1 Mafumu 13 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 13:1-34

Munthu wa Mulungu Wochokera ku Yuda

1Ndipo taonani, munthu wa Mulungu wochokera ku Yuda anapita ku Beteli molamulidwa ndi Yehova. Nthawi imeneyo nʼkuti Yeroboamu atayimirira pambali pa guwa akufukiza lubani. 2Mneneriyo anatemberera guwalo mofuwula potsata mawu a Yehova nati: “Guwa iwe, guwa iwe! Yehova akuti, ‘Taonani mʼbanja la Davide mudzabadwa mwana dzina lake Yosiya. Pa iwe, iyeyo adzaperekapo ngati nsembe, ansembe otumikira ku malo achipembedzo amene tsopano akufukiza lubani pa iwe, ndipo pa iwe adzatenthapo mafupa a anthu.’ ” 3Tsiku lomwelo munthu wa Mulungu uja anapereka chizindikiro ichi: “Chizindikiro chimene Yehova wanena ndi ichi: Taonani guwali lidzangʼambika pakati ndipo phulusa lili pamenepo lidzamwazika.”

4Mfumu Yeroboamu atamva zimene munthu wa Mulungu ananena motemberera guwa lansembe ku Beteli, anatambasula dzanja lake ali ku guwako ndipo anati, “Mugwireni!” Koma dzanja limene anatambasula kuloza munthu wa Mulunguyo linawuma kuti gwaa, kotero kuti sanathenso kulibweza. 5Nthawi yomweyo guwa lija linangʼambika pakati ndipo phulusa lake linamwazika molingana ndi chizindikiro chimene munthu wa Mulungu anapereka potsata mawu a Yehova.

6Pamenepo mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Undipempherere kwa Yehova Mulungu wako kuti andikomere mtima ndipo undipempherere kuti dzanja langa lichire.” Choncho munthu wa Mulungu anapempha kwa Yehova, ndipo dzanja la mfumu linachiritsidwa nʼkukhala ngati momwe linalili kale.

7Mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya, ndipo ndidzakupatsa mphatso.”

8Koma munthu wa Mulunguyo anayankha mfumu kuti, “Ngakhale mutandipatsa theka la chuma chanu, sindingapite nanu, kapena kudya chakudya, kapenanso kumwa madzi kuno. 9Pakuti Yehova anandilamula kuti, ‘Usakadye chakudya kapena kumwa madzi kapena kubwerera podzera njira imene unayendamo kale.’ ” 10Choncho munthu wa Mulunguyo anadzera njira ina ndipo sanatsate njira imene anayendamo pobwera ku Beteliko.

11Tsono ku Beteli kunkakhala mneneri wina wokalamba. Mmodzi mwa ana ake anamufotokozera zonse zomwe munthu wa Mulungu anachita kumeneko tsiku limenelo. Anawuzanso abambo ake zimene ananena kwa mfumu. 12Abambo awo aja anawafunsa kuti, “Kodi wadzera njira iti?” Ana akewo anamufotokozera njira imene munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo anadzera. 13Ndipo abambo aja anati kwa ana akewo, “Mangireni chishalo pa bulu.” Anawo atamangirira chishalo pa bulu, nkhalambayo inakwera buluyo 14ndipo inalondola munthu wa Mulunguyo. Inamupeza atakhala pansi pa mtengo wa thundu ndipo inamufunsa kuti, “Kodi ndiwe munthu wa Mulungu amene anabwera kuchokera ku Yuda?”

Munthuyo anayankha kuti, “Inde, ndineyo.”

15Choncho mneneri wokalambayo anati kwa iye, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya.”

16Munthu wa Mulungu uja anati, “Sindingabwerere nanu kapena kudya chakudya kapenanso kumwa madzi kuno. 17Pakuti ndawuzidwa ndi Yehova kuti, ‘Usadye chakudya kapena kumwa madzi kumeneko kapenanso kubwerera poyenda njira imene unayendamo popita.’ ”

18Mneneri wokalambayo anayankha kuti, “Inenso ndine mneneri ngati iwe. Ndipo mngelo wa Yehova anayankhula nane mawu a Yehova kuti, ‘Kamubweze abwere ku nyumba yako kuti akadye chakudya ndi kumwa madzi.’ ” Koma anamunamiza. 19Choncho munthu wa Mulungu uja anabwerera naye ndipo anakadya ndi kumwa madzi mʼnyumba mwake.

