約翰福音 20 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

約翰福音 20:1-31

耶穌復活

1週日清晨,天還未亮,抹大拉瑪麗亞就來到墳墓前,發現封住墓口的石頭已經挪開了。 2她趕快跑去告訴西門·彼得和耶穌所愛的那個門徒,說:「有人把主從墳墓裡搬走了,不知放到哪裡去了。」

3彼得和那個門徒聽了就出去,往墳墓那邊跑。 4兩個人一起跑,但那個門徒比彼得跑得快,所以先到了墳墓。 5他並沒有進去,只是探頭往裡看,看見細麻布還在那裡。 6西門·彼得隨後也來了,他進到裡邊,看到細麻布放在那裡, 7耶穌的裹頭巾則捲著放在另一處,沒有和細麻布放在一起。 8先到的那個門徒也進來了,看見這種情形,就信了。 9因為他們還不明白聖經上有關耶穌必要從死裡復活的話。 10然後,他們各自回家去了。

11瑪麗亞卻站在墳墓外面哭泣,邊哭邊往墳墓裡面看, 12看見兩個穿著白衣的天使分別坐在原來安放耶穌遺體的頭腳兩端。

13天使對她說:「婦人,你為什麼哭呢?」

她說:「有人把我的主搬走了,不知道放在什麼地方。」 14說完,她轉過身來,看見耶穌站在那裡,但她不知道那就是耶穌。

15耶穌問她:「婦人,你為什麼哭?你在找誰?」

瑪麗亞還以為祂是園丁,就說:「先生,如果是你把祂搬走了,請告訴我放在哪裡了,我好搬回來。」

16耶穌說:「瑪麗亞。」

瑪麗亞立即轉過頭來用希伯來話對祂說:「拉波尼!」拉波尼的意思是老師。

17耶穌說:「不要拉著我,我還沒有升到父那裡。你先去找我的眾弟兄,告訴他們我要升天去見我的父,也是你們的父;去見我的上帝,也是你們的上帝。」

18抹大拉瑪麗亞就去向門徒報訊,說:「我看見主了!」又把主對她說的話告訴門徒。

向門徒顯現

19當天晚上,即週日晚上,門徒因為害怕猶太人,把房門都關上了。忽然,耶穌來了,站在他們當中,對他們說:「願你們平安!」 20說完,讓他們看祂的手和肋旁。門徒看見主,十分歡喜。

21耶穌又說:「願你們平安。父怎樣差遣我,我也照樣差遣你們。」 22然後祂向他們吹了一口氣,說:「你們領受聖靈吧! 23你們赦免誰的罪,誰的罪就得到赦免;你們不赦免誰的罪,誰的罪就得不到赦免。」

向多馬顯現

24耶穌顯現的時候,十二個門徒中綽號「雙胞胎」的多馬不在場。 25其他門徒告訴他:「我們看見主了!」可是多馬說:「除非我親眼看見祂手上的釘痕,用手摸到祂手上的釘痕和祂的肋旁,否則我決不信。」

26過了八天,門徒又聚在一起,多馬也在,門都關著。突然耶穌來了,站在他們當中說:「願你們平安!」 27然後對多馬說:「把你的指頭放在我手上摸摸看,伸出手來摸摸我的肋旁。不要懷疑,要信!」

28多馬回答說:「我的主,我的上帝!」

29耶穌說:「你看見我才信,那些沒有看見就信的人有福了。」

30耶穌在門徒面前還行了許多神蹟,只是沒有記在這本書裡。 31而記載這些事的目的是為了使你們相信耶穌就是基督,是上帝的兒子,並且使你們這些信祂的人可以靠祂的名得到生命。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 20:1-31

Yesu Auka kwa Akufa

1Mmamawa tsiku loyamba la sabata, kukanali kamdimabe, Mariya wa ku Magadala anapita ku manda ndipo anaona kuti mwala unali utachotsedwa pa khomo la manda. 2Choncho anabwerera akuthamanga kwa Simoni Petro ndi wophunzira winayo, amene Yesu anamukonda, ndipo anati, “Iwo amuchotsa Ambuye mʼmanda, ndipo ife sitikudziwa kumene iwo amuyika Iye!”

3Choncho Petro ndi wophunzira winayo ananyamuka kupita ku manda. 4Onse awiri anathamanga pamodzi koma wophunzira winayo anamupitirira Petro, nafika ku manda moyambirira. 5Ndipo mmene anawerama nasuzumira mʼkati mwa manda anaona nsalu zili potero koma sanalowemo. 6Kenaka Simoni Petro, amene anali pambuyo pake, anafika ndi kulowa mʼmanda. Iye anaona nsaluzo zili pamenepo, 7pamodzinso ndi nsalu imene anakulungira nayo mutu wa Yesu. Nsaluyi inali yopindidwa pa yokha yosiyanitsidwa ndi inayo. 8Pomaliza wophunzira winayo, amene anafika ku manda moyambirira, analowanso mʼkati, iye anaona ndi kukhulupirira. 9(Iwo sanazindikire kuchokera mʼmalemba kuti Yesu anayanera kuuka kuchokera kwa akufa).

