馬太福音 22 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

馬太福音 22:1-46

王宴客的比喻

1耶穌又用比喻對他們說: 2「天國就像一個王為兒子籌備婚宴。 3他派奴僕去請受邀的客人,可是客人都不肯赴宴。 4王再派其他奴僕去,說,『去告訴被邀請的人,我的宴席已經備好,公牛和肥畜都宰了,一切都預備妥當,來赴婚宴吧!』 5那些人卻毫不理會地走了,一個去種田,一個去做買賣, 6其餘的竟然抓住王的奴僕,把他們羞辱一番後殺了。 7王大怒,派軍隊去剿滅凶手,燒毀他們的城。

8「然後,他對奴僕說,『婚宴已預備好了,只是被邀請的人不配。 9所以你們到街頭巷尾,把所有見到的人都請來。』 10奴僕到街上把遇到的人都請了來,好人壞人都有,大廳裡滿了客人。

11「王出來會見在座的客人,發現有一個人沒有穿禮服, 12就問他,『朋友,你來這裡怎麼不穿婚宴的禮服呢?』那人無言以對。 13王便吩咐侍從,『把他手腳綁起來丟到外面的黑暗裡,讓他在那裡哀哭切齒。』」

14耶穌又說:「被邀請的人多,選上的人少。」

以納稅問題刁難耶穌

15那時,法利賽人出去策劃怎樣從耶穌的話裡找把柄陷害祂。 16他們派了自己的門徒跟希律黨人一同去問耶穌:「老師,我們知道你誠實無偽,按真理傳上帝的道,你不徇情面,不以貌取人。 17那麼請告訴我們,納稅給凱撒對不對呢?」

18耶穌看出了他們的惡意,就說:「你們這些偽君子,為什麼試探我呢? 19拿一個納稅用的錢幣來給我看。」他們就拿給祂一個銀幣。

20耶穌問他們:「上面刻的是誰的像和名號?」

21他們說:「凱撒的。」

耶穌說:「那麼,屬於凱撒的東西應該給凱撒,屬於上帝的東西應該給上帝。」 22他們聽了很驚奇,只好離開祂走了。

論復活

23同一天,不相信死人會復活的撒都該人也來問耶穌, 24說:「老師,摩西說,『如果一個人死了,沒有兒女,只留下妻子,他的兄弟就當娶嫂嫂,替哥哥傳宗接代。』 25從前,我們這裡有弟兄七人,老大結了婚,沒有孩子就死了,把妻子留給了弟弟。 26二弟、三弟一直到七弟都相繼娶了嫂嫂,都沒留下孩子。 27最後,那女人也死了。 28那麼,到復活的時候,她將是誰的妻子呢?因為他們都娶過她。」

29耶穌說:「你們弄錯了。你們不明白聖經,也不知道上帝的能力。 30因為到復活的時候,人們將不娶也不嫁,就像天上的天使一樣。

31「關於死人復活的事,難道你們沒有讀過上帝對你們說過的話嗎? 32祂說,『我是亞伯拉罕的上帝,以撒的上帝,雅各的上帝。』上帝不是死人的上帝,而是活人的上帝。」 33眾人聽到祂的教導都很驚奇。

最大的誡命

34法利賽人聽見耶穌使撒都該人無言以對,就聚集在一起。 35其中有位律法專家試探耶穌說: 36「老師,請問律法中哪一條誡命最重要呢?」

37耶穌回答說:「『你要全心、全情、全意愛主——你的上帝』, 38這是第一條也是最重要的誡命。 39第二條也相似,就是『要愛鄰如己』。 40律法和先知的全部教導都以這兩條誡命為基礎。」

基督的身分

41耶穌趁著法利賽人聚在那裡,就問他們: 42「你們對基督有何看法?祂是誰的後裔?」他們答道:「大衛的後裔。」

43耶穌說:「那麼,為什麼大衛受聖靈感動,稱祂為主呢?大衛曾說,

44『主對我主說,

你坐在我的右邊,

等我使你的仇敵伏在你腳下。』

45既然大衛稱基督為主,基督又怎麼會是大衛的後裔呢?」 46沒人能回答耶穌的問題。從此再沒有人敢用問題來刁難耶穌了。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 22:1-46

Fanizo la Phwando la Ukwati

1Yesu anayankhula nawonso mʼmafanizo, nati, 2“Ufumu wakumwamba uli ngati mfumu imene inakonzera phwando mwana wake wamwamuna. 3Anatumiza antchito ake kwa amene anayitanidwa kuphwando koma anakana kubwera.

4“Kenaka anatumiza antchito ena nati, ‘Awuzeni oyitanidwa kuti phwando lakonzedwa: ndapha ngʼombe yayimuna ndi nyama zina zonenepa ndipo zonse zakonzedwa. Bwerani ku phwando laukwati.’

5“Koma iwo sanalabadire ndipo anachoka; wina anapita ku munda wake ndi wina ku malonda ake. 6Ndipo otsalawo anagwira antchito ake, nawazunza ndi kuwapha. 7Mfumu inakwiya. Inatumiza asilikali ake ndipo anawononga opha anzawowo ndi kutentha mzinda wawo.