20Ali pa tebulo, Yehova anayankhula ndi mneneri wokalambayo amene anamubweza munthu wa Mulunguyo. 21Iye anafuwulira munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo kuti, “Yehova akuti, ‘Iwe wanyoza mawu a Yehova ndipo sunasunge lamulo limene Yehova Mulungu wako anakupatsa. 22Iwe wabwerera ndi kudya chakudya ndiponso kumwa madzi ku malo amene Iye anakuwuza kuti usadye chakudya kapena kumwa madzi. Choncho mtembo wako sadzawuyika mʼmanda a makolo ako.’ ”

23Munthu wa Mulungu atatha kudya ndi kumwa, mneneri amene anamubweza uja anamangirira chishalo pa bulu wa munthu wa Mulunguyo. 24Akupita, anakumana ndi mkango pa msewu ndipo unamupha, mtembo wake unagwera pansi pa msewu, bulu uja anayima pambali pake ndipo mkango unayima pafupi ndi mtembowo. 25Ndipo taonani, anthu ena amene ankapita mu msewumo anaona mtembowo uli pansi potero, mkango utayima pa mbali pa mtembo uja ndipo anapita nakafotokozera anthu mu mzinda umene mumakhala mneneri wokalamba uja.

26Mneneri amene anamubweza mnzake ku njira uja atamva zimenezi, anati, “Ameneyo ndi munthu wa Mulungu amene wanyoza mawu a Yehova. Yehova wamupereka kwa mkango umene wamukhadzula ndi kumupha, monga momwe Yehova anamuchenjezera.”

27Mneneri wokalambayo anati kwa ana ake, “Mundimangire chishalo pa bulu,” ndipo anaterodi. 28Ndipo anapita, nakapezadi mtembo utagwera pansi mu msewu, bulu pamodzi ndi mkango atayima pambali pake. Koma mkangowo sunadye mtembowo kapena kukhadzula buluyo. 29Choncho mneneri wokalambayo anatenga mtembo wa munthu wa Mulunguyo, nawuyika pa bulu, ndipo anabwera nawo ku mzinda kuti alire maliro ndi kuyika mtembowo mʼmanda. 30Tsono anayika mtembowo mʼmanda amene mneneri wokalamba uja anadzikonzera, ndipo anamulira pomanena kuti, “Mʼbale wanga ine! Mʼbale wanga ine!”

31Atamuyika mʼmanda, iye anati kwa ana ake, “Ine ndikafa, mudzandiyike mʼmanda amene munthu wa Mulungu wayikidwa. Mudzayike mafupa anga pambali pa mafupa ake. 32Pakuti uthenga umene Yehova anamuyankhulitsa, wotsutsana ndi guwa lansembe la ku Beteli ndi nyumba zonse za chipembedzo za mʼmizinda ya ku Samariya, zidzachitika ndithu.”

33Ngakhale izi zinachitika, Yeroboamu sanasiye njira zake zoyipa, koma anasankhanso anthu wamba kukhala ansembe pa malo ake achipembedzo. Aliyense amene ankafuna kukhala wansembe iye anamupatula kukhala wansembe. 34Limeneli ndiye linali tchimo la nyumba ya Yeroboamu limene linabweretsa kugwa kwake ndiponso chiwonongeko mʼdzikomo.

New Russian Translation

3 Царств 13:1-34

1Когда Иеровоам стоял у жертвенника, чтобы возжечь кадильные благовония, из земель Иудеи в Вефиль, по слову Господа, пришел Божий человек. 2Он крикнул жертвеннику по слову Господа:

– Жертвенник, жертвенник! Так говорит Господь: «Родится дому Давида сын по имени Иосия. На тебе принесет он в жертву тех самых жрецов святилищ13:2 Букв.: «возвышенностей»., которые возжигают на тебе благовония, и сожжет на тебе человеческие кости»13:2 См. 4 Цар. 23:15-20. Там описывается исполнение этого пророчества..

3В тот же день Божий человек дал знамение:

– Вот знамение того, что это возвестил Господь: этот жертвенник расколется, а пепел на нем будет рассыпан.

4Услышав, что Божий человек прокричал жертвеннику Вефиля, царь Иеровоам протянул руку от жертвенника и сказал:

– Возьмите его!

Но рука, которую он протянул к тому человеку, иссохла, и он не мог повернуть ее к себе. 5А жертвенник раскололся, и пепел с него рассыпался, по знамению, что Божий человек дал по слову Господа.

