1 Mafumu 16 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 16:1-34

1Ndipo Yehova anayankhula kudzera mwa Yehu mwana wa Hanani, mawu odzudzula Baasa kuti, 2“Ine ndinakukuza kuchokera pa fumbi ndipo ndinakupanga kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli, koma iwe wakhala ukuyenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchimwitsa anthu anga Aisraeli naputa mkwiyo wanga chifukwa cha machimo awo. 3Taonani, Ine ndatsala pangʼono kuwononga Baasa pamodzi ndi nyumba yake, ndipo ndidzachitira nyumba yake zimene ndinachita pa nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati. 4Agalu adzadya aliyense wa banja la Baasa amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya iwo amene adzafere kuthengo.”

5Tsono ntchito zina za Baasa ndi zamphamvu zake zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli? 6Baasa anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Tiriza. Ndipo Ela mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake.

7Komatu Yehova anayankhula kwa Baasa pamodzi ndi banja lake lonse kudzera mwa mneneri Yehu mwana wa Hanani, chifukwa cha zoyipa zonse zimene iye anachita pamaso pa Yehova, kukwiyitsa Yehovayo nakhala ngati nyumba ya Yeroboamu ndiponso chifukwa anawonongeratu banja la Yeroboamu.

Ela Mfumu ya Israeli

8Mʼchaka cha 26 cha ufumu wa Asa mfumu ya Yuda, Ela mwana wa Baasa anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira ku Tiriza zaka ziwiri.

9Zimuri, mmodzi mwa akuluakulu ake, amene ankalamulira theka la magaleta ake, anamuchitira chiwembu. Nthawi imeneyi Ela anali ku Tiriza, akumwa koledzera nako mʼnyumba ya Ariza, munthu amene ankayangʼanira nyumba yaufumu ku Tiriza. 10Zimuri anadzalowa, namukantha ndi kumupha mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda. Ndipo Zimuriyo anakhala mfumu mʼmalo mwake.

11Zimuri atangoyamba kulamulira, anapha banja lonse la Baasa. Sanasiyepo munthu wamwamuna ndi mmodzi yemwe, wachibale kapena bwenzi lake. 12Choncho Zimuri anawononga banja lonse la Baasa, molingana ndi mawu amene Yehova anayankhula motsutsa Baasa kudzera mwa mneneri Yehu, 13chifukwa cha machimo onse amene Baasa ndi mwana wake Ela anachita nachimwitsa Israeli, anakwiyitsa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi mafano awo osapindulitsa.

14Tsono ntchito zina za Ela ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?

Zimuri Mfumu ya Israeli

15Mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda, Zimuri analamulira ku Tiriza masiku asanu ndi awiri. Gulu la ankhondo linali litamanga misasa pafupi ndi Gibetoni, mzinda wa Afilisti. 16Ankhondo amene anali ku misasa atamva kuti Zimuri wachita chiwembu ndi kupha mfumu, tsiku lomwelo ku misasako anasankha Omuri, mkulu wa ankhondo kukhala mfumu ya Israeli. 17Tsono Omuri ndi Aisraeli onse amene anali naye anachoka ku Gibetoni ndi kukazinga Mzinda wa Tiriza. 18Zimuri ataona kuti mzinda walandidwa, anathawira ku nsanja ya nyumba ya mfumu ndipo anatentha nyumbayo iye ali momwemo. Kotero iyeyo anafa, 19chifukwa cha machimo amene iye anachita, kuchita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuyenda mʼnjira za Yeroboamu, nachimwitsa nazo Aisraeli.

20Tsono ntchito zina za Zimuri ndi chiwembu chake chimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?

Omuri Mfumu ya Israeli

21Pambuyo pake Aisraeli anagawikana pakati: theka linatsatira Tibini mwana wa Ginati kuti limulonge ufumu, ndipo theka lina linatsatira Omuri. 22Koma anthu otsatira Omuri anali amphamvu kupambana amene ankatsatira Tibini mwana wa Ginati. Choncho Tibini anafa ndipo Omuri anakhala mfumu.