Yesu Aonekera kwa Mariya wa ku Magadala

10Kenaka ophunzira anabwerera ku nyumba zawo, 11koma Mariya anayima kunja kwa manda akulira. Pamene akulira, anawerama ndi kusuzumira mʼmanda 12ndipo anaona angelo awiri atavala zoyera, atakhala pamene panali mtembo wa Yesu, mmodzi kumutu ndi wina kumapazi.

13Iwo anamufunsa iye kuti, “Amayi, nʼchifukwa chiyani mukulira?”

Iye anati, “Amuchotsa Mbuye wanga, ndipo ine sindikudziwa kumene iwo amuyika.” 14Atanena izi, iye anatembenuka ndipo anaona Yesu atayima potero koma iye sanazindikire kuti anali Yesu.

15Iye anati, “Amayi, mukulira chifukwa chiyani? Ndani amene mukumufunafuna?”

Poganiza kuti anali mwini munda, iye anati, “Bwana, ngati inu mwamuchotsa, ndiwuzeni kumene mwamuyika, ndipo ine ndikamutenga.”

16Yesu anati kwa iye, “Mariya.”

Anatembenukira kwa Iye nafuwula mu Chiaramaiki kuti, “Raboni!” (kutanthauza Mphunzitsi).

17Yesu anati, “Usandigwire Ine, pakuti sindinapite kwa Atate. Mʼmalo mwake pita kwa abale anga ndikukawawuza kuti, ndikupita kwa Atate ndi kwa Atate anunso, kwa Mulungu wanga ndi Mulungu wanunso.”

18Mariya wa ku Magadala anapita kwa ophunzira ndi uthenga wakuti, “Ndamuona Ambuye!” Iye anawawuza iwo kuti Yesu ananena zinthu izi kwa iye.

Yesu Aonekera kwa Ophunzira ake Tomasi Palibe

19Madzulo a tsiku limenelo limene linali loyamba la Sabata ophunzira ake ali pamodzi, atatseka ndi kukhoma zitseko chifukwa choopa Ayuda, Yesu anabwera ndi kuyima pakati pawo nati, “Mtendere ukhale nanu!” 20Iye atatha kunena izi, anawaonetsa manja ake ndi mʼnthiti mwake. Ophunzira anasangalala kwambiri pamene anaona Ambuye.

21Yesu anatinso, “Mtendere ukhale nanu! Monga Atate anandituma Ine, Inenso ndikukutumani.” 22Ndi mawu amenewo Iye anawapumira ndipo anati, “Landirani Mzimu Woyera. 23Ngati mukhululukira aliyense machimo ake, iwo akhululukidwa; ngati simuwakhululukira, iwo sanakhululukidwe.”

Yesu Aonekera kwa Tomasi

24Koma Tomasi (otchedwa Didimo), mmodzi wa khumi ndi awiriwo, sanali ndi ophunzira pamene Yesu anabwera. 25Ophunzira enawo atamuwuza Tomasi kuti iwo anaona Ambuye, iye ananenetsa kuti, “Pokhapokha nditaona zizindikiro za misomali mʼmanja ake ndi kuyikamo chala changa mʼmene munali misomali ndi kukhudza dzanja langa mʼnthiti mwake, ine sindidzakhulupirira.”

26Patapita sabata, ophunzira ake analinso mʼnyumbamo ndipo Tomasi anali nawo. Ngakhale makomo anali otsekedwa, Yesu anabwera nayima pakati pawo, ndipo anati, “Mtendere ukhale nanu!” 27Kenaka anati kwa Tomasi, “Ika chala chako apa; ona manja anga. Tambasula dzanja lako ndi kukhudza mʼnthiti mwanga. Leka kukayika, khulupirira.”

28Tomasi anati kwa Iye, “Ambuye wanga ndi Mulungu wanga!”

29Kenaka Yesu anamuwuza kuti, “Kodi wakhulupirira chifukwa wandiona Ine? Ndi odala amene amakhulupirira ngakhale asanaone.”

Cholinga cha Uthenga Wabwino wa Yohane

30Yesu anachita zodabwitsa zambiri pamaso pa ophunzira ake zimene sizinalembedwe mʼbuku lino. 31Koma izi zalembedwa kuti mukhulupirire kuti Yesu ndi Khristu, Mwana wa Mulungu, ndi kuti mukakhulupirira mukhale nawo moyo mʼdzina lake.