1 Mafumu 17 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 17:1-24

Makwangwala Adyetsa Eliya

1Ndipo mneneri Eliya wa ku Tisibe ku Giliyadi, anati kwa Ahabu, “Pali Yehova wamoyo, Mulungu wa Israeli, amene ndimamutumikira, sipadzakhala mame kapena mvula zaka zikubwerazi, pokhapokha ine nditanena.”

2Pamenepo Yehova anayankhula ndi Eliya kuti, 3“Choka kuno, upite kummawa, ukabisale mʼmbali mwa mtsinje wa Keriti, pafupi ndi Yorodani. 4Uzikamwa mu mtsinjemo, ndipo ndalamula makwangwala kuti azikakudyetsa kumeneko.”

5Choncho Eliya anachita zomwe Yehova anamuwuza. Anapita ku mtsinje wa Keriti, pafupi ndi Yorodani, nakakhala kumeneko. 6Makwangwala ankabweretsera buledi ndi nyama mmawa ndi madzulo, ndipo ankamwa mu mtsinjemo.

Mayi Wamasiye wa ku Zarefati

7Patapita masiku, mtsinjewo unaphwa chifukwa mvula sinagwe mʼdzikomo. 8Yehova anayankhula naye kuti, 9“Nyamuka tsopano, pita ku Zarefati ku Sidoni ndipo ukakhale kumeneko. Ndalamula mkazi wamasiye wa kumeneko kuti azikakudyetsa.” 10Choncho iye ananyamuka napita ku Zarefati. Atafika pa chipata cha mzindawo, taonani mkazi wamasiye amatola nkhuni. Anamuyitana ndi kumuwuza kuti, “Patseni madzi pangʼono mʼchikho kuti ndimwe.” 11Mayi wamasiye uja ankapita kukatunga madzi, Eliya anamuyitananso namuwuza kuti, “Chonde munditengerekonso buledi.”

12Iye anayankha kuti “Pali Yehova Mulungu wanu wamoyo, ine ndilibe chakudya china chilichonse, koma kaufa pangʼono mʼmbiya ndi mafuta pangʼono mʼbotolo. Ine ndikutola tinkhuni tochepa kuti ndipite nato ku nyumba ndi kukaphika chakudya changa ndi cha mwana wanga, kuti tikadye kenaka tife.”

13Eliya anati kwa iye, “Musachite mantha. Pitani mukachite monga mwaneneramo. Koma poyamba mundipangire kachakudya pangʼono kuchokera pa ufa umene muli nawo ndi kubwera nako kwa ine, ndipo kenaka mukaphike choti mudye inuyo ndi mwana wanuyo. 14Pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ufa umene uli mʼmbiyamo sudzatha ndipo mafuta amene ali mʼbotolomo sadzathanso mpaka tsiku limene Yehova adzagwetse mvula pa dziko lapansi.’ ”

15Mayi wamasiyeyo anapita nakachita zimene Eliya anamuwuza. Choncho panali chakudya cha Eliya, mayiyo pamodzi ndi banja lake lonse chimene anadya masiku ambiri. 16Pakuti ufa umene unali mʼmbiya sunathe ndiponso mafuta amene anali mʼbotolo sanathe, monga momwe ananenera Yehova kudzera mwa Eliya.

17Tsiku lina mwana wake wa mkazi wamasiye uja, mwini nyumbayo, anadwala. Matenda ananka nakulirakulirabe, ndipo kenaka analeka kupuma. 18Mayiyo anati kwa Eliya, “Kodi ndakulakwirani chiyani, inu munthu wa Mulungu? Kodi munabwera kuno kudzandikumbutsa tchimo langa ndi kudzandiphera mwana wanga?”

19Eliya anayankha kuti, “Patseni mwana wanuyo.” Iye anatenga mwanayo mʼmanja mwa mayiyo napita naye mʼchipinda chapamwamba, kumene Eliyayo amagona, namugoneka pa bedi lake. 20Kenaka Eliya anafuwula kwa Yehova nati, “Inu Yehova Mulungu wanga, kodi mwabweretsanso choyipa chotere pa mkazi wamasiye amene ine ndikukhala naye, pakuchititsa kuti mwana wake afe?” 21Pamenepo Eliya anakumbatira mwanayo katatu ndi kufuwula kwa Yehova kuti, “Inu Yehova Mulungu wanga, mubwezereni mwanayu moyo wake!”

