1 Mafumu 1 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 1:1-53

Adoniya Adziyika Kukhala Mfumu

1Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti. 2Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”

3Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu. 4Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.

5Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake. 6(Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).

7Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza. 8Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.

9Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda, 10koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.

11Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa? 12Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni. 13Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’ 14Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”

15Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira. 16Batiseba anagwada nalambira mfumu.

Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”

17Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’ 18Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi. 19Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni. 20Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu. 21Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”

22Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa. 23Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.

24Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu? 25Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’ 26Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane. 27Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”

Davide Alonga Ufumu Solomoni

28Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.

29Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse, 30ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”

31Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”

32Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu, 33mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’ 34Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’ 35Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”

36Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero. 37Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”

38Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni. 39Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!” 40Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.

41Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”

42Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”

43Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu. 44Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu, 45ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo. 46Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu. 47Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake, 48inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’ ”

49Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana. 50Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe. 51Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’ ”

52Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.” 53Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”

Bibelen på hverdagsdansk

1. Kongebog 1:1-53

David som en gammel mand

1På sine gamle dage døjede kong David med at holde varmen. Uanset hvor mange tæpper man lagde over ham, frøs han altid.

2Hans rådgivere sagde da til ham: „Lad os lede efter en ung pige, som kan ligge i din favn og hjælpe dig til at holde varmen.” Det syntes David var en god idé.

3-4Så gennemsøgte de landet på kryds og tværs i håb om at finde den rigtige pige, og de fandt Abishag, en smuk ung pige fra Shunem. Hende førte de til kongen, og hun tog sig kærligt af ham, men der var ikke tale om noget seksuelt forhold.

Adonija gør krav på tronen

5Adonija, som var søn af kong David og Haggit, havde store tanker om sig selv, og han ville gerne være konge efter sin far. Derfor anskaffede han sig vogn, ryttere og en livgarde på 50 mand, der skulle løbe foran ham gennem byen. 6David hverken irettesatte ham eller satte spørgsmålstegn ved, hvad han gjorde. Adonija var en flot ung mand, og nummer to i tronfølgerækken efter Absalom. 7Han allierede sig med hærføreren Joab og præsten Ebjatar, som begge lovede at hjælpe ham til magten. 8Men præsten Zadok, profeten Natan, samt Benaja, Shimi, Rei og Davids livgarde svigtede ikke kongen. De nægtede at give Adonija tilsagn om støtte.

9En dag tog Adonija af sted til den såkaldte Slangesten ved Rogelkilden lidt uden for Jerusalem, hvor han ofrede småkvæg, hornkvæg og fedekalve. Til denne selvbestaltede kroningsfest inviterede han alle sine halvbrødre undtagen Salomon, og alle de kongelige embedsmænd i Juda 10med undtagelse af profeten Natan, Benaja og kongens livgarde.

11Da gik profeten Natan til Batsheba, Salomons mor, og sagde: „Har du hørt, at Adonija har udråbt sig selv til konge, uden at David aner noget om det? 12Hvis du har dit eget og din søn Salomons liv kært, så gør som jeg siger: 13Gå straks til kong David og sig til ham: ‚Herre, lovede du mig ikke, at Salomon skulle overtage tronen efter dig? Hvorfor er Adonija så blevet udråbt til konge?’ ” 14Og Natan tilføjede: „Mens du er hos kongen, kommer jeg og bekræfter hvert eneste ord, du siger.”

15Derpå gik Batsheba ind i kongens soveværelse. David var jo meget gammel, og Abishag var hos ham. 16Batsheba bøjede sig dybt for kongen, og han spurgte: „Hvad vil du?”

17„Min herre,” svarede hun. „Du aflagde det løfte over for Herren, din Gud, at min søn Salomon skulle afløse dig på tronen. 18Men i stedet er Adonija blevet udråbt til konge uden dit vidende. 19Han har kronet sig selv og ofret en masse hornkvæg, småkvæg og fedekalve. Både Ebjatar og Joab og alle dine sønner på nær Salomon er med til festen. 20Og nu, min herre konge, venter hele Israel på at få at vide, om du virkelig har udpeget Adonija som din efterfølger. 21Hvis du ikke griber ind nu, vil Salomon og jeg blive henrettet, så snart du er død.”

22-23Mens Batsheba talte med David, ankom Natan til paladset, og tjenerne meddelte kongen: „Profeten Natan er her for at tale med dig,” Batsheba blev bedt om at gå ud, så kongen kunne høre, hvad Natan havde at sige.

