1 Atesalonika 5 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Atesalonika 5:1-28

Tsiku la Ambuye

1Tsono abale, za nthawi ndi nyengo yake nʼkosafunikira kuti tikulembereni, 2chifukwa mukudziwa bwino lomwe kuti tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala usiku. 3Pamene anthu akunena kuti, “Mtendere ndi chitetezo,” chiwonongeko chidzafika pa iwo mwadzidzidzi, monga zowawa za amayi pobereka, ndipo sadzathawa.

4Koma inu abale, simuli mu mdima kuti tsiku limeneli lidzakudzidzimutseni ngati mbala. 5Nonse ndinu ana a kuwunika ndi ana a usana. Sindife anthu a usiku kapena mdima. 6Chomwecho tsono, tisafanane ndi ena amene akugona koma tikhale maso ndi odzisunga. 7Pakuti amene akugona, amagona usiku, ndi amene amaledzera, amaledzera usiku. 8Koma popeza ndife a usana, tikhale odzisunga, titavala chikhulupiriro ndi chikondi ngati chovala pachifuwa, ndi chiyembekezo cha chipulumutso ngati chipewa. 9Pakuti Mulungu sanatisankhe kuti tikavutike ndi mkwiyo koma kuti tilandire chipulumutso kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. 10Iye anatifera ndi cholinga chakuti, kaya tili ndi moyo kapena tagona, tikhale naye pamodzi. 11Choncho limbikitsanani wina ndi mnzake ndi kuthandizana kukula mu mzimu, monga momwe mukuchitira.

Malangizo Otsiriza

12Tsopano tikukupemphani abale kuti muziwalemekeza amene akugwira ntchito pakati panu, amene amakuyangʼanirani mwa Ambuye ndi amene amakulimbikitsani. 13Muziwachitira ulemu kwambiri mwachikondi chifukwa cha ntchito yawo. Mukhale pa mtendere wina ndi mnzake. 14Ndipo tikukupemphani abale, muwachenjeze amene akungokhala osagwira ntchito, alimbikitseni amanyazi, thandizani ofowoka ndipo muzilezera mtima aliyense. 15Onetsetsani kuti wina asabwezere choyipa kwa omuchitira choyipa koma nthawi zonse yesetsani kukhala okoma mtima kwa wina ndi mnzake; ndiponso ndi kwa anthu ena onse.

16Kondwerani nthawi zonse. 17Pempherani kosalekeza. 18Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu.

19Musazimitse moto wa Mzimu Woyera. 20Musanyoze mawu a uneneri. 21Yesani zinthu zonse. Gwiritsitsani chimene ndi chabwino. 22Mupewe choyipa cha mtundu wina uliwonse.

23Mulungu mwini, Mulungu wamtendere, akuyeretseni kotheratu. Mzimu wanu wonse, moyo ndi thupi zisungidwe zopanda cholakwa mpaka kubwera kwa Ambuye athu Yesu Khristu. 24Amene anakuyitanani ndi wokhulupirika ndipo Iye adzachita zimenezi.

25Abale, mutipempherere. 26Perekani moni wachikondi kwa onse. 27Pamaso pa Ambuye ndikulamula kuti kalatayi iwerengedwe kwa abale onse.

28Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale nanu.

Luganda Contemporary Bible

1 Basessaloniika 5:1-28

15:1 a Bik 1:7 b 1Bs 4:9Naye ku bikwata ku by’entuuko n’ebiro, abooluganda, ssetaaga kwongera kubawandiikira. 25:2 a 1Ko 1:8 b 2Pe 3:10Kubanga mmwe mwennyini mumanyi bulungi nti olunaku lwa Mukama waffe lulijja ng’omubbi bw’ajja ekiro. 3Abantu balirowooza mu mitima gyabwe nti, “Tulina emirembe era tulina obukuumi,” amangwango okuzikirira ne kulyoka kubajjira, ng’okulumwa bwe kujjira omukazi agenda okuzaala omwana; ne batawona n’akatono.