22Yehova anamva kufuwula kwa Eliya, ndipo moyo wa mwanayo unabwerera mwa iye ndipo anatsitsimuka. 23Eliya ananyamula mwanayo natsika naye kuchoka mʼchipinda chapamwamba chija nalowa naye mʼnyumba. Anamupereka kwa amayi ake ndipo anati, “Taonani, mwana wanu ali ndi moyo!”

24Pamenepo mayiyo anati kwa Eliya, “Tsopano ndadziwa kuti ndinu munthu wa Mulungu ndipo mawu a Yehova amene mumayankhula ndi owona.”

New Russian Translation

3 Царств 17:1-24

Илия предсказывает засуху

1Илия из Тишбы, что в Галааде17:1 Или: «тишбитянин из галаадских поселенцев»., сказал Ахаву:

– Верно, как и то, что жив Господь, Бог Израиля, Которому я служу, – в эти годы не будет ни росы, ни дождя, разве только по моему слову.

2К Илии было слово Господа:

3– Уходи отсюда, поверни на восток и спрячься у реки Керита, что к востоку от Иордана. 4Из реки ты будешь пить, а кормить тебя Я повелел воронам.

5И он сделал, как сказал ему Господь. Он пошел к реке Кериту, что к востоку от Иордана, и остался там. 6Вороны приносили ему хлеб и мясо утром и вечером, а пил он из реки.

Илия и вдова из Сарепты

7Через некоторое время река пересохла, потому что в стране не было дождя. 8Тогда к нему было слово Господа:

9– Теперь ступай в Сарепту17:9 Сарепта – финикийский город, находившийся на территории современного государства Ливан. А значит пророк должен был покинуть пределы Израиля., что близ Сидона, и живи там. Я повелел одной вдове кормить тебя.

10И он пошел в Сарепту. Когда он подошел к воротам города, там была вдова, которая собирала дрова. Он позвал ее и сказал:

– Принеси мне в сосуде немного воды попить.

11Когда она пошла, он окликнул ее и сказал:

– Принеси мне и кусок хлеба.

12– Верно, как и то, что жив Господь, твой Бог, – ответила она, – у меня нет хлеба – лишь пригоршня муки в кадке да немного масла в кувшине. Вот возьму пару поленьев и пойду, приготовлю из этой муки еду для себя и для сына. Съедим это, а потом и умрем.

13Илия сказал ей:

– Не бойся. Иди домой и сделай так, как сказала. Но сперва сделай для меня из того, что у тебя есть, маленькую лепешку и принеси мне, а потом приготовь что-нибудь для себя и своего сына. 14Ведь так говорит Господь, Бог Израиля: «Мука в кадке не переведется и масло в кувшине не кончится до того дня, когда Господь пошлет на землю дождь».

15Она пошла и сделала так, как сказал ей Илия. И каждый день у нее, у Илии и у ее семьи была пища. 16Мука в кадке не переводилась и масло в кувшине не кончалось – по слову Господа, сказанному Илией.

Воскрешение сына вдовы

17Через некоторое время сын той женщины, хозяйки дома, заболел. Ему становилось все хуже и хуже, и наконец он перестал дышать. 18Тогда она сказала Илии:

– Что у тебя против меня, человек Божий? Ты пришел, чтобы напомнить мне о моем грехе и убить моего сына?

19– Дай мне своего сына, – ответил ей Илия.

Он взял его у нее из рук, отнес в верхнюю комнату, где он жил, и положил его на постель. 20Затем он воззвал к Господу:

– Господи, Боже мой, неужели Ты наведешь беду и на вдову, у которой я живу, умертвив ее сына?

21Он простерся над мальчиком три раза и воззвал к Господу:

– Господи, Боже мой, пусть жизнь этого мальчика вернется к нему!

22Господь услышал мольбу Илии, и жизнь мальчика вернулась к нему, и он ожил. 23Илия взял мальчика и отнес его вниз из своей комнаты в дом. Он отдал его матери и сказал:

– Смотри, твой сын жив!

24Женщина сказала Илии:

– Теперь я знаю, что ты – человек Божий и что слово Господа, сказанное тобой, истинно.