanayu.”

28Pamene Aisraeli onse anamva za chigamulo chimene mfumu inapereka, anaopa mfumuyo kwambiri, chifukwa anaona kuti mfumu inali ndi nzeru zochokera kwa Mulungu zoweruzira mwachilungamo.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

3 Царств 3:1-28

Просьба Сулаймона о мудрости

(2 Лет. 1:3-12)

1Сулаймон породнился с фараоном, царём Египта, женившись на его дочери. Он поселил её в Городе Довуда, пока не закончил строить свой дворец, храм Вечного и стену вокруг Иерусалима.

2А народ, по-прежнему, приносил жертвы в святилищах на возвышенностях, потому что храм для поклонения Вечному всё ещё не был построен. 3Сулаймон любил Вечного, следуя наказам своего отца Довуда, но и он приносил жертвы и возжигал благовония, находящиеся в сосудах, в святилищах на возвышенностях.

4Царь отправился в Гаваон, чтобы принести жертвы, потому что там было самое главное из святилищ, и вознёс на том жертвеннике тысячу всесожжений. 5В Гаваоне Вечный явился Сулаймону во сне ночью. Всевышний сказал:

– Проси у Меня, чего хочешь.

6Сулаймон ответил:

– Ты явил Твоему рабу, моему отцу Довуду, великую милость, так как он был верен Тебе, праведен и прям сердцем. Ты сохранил эту великую милость и даровал ему сына, чтобы тот сегодня сел на его престол. 7И теперь, Вечный, мой Бог, Ты сделал Твоего раба царём вместо моего отца Довуда. Но я совсем молод и не знаю, как исполнять свой долг. 8Твой раб – среди Твоего народа, который Ты избрал, великого народа, слишком многочисленного, чтобы его пересчитать или исчислить. 9Дай Твоему рабу разумное сердце, чтобы править Твоим народом и различать между добром и злом. Ведь кто способен править Твоим многочисленным народом?

10Владыка был доволен, что Сулаймон просил об этом. 11Всевышний сказал ему:

– Так как ты просил об этом и не просил себе ни долгой жизни, ни богатства, ни смерти своим врагам, но лишь мудрости, чтобы разумно судить, 12Я исполню то, о чём ты просил. Я даю тебе мудрое и разумное сердце, и как до тебя не было подобного тебе, так и после тебя никто с тобой не сравнится. 13Более того, Я даю тебе и то, о чём ты не просил, – и богатство, и славу, так что при твоей жизни среди царей тебе не будет равного. 14И если ты будешь ходить Моими путями и слушаться Моих установлений и повелений, как делал твой отец Довуд, Я дам тебе долгую жизнь.

15Тут Сулаймон проснулся и понял, что это был сон. Он пришёл в Иерусалим, встал перед сундуком соглашения с Владыкой и принёс всесожжения и жертвы примирения. После этого он устроил для всего двора пир.

Мудрое разрешение спора

16Однажды к царю пришли две женщины-блудницы и встали перед ним. 17Одна из них сказала:

– О мой господин! Мы с этой женщиной живём в одном доме, и когда она была в доме, я родила. 18А на третий день после этого родила и она. Мы были вместе, никого с нами в доме не было, только мы вдвоём. 19Ночью сын этой женщины умер, потому что она случайно задавила его во сне. 20Среди ночи она поднялась и взяла моего сына, пока твоя рабыня спала. Она положила его к своей груди, а своего мёртвого сына положила к моей груди. 21Утром я встала, чтобы покормить своего сына, а он мёртвый, но когда я рассмотрела его на свету, мне стало ясно, что это не мой сын, которого я родила.

22Другая женщина сказала:

– Нет! Тот, что живой, – это мой сын, твой – тот, что мёртвый!

Но первая настаивала:

– Нет! Тот, что мёртвый, – твой, а живой – мой!

И так они препирались перед царём.

23Царь сказал:

– Одна говорит: «Мой сын жив, а твой мёртв», а другая говорит: «Нет! Твой сын мёртв, а мой жив».

24Затем царь сказал:

– Принесите мне меч.

И царю принесли меч. 25Тогда он повелел:

– Разрубите живого ребёнка надвое и дайте одну половину этой женщине, а другую – той.

26У той женщины, чей сын был жив, вздрогнуло сердце от жалости к своему сыну, и она сказала царю:

– О мой господин! Отдайте ей ребёнка живым! Не убивайте его!

Но другая сказала:

– Ни я, ни ты его не получим. Разрубите его!

27Тогда царь постановил:

– Отдайте живого ребёнка первой женщине. Не убивайте его, она его мать.

28Когда весь Исроил услышал о приговоре, который вынес царь, они стали уважать его, потому что увидели, что в нём мудрость от Всевышнего, чтобы творить суд.