Da Natan kom ind i soveværelset, bøjede han sig dybt for kongen 24og spurgte: „Herre, er det rigtigt, at du har udpeget Adonija til at blive din efterfølger? Er det ham, der skal sidde på tronen efter dig? 25I dag fejrede han kroningsfest ved at ofre en masse hornkvæg, småkvæg og fedekalve, og han inviterede dine sønner til festen sammen med Joab og Ebjatar. I dette øjeblik fester og drikker de og råber: ‚Længe leve kong Adonija!’ 26Men Zadok, Benaja, Salomon og jeg blev ikke inviteret. 27Sker det efter din befaling? Har du virkelig udpeget Adonija til tronfølger uden at sige et ord om det til dine betroede embedsmænd?”

David gør Salomon til konge

28„Kald på Batsheba!” befalede kong David sine tjenere, da Natan var gået. Så kom hun tilbage og stod foran kongen. 29Da sagde David: „Jeg lover ved den levende Gud, som trofast har hjulpet mig gennem alle farer, 30at jeg i dag vil indfri det løfte, jeg gav dig ind for Guds ansigt: Din søn Salomon skal være min efterfølger på tronen!”

31Da bøjede Batsheba sig dybt for ham og udbrød: „Gid min herre og konge må leve for evigt!”

32„Kald Zadok ind,” beordrede kongen, „også Natan og Benaja!”

Da de var kommet, 33sagde han til dem: „Tag Salomon og mine mænd med jer til Gihon, og giv Salomon mit eget muldyr at ride på. 34Dér ved Gihonkilden skal Zadok i sin egenskab af præst og Natan som profet salve ham til konge over Israels folk. Efter salvningen skal I lade blæse i vædderhornet og udråbe et længe leve for kong Salomon. 35Og når I kommer tilbage, skal I sætte ham på min kongetrone, for jeg har udpeget ham til at være konge over Israel og Juda.”

36„Amen!” svarede Benaja. „Herren, min konges Gud, vil føre det igennem! 37Gid Herren må velsigne Salomon, som han har velsignet dig—ja, må Salomons kongedømme blive endnu mægtigere end dit!”

38Så fik Zadok, Natan og Benaja fat på Salomon og lod ham ride på kongens private muldyr, og de tog alle af sted til Gihon sammen med den kongelige livgarde. 39Zadok havde hentet hornet med den hellige salveolie fra teltet, hvor arken stod, og da de kom til Gihon, hældte han olien ud over Salomons hoved. Salomon var dermed salvet til konge. Der blev blæst i vædderhornet, og folket råbte: „Længe leve kong Salomon!” 40Derpå fulgte de Salomon tilbage til Jerusalem. Undervejs spillede folk på fløjte og jublede så højt, at jorden gyngede under dem.

41I mellemtiden var Adonijas kroningsfest ved at være til ende. Gæsterne var netop ved at bryde op, da de hørte lyden af vædderhornet inde fra byen.

„Hvad sker der?” udbrød Joab. „Hvad er der på færde i byen?” 42I det samme ankom præsten Ebjatars søn, Jonatan.

„Velkommen!” sagde Adonija til Jonatan. „En mand som du kommer sikkert med gode nyheder!”

43„Desværre!” råbte Jonatan. „Kong David har netop udråbt Salomon til konge! 44-45Han gav ham sit eget private muldyr og sendte ham til Gihon sammen med Zadok, Natan og Benaja, eskorteret af den kongelige livgarde. Der salvede Zadok og Natan ham til konge. De er netop vendt tilbage fra Gihon, og byen er på den anden ende af begejstring. Det er grunden til al den larm. 46Salomon er nu indsat som konge, 47-48og hele hoffet lykønsker kong David og siger: ‚Gid din Gud må gøre Salomon endnu mere berømt end dig—og hans kongedømme endnu mægtigere end dit!’ Kongen har fra sin seng udtrykt sin taknemmelighed til Gud og sagt: ‚Lovet være Herren, Israels Gud, som i dag har gjort mig den glæde at udvælge en af mine sønner til konge efter mig!’ ”

49-50Ved de ord sprang Adonija og hans gæster panikslagne op fra bordet og flygtede for livet. Adonija skyndte sig til helligdommen og greb fat i de horn, der sad på hjørnerne af alteret.

51Salomon fik besked om, at Adonija havde søgt tilflugt ved alterets horn, og at han sagde: „Jeg bliver her, indtil Salomon sværger på, at han ikke vil slå mig ihjel.” 52Salomons reaktion var: „Hvis han vil være loyal over for mig, skal jeg ikke krumme et hår på hans hoved, men hvis han pønser på at undergrave mit kongedømme, skal han dø.” 53Så sendte kong Salomon sine mænd af sted for at hente Adonija ved alteret. Han blev ført frem for kongen og kastede sig ned foran ham med ansigtet mod jorden. Men Salomon nøjedes med at sige til ham: „Du har frihed til at gå hjem.”