1 Atesalonika 2 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Atesalonika 2:1-20

Utumiki wa Paulo ku Atesalonika

1Abale, mukudziwa kuti kudzacheza kwathu kwa inu sikunali kosapindulitsa. 2Monga mukudziwa, ife nʼkuti titazunzika ndi kunyozedwa ku Filipi. Koma mothandizidwa ndi Mulungu wathu, tinalimba mtima mpaka kukulalikirani uthenga wake wabwino ngakhale ambiri ankatsutsana nafe. 3Pakuti kulalikira kumene tikuchita, sitikuchita ndi maganizo olakwika kapena zolinga zoyipa, kapenanso kufuna kukunamizani. 4Koma timayankhula monga anthu ovomerezeka ndi Mulungu ndi osungitsidwa Uthenga Wabwino. Ife sitikufuna kukondweretsa anthu koma Mulungu, amene amasanthula mitima yathu. 5Monga mukudziwa kuti sitinagwiritse ntchito mawu oshashalika kapena mtima wofuna phindu, Mulungu ndiye mboni yathu. 6Ife sitinafune kutamidwa ndi anthu, kapena ndi inu, kapena wina aliyense mwa inu. 7Ngati atumwi a Khristu tikanatha kukhala cholemetsa kwa inu, mʼmalo mwake tinali ngati ana aangʼono pakati panu.

Monga mmene amayi amasamalira ana awo angʼono, 8moteronso tinakusamalirani. Chifukwa tinakukondani kwambiri, tinali okondwa kugawana nanu osati Uthenga Wabwino wa Mulungu wokha, komanso miyoyo yathu. 9Abale, pakuti mukumbukira kugwira ntchito kwathu kwambiri ndi kuvutika; ife tinagwira ntchito usana ndi usiku ndi cholinga chakuti tisakhale cholemetsa, kwa aliyense pamene ife tinkalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu kwa inu.

10Inu ndinu mboni, ndiponso Mulungu, kuti tinali oyera mtima, olungama ndi wopanda chifukwa pakati panu amene munakhulupirira. 11Monga mudziwa kuti ife tinkasamala aliyense wa inu monga abambo amasamalira ana ake, 12kulimbikitsa, kutonthoza ndi kukupemphani kuti mukhale moyo oyenera Mulungu amene anakuyitanani kuti mulowe mu ufumu wake ndi ulemerero.

13Ndipo ifenso tikuyamika Mulungu kosalekeza chifukwa mutalandira Mawu a Mulungu, amene munawamva kuchokera kwa ife, munawalandira osati ngati mawu a anthu, koma monga momwe alili, Mawu a Mulungu, amene akugwira ntchito mwa inu amene mukhulupirira. 14Pakuti inu abale, munakhala otsanzira mipingo ya Mulungu ya ku Yudeya, imene ili mwa Khristu Yesu. Munasautsidwa kuchokera kwa anthu a mtundu wanu, zinthu zomwezo zimene mipingo imeneyi inasautsidwa ndi Ayuda, 15amene anapha Ambuye Yesu ndi aneneri ndipo anatithamangitsanso ife. Iwo sakondweretsa Mulungu ndipo amadana ndi anthu onse 16ndikutiretsa ife kuti tisayankhule ndi a mitundu ina kuti angapulumuke. Motero iwo amadziwunjikira okha machimo awo. Mkwiyo wa Mulungu wa afikira tsopano.

Paulo Afunitsitsa Kuonanso Atesalonika

17Koma abale, titasiyana kwa nthawi pangʼono (mʼthupi osati mʼmaganizo), tinayesetsa koposa kuti tikuoneni. 18Pakuti ife tinafuna kubweranso kwa inu, makamaka ine Paulo, ndinayesa kangapo koma Satana anatiletsa. 19Nanga chiyembekezo chathu, chimwemwe chathu kapena chaufumu chimene ife tidzanyadira pamaso pa Ambuye athu Yesu Khristu pamene abwere ndi chiyani? Kodi si inu? 20Indedi, inu ndinu ulemerero wathu ndi chimwemwe.

Knijga O Kristu

1 Solunjanima 2:1-20

Pavao se sjeća posjeta Solunjanima

1Znate i sami, draga braćo i sestre, da naš dolazak k vama nije bio uzaludan. 2Znate da su nas prije toga u Filipima zlostavljali i izvrgnuli ruglu. Ipak smo se odvažili, pouzdajući se u Boga, propovijedati vam evanđelje, iako uz tešku borbu. 3Vidite dakle da u našemu propovijedanju nema govora o zabludi, nečistim pobudama ili prijevari.

4Navješćujemo Radosnu vijest upravo onako kako nam je Bog povjerio da činimo. Ne trudimo se ugoditi ljudima, nego Bogu koji proniče srca. 5Nikada vas nismo pokušali pridobiti laskanjem. Bog nam je svjedok i da nikada ništa nismo činili iz pohlepe. 6Niti smo od ljudi tražili slavu—ni od vas ni od bilo koga drugoga. 7Mogli smo od vas kao Kristovi apostoli što i zahtijevati, ali nismo. Bili smo prema vama blagi poput majke koja s ljubavlju njeguje svoju djecu. 8Toliko smo vas voljeli da smo vam htjeli predati ne samo Božju Radosnu vijest nego i vlastiti život.

9Pa sjećate se, draga braćo i sestre, našega teškog truda i umora! Dok smo vam propovijedali evanđelje, radili smo noću i danju da nikomu od vas ne budemo na teret. 10I vi i Bog ste nam svjedoci da smo se sveto, pravedno i besprijekorno vladali prema vama vjernicima. 11Postupali smo prema svakomu od vas kao otac prema vlastitoj djeci. 12Poticali smo vas, hrabrili i zaklinjali da živite životom dostojnim Boga koji vas je pozvao u svoje kraljevstvo da s njime dijelite njegovu slavu.

13Zato bez prestanka zahvaljujemo Bogu što Božju poruku koju smo vam navijestili niste primili kao ljudsku, nego kao Božju riječ, što ona uistinu i jest. A ona djeluje u vama koji vjerujete.

14Vi ste, draga braćo, pretrpjeli od svojih sunarodnjaka progonstvo te ste tako prošli jednako kao i članovi Božjih kršćanskih crkava u Judeji, koje su zbog vjere u Krista Isusa progonili njihovi vlastiti sunarodnjaci, Židovi. 15Oni su poubijali vlastite proroke, pa čak i Gospodina Isusa. Nas su žestoko progonili. Ne ugađaju Bogu i neprijatelji su svim ljudima 16jer nam priječe propovijedati poganima da se oni ne bi spasili. Navršili su tako mjeru svojih zlodjela. Navukli su na sebe najveći Božji gnjev.

Timotejeva pohvala Crkvi

17Draga braćo, pošto smo zakratko bili odvojeni od vas (ali ne i srcem), vruće smo čeznuli za vama te smo pokušali doći da vas vidimo. 18Zaista smo nastojali doći k vama, ja Pavao i više puta, ali Sotona nas je spriječio. 19Tko će, na koncu, biti naša nada i radost, naš ponos i naša nagrada pred našim Gospodinom Isusom kada opet dođe? 20Vi ste naša slava i naša radost!