23Mʼchaka cha 31 cha Asa mfumu ya Yuda, Omuri anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira zaka 12 ndi miyezi isanu ndi umodzi ku Tiriza. 24Iye anagula phiri la Samariya kwa Semeri pa mtengo wa ndalama 6,000 za siliva ndipo pa phiripo anamangapo mzinda, nawutcha Samariya, potsata dzina la Semeri, dzina la mwini wakale wa phirilo.

25Koma Omuri anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anachimwa kuposa mafumu ena onse amene analipo iye asanakhale mfumu. 26Pakuti iye anayenda mʼnjira zonse za Yeroboamu mwana wa Nebati, ndipo tchimo lake anachimwitsa nalo Aisraeli, nakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli ndi mafano awo opandapake.

27Tsono ntchito zina za Omuri ndi zamphamvu zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli? 28Choncho Omuri anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Samariya. Ndipo Ahabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

Ahabu Akhala Mfumu ya Israeli

29Mʼchaka cha 38 cha ufumu wa Asa, mfumu ya Yuda, Ahabu mwana wa Omuri anakhala mfumu ya Israeli nalamulira Israeli ku Samariya zaka 22. 30Ahabu mwana wa Omuri anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova kupambana mafumu onse akale. 31Iye sanachiyese ngati chinthu chochepa chabe kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, koma anakwatiranso Yezebeli, mwana wa Etibaala mfumu ya Asidoni, nayamba kutumikira Baala ndi kumupembedza. 32Iye anapangira Baala guwa lansembe mʼnyumba ya Baala imene anamanga ku Samariya. 33Ahabu anapanganso fano la Asera ndi kukwiyitsa kwambiri Yehova Mulungu wa Israeli, kupambana mafumu onse a Israeli amene analipo iye asanakhale mfumu.

34Pa nthawi ya Ahabu, Hiyeli wa ku Beteli anamanganso mzinda wa Yeriko. Pa nthawi yomanga maziko ake, mwana wake woyamba wa mwamuna, Abiramu anamwalira, ndipo pa nthawi yomanga zipata zake, mwana wa mngʼono wa mwamuna Segubu, anamwaliranso. Izi zinachitika monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa Yoswa mwana wa Nuni.

Священное Писание

3 Царств 16:1-34

1К Иеву, сыну Ханани, было слово Вечного о Бааше:

2– Я поднял тебя, Бааша, из праха и сделал вождём Моего народа Исраила, но ты ходил путями Иеровоама и склонял Мой народ Исраил к греху, вызывая Мой гнев. 3И вот Я истреблю тебя и твой дом и сделаю с твоим домом то же, что с домом Иеровоама, сына Невата. 4Тех из твоей семьи, кто умрёт в городе, пожрут псы, а тех, кто умрёт в поле, склюют птицы.

5Прочие события царствования Бааши, то, что он сделал, и его свершения записаны в «Книге летописей царей Исраила». 6Бааша упокоился со своими предками и был похоронен в Тирце. И царём вместо него стал его сын Ела.

7Но через пророка Иеву, сына Ханани, уже было слово Вечного о Бааше и о его доме – за всё то зло, что он совершил в глазах Вечного, вызывая Его гнев делами, которые творил, подражая дому Иеровоама, а также за то, что он его уничтожил.

Ела – царь Исраила

8На двадцать шестом году правления Асы, царя Иудеи, царём Исраила стал Ела, сын Бааши, и правил в Тирце два года.

9Зимри, один из его приближённых, под началом у которого была половина царских колесниц, составил против него заговор. Когда Ела был в Тирце и напился до бесчувствия в доме Арцы, распорядителя его дворца, 10Зимри вошёл и убил его. Это было на двадцать седьмом году правления Асы, царя Иудеи. Зимри стал царём вместо Елы.

