1 Akorinto 2 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Akorinto 2:1-16

1Pamene ndinabwera kwa inu, abale, sindinabwere ndi luntha lodziwa kuyankhula kapena nzeru zapamwamba pamene ndinachitira umboni chinsinsi cha Mulungu. 2Pakuti ndinatsimikiza pamene ndinali ndi inu kuti ndisadziwe kanthu kena kupatula Yesu Khristu wopachikidwayo. 3Ndinabwera kwa inu wofowoka ndi wamantha, ndiponso wonjenjemera kwambiri. 4Uthenga ndi ulaliki wanga sunali wa mawu anzeru ndi onyengerera koma woonetsa mphamvu za Mzimu, 5kuti chikhulupiriro chanu chisatsamire pa nzeru ya anthu koma pa mphamvu za Mulungu.

Nzeru Yochokera kwa Mzimu

6Komabe ife timayankhula uthenga wa nzeru kwa okhwima, koma osati ndi nzeru ya mʼbado uno kapena ya olamula a mʼbado uno, amene mphamvu yawo ikutha. 7Ayi, ife timayankhula za nzeru yobisika ya Mulungu, nzeru imene inabisidwa ndipo imene Mulungu anatikonzera mu ulemerero wathu isanayambe nthawi. 8Palibe olamulira aliyense wa mʼbado uno amene anamumvetsetsa popeza anakamumvetsetsa sakanamupachika Ambuye wa ulemerero. 9Komabe monga zalembedwa kuti,

“Palibe diso linaona,

palibe khutu linamva,

palibe amene anaganizira,

zimene Mulungu anakonzera amene amukonda”

10koma Mulungu waululira ife mwa Mzimu wake.

Mzimu amafufuza zinthu zonse, ndi zozama za Mulungu zomwe. 11Kodi ndani mwa anthu angadziwe maganizo a munthu wina, kupatula mzimu wa munthuyo wokhala mʼkati mwake? Chimodzimodzinso palibe amene adziwa maganizo a Mulungu kupatula Mzimu wa Mulunguyo. 12Mzimu amene tinalandira ife si wa dziko lapansi koma Mzimu wochokera kwa Mulungu wotipatsa ife mwaulere. 13Izi ndi zimene timayankhula osati mʼmawu wophunzitsidwa ndi nzeru za munthu koma mʼmawu wophunzitsidwa ndi Mzimu, kufotokozera zoonadi zauzimu mʼmawu auzimu. 14Munthu wopanda Mzimu savomereza zinthu zimene zichokera kwa Mzimu wa Mulungu, popeza ndi zopusa kwa iyeyo, ndipo sangazimvetsetse chifukwa zimazindikirika mwa Mzimu. 15Munthu wauzimu amaweruza pa zinthu zonse, koma iye mwini saweruzidwa ndi munthu aliyense. 16Pakuti

“Ndani anadziwa malingaliro a Ambuye,

kuti akhoza kumulangiza Iye.”

Koma tili nawo mtima wa Khristu.

New Russian Translation

1 Коринфянам 2:1-16

Проповедь в силе Духа

1Братья, когда я пришел к вам, чтобы возвещать о тайне Божьей, то мои слова не отличались ни красноречием, ни особой мудростью. 2Находясь среди вас, я решил не знать ничего, кроме Иисуса Христа, и притом распятого. 3Я пришел к вам слабым, полным страха и трепета. 4И моя весть и моя проповедь были не в убедительных словах человеческой мудрости, но в проявлении силы Духа, 5чтобы ваша вера основывалась не на мудрости человеческой, а на силе Божьей.

Мудрость от Духа

6Мудрость же мы возвещаем среди людей духовно зрелых, но это не мудрость этого мира и не мудрость преходящих властителей этого мира. 7Нет, мы говорим о тайной мудрости Божьей, которая до сих пор была скрыта, но еще до сотворения мира предназначена Им для нашей славы. 8Те, кому принадлежит власть в этом мире, не поняли ее, иначе они не распяли бы Господа славы. 9Но как написано:

«Не видел глаз,

не слышало ухо,

и не приходило на сердце человеку то,

что Бог приготовил любящим Его»2:9 См. Ис. 52:15; 64:4..

10Нам же Бог открыл это Духом Своим, потому что Духу известно все. Он проникает во все глубины премудрости Божьей. 11Кто может знать мысли человека, кроме его собственного духа, живущего в нем? Так же и замыслов Бога никто не знает, кроме Духа Божьего.

12Мы же получили не дух этого мира, а Духа от Бога, чтобы нам понять все дарованное нам Богом. 13Об этом мы возвещаем не словами человеческой мудрости, но словами, которым нас научил Дух. Мы объясняем духовные истины словами, которым нас учит Дух. 14Недуховный человек не принимает того, что приходит от Духа Божьего. Он считает это глупостью и не может понять, потому что об этом можно судить только духовно. 15Духовный же человек может судить обо всем, тогда как о нем никакой человек судить не может, 16потому что

«кто постиг разум Господа,

чтобы советовать Ему?»2:16 Ис. 40:13.

Мы же имеем разум Христов.