1 Atesalonika 5 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Atesalonika 5:1-28

Tsiku la Ambuye

1Tsono abale, za nthawi ndi nyengo yake nʼkosafunikira kuti tikulembereni, 2chifukwa mukudziwa bwino lomwe kuti tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala usiku. 3Pamene anthu akunena kuti, “Mtendere ndi chitetezo,” chiwonongeko chidzafika pa iwo mwadzidzidzi, monga zowawa za amayi pobereka, ndipo sadzathawa.

4Koma inu abale, simuli mu mdima kuti tsiku limeneli lidzakudzidzimutseni ngati mbala. 5Nonse ndinu ana a kuwunika ndi ana a usana. Sindife anthu a usiku kapena mdima. 6Chomwecho tsono, tisafanane ndi ena amene akugona koma tikhale maso ndi odzisunga. 7Pakuti amene akugona, amagona usiku, ndi amene amaledzera, amaledzera usiku. 8Koma popeza ndife a usana, tikhale odzisunga, titavala chikhulupiriro ndi chikondi ngati chovala pachifuwa, ndi chiyembekezo cha chipulumutso ngati chipewa. 9Pakuti Mulungu sanatisankhe kuti tikavutike ndi mkwiyo koma kuti tilandire chipulumutso kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. 10Iye anatifera ndi cholinga chakuti, kaya tili ndi moyo kapena tagona, tikhale naye pamodzi. 11Choncho limbikitsanani wina ndi mnzake ndi kuthandizana kukula mu mzimu, monga momwe mukuchitira.

Malangizo Otsiriza

12Tsopano tikukupemphani abale kuti muziwalemekeza amene akugwira ntchito pakati panu, amene amakuyangʼanirani mwa Ambuye ndi amene amakulimbikitsani. 13Muziwachitira ulemu kwambiri mwachikondi chifukwa cha ntchito yawo. Mukhale pa mtendere wina ndi mnzake. 14Ndipo tikukupemphani abale, muwachenjeze amene akungokhala osagwira ntchito, alimbikitseni amanyazi, thandizani ofowoka ndipo muzilezera mtima aliyense. 15Onetsetsani kuti wina asabwezere choyipa kwa omuchitira choyipa koma nthawi zonse yesetsani kukhala okoma mtima kwa wina ndi mnzake; ndiponso ndi kwa anthu ena onse.

16Kondwerani nthawi zonse. 17Pempherani kosalekeza. 18Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu.

19Musazimitse moto wa Mzimu Woyera. 20Musanyoze mawu a uneneri. 21Yesani zinthu zonse. Gwiritsitsani chimene ndi chabwino. 22Mupewe choyipa cha mtundu wina uliwonse.

23Mulungu mwini, Mulungu wamtendere, akuyeretseni kotheratu. Mzimu wanu wonse, moyo ndi thupi zisungidwe zopanda cholakwa mpaka kubwera kwa Ambuye athu Yesu Khristu. 24Amene anakuyitanani ndi wokhulupirika ndipo Iye adzachita zimenezi.

25Abale, mutipempherere. 26Perekani moni wachikondi kwa onse. 27Pamaso pa Ambuye ndikulamula kuti kalatayi iwerengedwe kwa abale onse.

28Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale nanu.

New Serbian Translation

1. Солуњанима 5:1-28

Будите спремни за Господњи долазак

1А што се тиче времена и часа, о томе нема потребе да вам се пише. 2Ви, наиме, врло добро знате да ће дан Господњи доћи као што лопов долази ноћу. 3Кад људи буду говорили: „Мир и сигурност“, тада ће их изненада задесити пропаст, као трудови трудницу, и неће моћи да побегну.

4Али ви, браћо, нисте у тами да би вас овај дан затекао као лопов, 5јер ви сте сви синови светла и синови дана. Ми не припадамо тами и ноћи. 6Зато не спавајмо као други, већ бдијмо и будимо трезни. 7Јер, они који спавају, ноћу спавају, и који се опијају, ноћу се опијају. 8Али, пошто припадамо дану, будимо трезни, обучени у оклоп вере и љубави и с кацигом наде на спасење.

9Бог нас, наиме, није одредио да искусимо гнев, већ да добијемо спасење посредством нашег Господа Исуса Христа. 10Он је умро за нас да бисмо ми са њим живели, било да смо још живи или смо већ умрли. 11Зато, бодрите једни друге и изграђујте се међусобно, као што то већ и чините.

Последња упутства и поздрави

12Молимо вас, браћо, да поштујете оне који се труде међу вама, оне који вас, по Господњој вољи, воде и опомињу. 13Цените их изнад свега и волите због службе коју обављају. Живите међу собом у миру. 14Заклињемо вас, браћо, опомињите неуредне, бодрите малодушне, помажите слабима, будите стрпљиви са сваким. 15Гледајте да нико никоме не враћа зло за зло, него се увек трудите да чините добро једни другима и свима.

16Увек се радујте! 17Молите се без престанка! 18Захваљујте на свему, јер је то Божија воља за вас у Христу Исусу.

19Не спутавајте Духа. 20Не презирите пророштва, 21него све проверавајте, па што је добро, задржите. 22Клоните се сваког зла.

23А Бог мира нека доврши ваше посвећење, те да се цело ваше биће – дух, душа и тело – сачувају беспрекорним за долазак Господа нашег Исуса Христа. 24Веран је Бог који вас позива, он ће то и учинити.

25Браћо, молите се за нас.

26Поздравите сву браћу светим пољупцем.

27Заклињем вас пред Господом да прочитате ову посланицу свој браћи.

28Милост Господа нашега Исуса Христа с вама!