11Как только он воцарился и воссел на престол, он тут же перебил всю семью Бааши. Он не оставил в живых ни одного мужчину – ни родственника, ни друга. 12Зимри истребил всю семью Бааши по слову, которое Вечный сказал о Бааше через пророка Иеву: 13за все грехи, которые Бааша и его сын Ела совершили сами и заставили совершить Исраил, вызывая гнев Вечного, Бога Исраила, ничтожными идолами.

14Прочие события царствования Елы и всё, что он сделал, записано в «Книге летописей царей Исраила».

Борьба за власть в Исраиле

15На двадцать седьмом году правления Асы, царя Иудеи, Зимри стал править в Тирце, но правил всего семь дней. Войско тогда стояло станом у филистимского города Гиббетона. 16Когда исраильтяне в стане услышали о том, что Зимри составил заговор против царя и убил его, они в тот же день провозгласили царём Исраила военачальника Омри. 17После этого Омри и все исраильтяне ушли из-под Гиббетона и осадили Тирцу. 18Когда Зимри увидел, что город взят, он ушёл во внутренние укрепления царского дворца и поджёг его. Так он погиб 19из-за грехов, которые он совершил, творя зло в глазах Вечного, и за то, что ходил путями Иеровоама, пребывая в грехе, который тот совершил сам и к которому склонил Исраил.

20Прочие события царствования Зимри и заговор, который он составил, записаны в «Книге летописей царей Исраила».

21Тогда народ Исраила разделился: половина народа хотела сделать царём Тивни, сына Гината, а другая половина стояла за Омри. 22Но сторонники Омри оказались сильнее сторонников Тивни, сына Гината. И Тивни погиб, а Омри стал царём.

Омри – царь Исраила

23На тридцать первом году правления Асы, царя Иудеи, Омри стал царём Исраила и правил двенадцать лет, из них шесть – в Тирце. 24Он купил самарийский холм у Шемера за семьдесят два килограмма16:24 Букв.: «два таланта». серебра и построил на холме город, назвав его Самарией – по имени Шемера, бывшего владельца холма.

25Омри делал зло в глазах Вечного и грешил больше, чем все, кто был до него. 26Он ходил всеми путями Иеровоама, сына Невата, и пребывал в его грехе, к которому тот склонил Исраил, гневя Вечного, Бога Исраила, ничтожными идолами.

27Прочие события царствования Омри, то, что он сделал, и его свершения записаны в «Книге летописей царей Исраила». 28Омри упокоился со своими предками и был похоронен в Самарии. И царём вместо него стал его сын Ахав.

Ахав – царь Исраила

29На тридцать восьмом году правления Асы, царя Иудеи, царём Исраила стал Ахав, сын Омри, и правил в Самарии Исраилом двадцать два года. 30Ахав, сын Омри, делал больше зла в глазах Вечного, чем все, кто был до него. 31Мало того, что он оставался в грехах Иеровоама, сына Невата, он ещё и женился на Иезевели, дочери Этбаала, царя сидонян, и начал служить Баалу16:31 Баал – ханаанский бог плодородия и бог-громовержец. и поклоняться ему. 32Он установил жертвенник в храме Баала, который построил в Самарии. 33Ещё Ахав делал столбы Ашеры, и больше, чем все цари Исраила до него, он делал то, что вызывало гнев Вечного, Бога Исраила.

34Во времена Ахава Хиил из Вефиля восстановил Иерихон. Он заложил его основания ценой своего первенца Авирама и поставил его ворота ценой своего младшего сына Сегува, по слову Вечного, сказанному через Иешуа, сына Нуна16:34 См. Иеш. 6:25. Вероятно, Хиил принёс своих сыновей в жертву, что было обычным среди окружавших исраильтян языческих народов и говорило о духовном падении народа Всевышнего..