6Тогда царь сказал Божьему человеку:

– Умилостиви Господа, твоего Бога, и помолись за меня, чтобы моя рука выздоровела.

Божий человек умилостивил Господа, и рука царя выздоровела и стала, как прежде. 7Царь сказал Божьему человеку:

– Пойдем ко мне в дом, подкрепись, а я одарю тебя.

8Но Божий человек ответил царю:

– Даже если бы ты давал мне половину твоего добра, я не пошел бы с тобой и не стал бы ни есть здесь хлеба, ни пить воды. 9Ведь словом Господа мне было велено: «Не ешь хлеба, не пей воды и не возвращайся тем путем, по которому идешь».

10И он пошел другой дорогой, чтобы не возвращаться тем путем, по которому пришел в Вефиль.

Непослушание пророка

11А в Вефиле жил один старый пророк, сыновья которого пришли и рассказали13:11 Так в ряде древних переводов; в нормативном еврейском тексте: «сын которого пришел и рассказал». ему обо всем, что совершил там в тот день Божий человек. Они передали отцу и то, что он сказал царю. 12Отец спросил их:

– Какой дорогой он пошел?

И сыновья показали ему, какой дорогой пошел Божий человек из земель Иудеи. 13Он сказал сыновьям:

– Оседлайте мне осла.

Когда они оседлали ему осла, он сел на него 14и поехал за Божьим человеком. Он нашел его сидящим под дубом и спросил:

– Ты ли Божий человек, который пришел из земель Иудеи?

– Я, – ответил он.

15Тогда пророк сказал ему:

– Пойдем ко мне в дом, поешь.

16Он сказал:

– Я не могу вернуться с тобой и не могу здесь ни есть хлеба, ни пить воды. 17Словом Господа мне было сказано: «Не ешь там хлеба, не пей воды и не возвращайся тем путем, по которому идешь туда».

18Старый пророк ответил:

– Я такой же пророк, как и ты. Ангел сказал мне по слову Господа: «Верни его к себе домой, чтобы он поел хлеба и попил воды». (А это была ложь.)

19И Божий человек возвратился с ним, ел и пил у него дома. 20Пока они еще сидели за столом, к старому пророку, который возвратил его, было слово Господа. 21Он закричал Божьему человеку, который пришел из земель Иудеи:

– Так говорит Господь: «Ты не послушался слова Господа и нарушил повеление, которое дал тебе Господь, твой Бог. 22Ты вернулся, ел хлеб и пил воду там, где Он запретил тебе есть и пить. Поэтому твое тело не будет погребено в гробнице твоих отцов».

23Когда Божий человек поел и попил, пророк, который возвратил его, оседлал для него осла. 24Тот ушел, но по дороге на него напал лев и убил его. Его тело лежало брошенным на дороге, а возле него стояли осел и лев. 25Люди, что проходили мимо, увидели лежащее тело и льва, стоящего возле тела. Они пошли и рассказали об этом в том городе, где жил старый пророк. 26Когда пророк, который возвратил его с пути, услышал об этом, он сказал:

– Это тот Божий человек, который не послушался слова Господа. Господь отдал его льву, который растерзал и умертвил его, как Господь и говорил ему Своим словом.

27Пророк сказал сыновьям:

– Оседлайте мне осла.

И они сделали это.

28Он вышел и нашел тело, лежавшее на дороге, возле которого стояли осел и лев. Лев же не съел тела и не растерзал осла. 29Пророк поднял тело Божьего человека, положил его на осла и привез обратно в город, чтобы оплакать и похоронить его. 30Он положил тело в свою гробницу и оплакивал его, восклицая:

– О, мой брат!

31Похоронив его, он сказал сыновьям:

– Когда я умру, похороните меня в гробнице, где погребен Божий человек; положите мои кости рядом с его костями13:31 В некоторых рукописях присутствуют слова: «чтобы мои кости сохранились с его костями».. 32Ведь то, что он возвестил по слову Господа против жертвенника Вефиля и против всех святилищ на возвышенностях в городах Самарии, непременно исполнится.

Упорство Иеровоама

33Но даже после этого Иеровоам не переменил своего злого пути и снова назначил священников из народа для святилищ на возвышенностях. Он посвящал в жрецы для святилищ на возвышенностях любого, кто хотел. 34Таков был грех дома Иеровоама, который привел его к падению и к искоренению с лица земли.