約伯記 2 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

約伯記 2:1-13

約伯失去健康

1又有一天,眾天使來朝見耶和華,撒旦也在他們當中。 2耶和華問撒旦:「你從哪裡來?」撒旦答道:「我在地上到處遊走。」 3耶和華問道:「你注意到我的僕人約伯了嗎?世上沒有人像他那樣純全正直,敬畏我,遠離罪惡。雖然你鼓動我無緣無故地攻擊他、毀滅他,他仍然持守自己的純正。」 4撒旦回答說:「人會以皮換皮,為了保全生命,情願捨棄一切。 5倘若你伸手傷害他的骨和肉,他必當面褻瀆你。」 6耶和華說:「好吧,他在你手中,但要留他一命。」 7於是,撒旦從耶和華面前退去,開始加害約伯,使他從頭到腳長毒瘡。 8約伯坐在爐灰中,拿瓦片刮身體。 9他的妻子對他說:「你還要持守自己的純正嗎?不如褻瀆上帝,死掉算了!」 10約伯回答說:「你說話像個愚昧的婦人。難道我們只從上帝手裡接受祝福,卻不接受災殃嗎?」約伯遭此不幸,仍毫無怨言。

約伯的三個朋友

11約伯的三個朋友提幔以利法書亞比勒達拿瑪瑣法聽到他的不幸遭遇,便各自從家鄉動身,相約一起來探望、安慰他。 12他們遠遠地看見約伯,幾乎認不出是他,禁不住放聲大哭,各自撕裂外袍,揚起塵土,讓土落在頭上。 13他們看到約伯極其痛苦,就陪著他在地上坐了七天七夜,沒有對他說一句話。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 2:1-13

Yobu Ayesedwa Kachiwiri

1Tsiku linanso pamene ana a Mulungu anabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anabwera nawo limodzi kudzadzionetsa pamaso pa Yehova. 2Ndipo Yehova anati kwa Satana, “Kodi iwe ukuchokera kuti?”

Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”

3Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa. Ndipo iye akanalibe wangwiro, ngakhale iwe unandiwumiriza kuti ndikulole kuti umuvutitse popanda chifukwa.”

4Satana anayankha kuti, “Iye ayesedwe mʼthupi mwake. Munthu angathe kupereka zonse ali nazo malingana iyeyo ali ndi moyo. 5Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kuwononga thupi lake, ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”

6Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, iye ali mʼmanja mwako; koma moyo wake usawuchotse.”

7Choncho Satana anachoka pamaso pa Yehova napita kukazunza Yobu ndi zilonda zaululu pa thupi lake lonse. 8Pamenepo Yobu anatenga phale ndi kumadzikanda nalo atakhala pa dzala la phulusa.

9Mkazi wake anati kwa iye, “Kodi ukuwumirirabe kukhala wangwiro? Tukwana Mulungu kuti ufe!”

10Yobu anayankha kuti, “Ukuyankhula ngati mkazi wopusa. Kodi tidzalandira zokoma zokhazokha kwa Mulungu, osalandiranso zowawa?”

Mu zonsezi, Yobu sanachimwe pa zimene anayankhula.

Abwenzi Atatu a Yobu

11Abwenzi atatu a Yobu, Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama, atamva za tsoka lonse limene linamugwera iye, ananyamuka ku nyumba zawo nakumana malo amodzi mopangana kuti apite ndi kukamupepesa Yobu ndi kumutonthoza. 12Atamuona Yobuyo, iwo ali chapatalipo, sanathe kumuzindikira. Choncho anayamba kulira mokweza mawu ndipo anangʼamba mikanjo yawo ndi kuwaza fumbi pa mitu yawo. 13Tsono anakhala naye pamodzi pansi kwa masiku asanu ndi awiri, usana ndi usiku omwe. Palibe ndi mmodzi yemwe anayankhula naye, chifukwa anazindikira kuti Yobu amavutika kwambiri.