45:4 Bik 26:18; 1Yk 2:8Naye mmwe, abooluganda abaagalwa temuli mu kizikiza ku nsonga zino, era temugenda kwekanga lunaku olwo ng’abayingiriddwa omubbi; 5Kubanga mmwe mwenna muli baana ba musana era baana ba butangaavu. Tetuli ba kiro yadde ab’ekizikiza. 65:6 Bar 13:11Noolwekyo tuleme kwebaka ng’abalala naye tutunulenga okwegomba kuleme okutufuga. 75:7 Bik 2:15; 2Pe 2:13Kubanga abeebaka beebaka kiro, n’abatamiira batamiira kiro. 85:8 a Bef 6:14 b Bar 8:24 c Bef 6:17Naye ffe, kubanga tuli ba musana, tulemenga okutamiira. Twambale okukkiriza n’okwagala ng’ekyomu kifuba, era tube n’essuubi ery’obulokozi nga ye nkufiira yaffe. 95:9 2Bs 2:13, 14Kubanga ffe Katonda teyatulondera kufukibwako kiruyi kya busungu, wabula okutulokola ng’ayita mu Mukama waffe Yesu Kristo, 105:10 2Ko 5:15eyatufiirira ka tube nga tuli balamu oba nga tufudde, tulyoke tubeere balamu wamu naye. 11Kale mugumyaganenga era muzimbaganenga nga bwe mubadde mukola.

Ebiragiro Ebisembayo

125:12 1Ti 5:17; Beb 13:17Kaakano tubeegayirira abooluganda, mumanye abafuba okukola emirimu mu mmwe era ababakulembera mu Mukama waffe era abababuulirira, 135:13 Mak 9:50mubassengamu nnyo ekitiibwa mu kwagala olw’omulimu gwabwe. Mubenga bantu ba mirembe. 145:14 a 2Bs 3:6, 7, 11 b Bar 14:1Tubakuutira abooluganda, mubuulirirenga abagayaavu, mugumyenga abo abalimu okutya, muyambenga abatalina maanyi, mubenga bagumiikiriza eri abantu bonna. 155:15 1Pe 3:9Mulabenga nga mu mmwe temuli muntu asasula ekibi olw’ekibi, naye bulijjo mukolenga obulungi buli muntu ne munne, era n’eri abantu bonna. 165:16 Baf 4:4Musanyukenga ennaku zonna.

Musabenga

17Musabenga obutayosa. 18Mwebazenga olwa buli kintu kyonna, kubanga ekyo Katonda ky’abaagaliza mmwe abali mu Kristo Yesu. 195:19 Bef 4:30Temuzikizanga Mwoyo Mutukuvu, 205:20 1Ko 14:1-40era temunyoomanga abo aboogera eby’obunnabbi, 215:21 1Ko 14:29; 1Yk 4:1naye mwekenneenyenga ebintu byonna, kale bwe bibanga ebirungi mubinywezenga. 22Mwewalenga buli ngeri ya kibi.

235:23 Bar 15:33Katonda ow’emirembe abatukulize ddala, era omwoyo gwammwe gwonna, n’emmeeme yammwe n’omubiri gwammwe, bikuumibwenga nga tebiriiko kya kunenyezebwa okutuusa ku lunaku olw’okujja kwa Mukama waffe Yesu Kristo. 245:24 1Ko 1:9Oyo eyabayita mwesigwa era alikituukiriza.

255:25 Bef 6:19Abooluganda, naffe, mutusabirenga.

26Mulamuse abooluganda bonna mu kulamusa okutukuvu.

27Mbalagira mu linnya lya Mukama waffe ebbaluwa eno mugisomere abooluganda bonna.

28Ekisa kya Mukama waffe Yesu Kristo kibeerenga nammwe.