8“Pamenepo anati kwa antchito ake, ‘Phwando laukwati lakonzedwa, koma amene ndinawayitana sanali oyenera. 9Pitani ku mphambano za misewu ndipo kayitaneni aliyense amene mukamupeze kuti abwere ku phwando.’ 10Pamenepo antchitowo anapita ku misewu nakasonkhanitsa anthu onse amene anakawapeza, abwino ndi oyipa omwe, ndipo nyumba ya madyerero inadzaza ndi oyitanidwa.

11“Koma pamene mfumu inabwera kudzaona oyitanidwawo, inaona munthu amene sanavale zovala zaukwati. 12Inamufunsa kuti, ‘Bwenzi walowa bwanji muno wopanda zovala zaukwati?’ Munthuyo anakhala chete.

13“Pamenepo mfumuyo inawuza otumikira kuti, ‘Mʼmangeni manja ndi miyendo, ndipo muponyeni kunja, ku mdima kumene kudzakhale kulira ndi kukuta mano.’

14“Popeza oyitanidwa ndi ambiri koma osankhidwa ndi ochepa.”

Za Kupereka Msonkho

15Kenaka Afarisi anatuluka nakakonza njira zomupezera zifukwa Yesu mʼmawu ake. 16Anatumiza ophunzira awo kwa Iye pamodzi ndi Aherodia. Anati, “Aphunzitsi, tidziwa kuti ndinu wangwiro ndi kuti mumaphunzitsa mawu a Mulungu monga mwa choonadi. Simutekeseka ndi anthu, popeza simusamala kuti kodi ndi ndani? 17Tiwuzeni tsono maganizo anu ndi otani, kodi nʼkololedwa kupereka msonkho kwa Kaisara kapena ayi?”

18Koma Yesu podziwa maganizo awo oyipa anati, “Inu achiphamaso, bwanji mufuna kundipezera chifukwa? 19Onetseni ndalama imene mumapereka msonkho.” Iwo anabweretsa dinari, 20ndipo anawafunsa kuti, “Kodi chithunzi ichi ndi malemba awa ndi za ndani?”

21Iwo anayankha kuti, “Ndi za Kaisara.”

Pamenepo anawawuza kuti, “Perekani kwa Kaisara zake za Kaisara, ndi kwa Mulungu zake za Mulungu.”

22Atamva izi, anadabwa, ndipo anamusiya Iye, nachoka.

Ukwati ndi za Kuuka kwa Akufa

23Tsiku lomwelo Asaduki amene amati kulibe za kuukanso, anabwera kwa Iye ndi funso. 24Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatiwuza kuti munthu akamwalira wosasiya ana, mʼbale wake akuyenera kukwatira mkazi wamasiyeyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo. 25Tsopano panali abale asanu ndi awiri pakati pathu. Woyambayo anakwatira ndipo anamwalira, ndipo popeza analibe ana, mʼbale wake analowa chokolo. 26Izi zinachitikiranso mʼbale wa chiwiri ndi wachitatu mpaka wachisanu ndi chiwiri. 27Pa mapeto pake mkaziyo anamwaliranso. 28Tsopano, kodi akadzaukitsidwa adzakhala mkazi wa ndani mwa asanu ndi awiriwa popeza aliyense anamukwatirapo?”

29Yesu anayankha kuti, “Inu mukulakwitsa chifukwa simukudziwa malemba kapena mphamvu ya Mulungu. 30Anthu akadzaukitsidwa, sadzakwatira kapena kukwatiwa; adzakhala ngati angelo kumwamba. 31Koma za kuukitsidwa kwa akufa, kodi simunawerenge zimene Mulungu ananena kwa inu kuti, 32‘Ine ndine Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo?’ Iyeyo si Mulungu wa akufa koma wa amoyo.”

33Magulu a anthu atamva zimenezi, anazizwa ndi chiphunzitso chake.

Lamulo Lalikulu Koposa

34Pakumva kuti Yesu anawakhalitsa chete Asaduki, Afarisi anasonkhana pamodzi. 35Mmodzi wa iwo, katswiri wa malamulo anamuyesa Iye ndi funso ndipo anati, 36“Aphunzitsi, kodi lamulo lalikulu koposa mu malamulo ndi liti?” 37Yesu anayankha kuti, “Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse ndi moyo wako wonse ndi nzeru zako zonse. 38Ili ndi lamulo loyamba ndi loposa onse. 39Ndipo lachiwiri ndi lofanana nalo: ‘Konda mnansi wako monga iwe mwini.’ 40Malamulo onse ndi aneneri zakhazikika pa malamulo awiriwa.”

Kodi Khristu ndi Mwana wa Ndani?

41Afarisi atasonkhana pamodzi, Yesu anawafunsa kuti, 42“Kodi mukuganiza bwanji za Khristu? Ndi Mwana wa ndani?”

Iwo anayankha kuti, “Mwana wa Davide.”

43Iye anawawuza kuti, “Nanga zikutheka bwanji kuti Davide poyankhula mwa Mzimu Woyera amatchula Iye ‘Ambuye?’ Pakuti akuti,

44“Ambuye anati kwa Ambuye wanga:

‘Khala pa dzanja langa lamanja

mpaka ndiyike adani ako

pansi pa mapazi ako.’

45Ngati tsono Davide amamutchula ‘Ambuye,’ zingatheke bwanji kukhala mwana wake?” 46Panalibe wina anatha kuyankha, ndipo kuchokera pamenepo, panalibe wina anayerekeza kumufunsa funso.