1 Akorinto 4 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Akorinto 4:1-21

Atumiki a Khristu

1Choncho tsono anthu atione ife monga atumiki a Khristu, ndiponso ngati osunga zinsinsi za Mulungu. 2Chofunika kwambiri nʼchakuti amene apatsidwa udindo oyangʼanira aonetse kukhulupirika. 3Ine ndilibe nazo kanthu ngati ndiweruzidwa ndi inu kapena khothi lina lililonse. Ndithu, inenso sindidziweruza ndekha. 4Chikumbumtima changa sichikunditsutsa, koma sikuti ndine wolungama. Wondiweruza ine ndi Ambuye. 5Chomwecho musaweruze nthawi yoweruza isanakwane. Dikirani mpaka Ambuye atabwera. Iye adzaonetsa poyera zimene zabisika mu mdima ndipo adzaonetsa maganizo a mʼmitima ya anthu. Pa nthawi imeneyo aliyense adzalandira kwa Mulungu chiyamiko.

6Tsono abale, ndapereka chitsanzo cha ine mwini ndi Apolo kuti mupindule. Phunzirani kwa ife tanthauzo la mawu akuti, “Musamapitirire zimene Malemba akunena,” kuti musamanyade pamene wina aposa mnzake. 7Pakuti ndani amakusiyanitsani ndi wina aliyense? Nʼchiyani muli nacho chimene simunalandire? Ndipo ngati munalandira, bwanji mumadzitukumula ngati kuti simunalandire?

8Inu muli nazo kale zonse zimene mufuna! Inu mwalemera kale! Inu mwayamba kale kulamulira ife! Ndilakalaka mukanakhaladi mafumu kuti ife tikhale nawo mafumu pamodzi ndi inu. 9Pakuti kwa ine zikuoneka ngati kuti Mulungu watiyika ife atumwi pachionetsero, kumapeto kwa mndandanda, monga anthu oweruzidwa kuti akaphedwe mʼmabwalo. Ife tayikidwa kuti tionekere ku dziko lonse, kwa angelo ndi anthu. 10Ife ndife opusa chifukwa cha Khristu, koma inu ndinu anzeru mwa Khristu! Ife ndife ofowoka koma inu ndinu amphamvu! Inu ndinu olemekezeka koma ife ndife opeputsidwa! 11Mpaka pano tili ndi njala ndi ludzu, tili ndi sanza, tikuzunzidwa, tilibe nyumba. 12Timagwira ntchito molimbika ndi manja athu. Akamatitemberera, ife timadalitsa; tikasautsidwa, ife timapirira. 13Pamene atilalatira timayankha mwachifundo. Mpaka pano takhala ngati zinyalala za dziko, monga zakudzala za dziko lapansi.

Pempho ndi Chenjezo

14Sindikulemba izi kuti ndikuchititseni manyazi, koma kukuchenjezani monga ana anga okondedwa. 15Ngakhale muli ndi anthu 10,000 okutsogolerani mwa Khristu, mulibe abambo ambiri, popeza mwa Khristu Yesu, ine ndakhala abambo anu kudzera mu Uthenga Wabwino. 16Chifukwa chake ndikukupemphani kuti munditsanze ine. 17Chifukwa cha ichi ndikutumiza kwa inu Timoteyo, mwana wanga amene ndimamukonda, amene ndi wokhulupirika mwa Ambuye. Adzakukumbutsani inuyo za moyo wanga mwa Khristu Yesu, umene ukugwirizana ndi zimene ndimaphunzitsa paliponse mu mpingo uliwonse.

18Ena mwa inu mukudzitukumula, ngati kuti sindingabwere kwanu. 19Koma ndibwera kwanuko posachedwapa, ngati Ambuye alola, ndipo ndi pamene ndidzadziwe osati zimene anthu odzitukumulawa akuyankhula, koma kuti mphamvu zawo nʼzotani. 20Pakuti ufumu wa Mulungu si mawu chabe koma mphamvu. 21Kodi musankha chiyani? Kodi ndidzabwere ndi chikwapu, kapena mu chikondi ndiponso mwa mzimu wofatsa?

New Russian Translation

1 Коринфянам 4:1-21

Основатель церкви дает наставления членам церкви

1Итак принимайте нас как служителей Христа, которым были вверены тайны Божьи. 2От тех, кому оказано такое доверие, требуется верность. 3Меня очень мало заботит, как вы или кто-то другой будет обо мне судить. Я и сам не сужу себя. 4Совесть моя чиста, хотя не это оправдывает меня. Но мой судья – Господь. 5Поэтому ни о чем не судите заранее, но ждите возвращения Господа. Он все тайное сделает явным и обнажит скрытые намерения человеческих сердец, и тогда каждый получит от Него похвалу.

6Я говорю это, братья, обо мне и об Аполлосе ради вашего блага, чтобы вы на нашем примере постигли, что означает изречение: «Ничего сверх того, что написано», и чтобы вы не хвастались кем-то одним, ставя его выше другого. 7Кто же делает тебя лучше других? Что у тебя есть своего, чего бы ты не получил от Бога? Если ничего такого нет, то что же ты хвалишься подаренным?

8У вас уже все есть! Вы уже богаты! Вы без нас стали править! О, как бы я хотел, чтобы вы действительно правили, и тогда мы могли бы править вместе с вами! 9Потому что мне кажется, что Бог выставил нас, апостолов, как последних из людей, как осужденных на смертную казнь, на всеобщее обозрение. Мы стали зрелищем для мира, для ангелов и для людей. 10Мы стали «глупцами» ради Христа, вы же «мудрецы» во Христе! Мы «слабы», а вы – «сильны»! Вас прославляют, а нас бесчестят! 11Мы по-прежнему испытываем голод и жажду, отсутствие одежды и терпим побои, у нас нет жилья, 12мы тяжело работаем своими руками. Когда нас проклинают, мы в ответ благословляем; нас преследуют, а мы терпим. 13О нас говорят самое плохое, а мы отвечаем добром. До сегодняшнего дня мы как отбросы общества, всеми презираемые.

14Я пишу это не для того, чтобы устыдить вас, нет, я хочу вас предупредить как моих любимых детей. 15Хотя у вас тысячи учителей во Христе, у вас, все же, не много отцов. Я же стал вашим отцом через Радостную Весть об Иисусе Христе. 16Поэтому умоляю вас: следуйте моему примеру. 17Для этого я и посылаю к вам Тимофея, моего дорогого и верного сына в Господе. Он напомнит вам о моем образе жизни в Иисусе Христе, которому я учу везде, в каждой церкви.

18Некоторые из вас возгордились, полагая, что я не приду к вам. 19Но я скоро приду к вам, если на то будет воля Господа, и тогда узнаю, чего стоят не слова этих гордецов, а их сила. 20Потому что Царство Божье проявляется не в слове, а в силе. 21Выбирайте сами: прийти мне с розгой или же с любовью и в духе кротости?