申命記 2 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

申命記 2:1-37

曠野漂流

1「之後,我們遵照耶和華的吩咐掉轉頭,沿紅海的路前往曠野,在西珥山區繞行了很久。 2後來,耶和華對我說, 3『你們在這山區繞行的日子夠了,現在轉向北方吧。 4你告訴眾人,你們將經過西珥,那裡住著你們的親屬以掃的子孫。他們懼怕你們,所以要格外謹慎, 5不要惹他們,因為我已把西珥山賜給以掃作產業,他們的土地,我一寸也不會賜給你們。 6你們吃的、喝的,都要花錢向他們買。 7你們的上帝耶和華使你們凡事蒙福,看顧著你們走過這遼闊的曠野,四十年來與你們同在,使你們一無所缺。』

8「於是,我們繞過我們親屬以掃的子孫所住的西珥,沿亞拉巴的路,經過以拉他以旬·迦別,向摩押曠野走去。 9耶和華對我說,『不可騷擾摩押人,不可與他們爭戰,因為我不會把他們的土地賜給你,我已把亞珥賜給羅得的子孫為業。』

10「從前以米人住在亞珥,他們人數眾多,像亞衲人一樣身材高大。 11以米人同亞衲人一樣也被稱為利乏音人,但摩押人稱他們為以米人。 12以前,何利人也住在西珥,但以掃的子孫消滅了他們,佔領了他們的土地,住在那裡,正如後來以色列人佔領了耶和華賜給他們的土地。 13耶和華又說,『現在,你們要動身過撒烈溪。』於是,我們過了撒烈溪。 14我們從離開加低斯·巴尼亞到穿過撒烈溪用了三十八年。期間,那一代戰士都死光了,正如耶和華的誓言。 15其實是耶和華的手攻擊他們,直到把他們從營中全部消滅。

16「所有的戰士都死後, 17耶和華對我說, 18『今天你要從亞珥繞過摩押邊境。 19亞捫人之地後,不可騷擾他們,不可與他們爭戰,因為我不會把他們的土地賜給你們,我已把那裡賜給羅得的子孫作產業。』 20那裡以前也是利乏音人住的地方,亞捫人稱利乏音人為散送冥21利乏音族人數眾多,像亞衲人一樣身材高大。耶和華消滅了他們,讓亞捫人佔領他們的土地,住在那裡。 22耶和華也曾為以掃的子孫消滅住在西珥何利人,讓他們佔據何利人的土地,住在那裡,直到今日。 23同樣,來自克里特迦斐托人消滅了迦薩附近的亞衛人,住在那裡。 24耶和華說,『起來穿過亞嫩谷,我已將亞摩利希實本西宏和他的土地交在你手中,你要攻打他,佔領他的土地。 25從今天起,我要使天下萬民在你面前驚恐萬狀,一聽到你的名字就嚇得發抖。』

擊敗希實本王

26「於是,我從基底莫曠野派使者去見希實本西宏,提出和平的建議,說, 27『請允許我們從貴國經過,我們只走大路,不會偏離。 28我們吃的喝的,都會按價向你買,只求讓我們借道經過, 29就像西珥以東人和亞珥摩押人那樣對待我們。我們只想過約旦河,去我們的上帝耶和華所賜之地。』 30希實本西宏卻拒絕我們的請求,因為我們的上帝耶和華使他頑固不化,好讓我們擊敗他,正如今日的情形。 31耶和華對我說,『看啊,我已把西宏和他的土地交給你了,去佔領那裡,奪取他的土地吧。』 32西宏率領全軍在雅雜與我們交戰。 33我們的上帝耶和華使西宏父子及其軍隊敗在我們手下,全軍覆沒。 34我們攻佔了西宏的所有城邑,將其夷為平地,殺光城中的男女老幼,一個不留, 35只留下牲畜和財物作戰利品。 36亞嫩谷邊的亞羅珥和谷中的城,直到基列的所有城邑全被我們攻克,我們的上帝耶和華把這一切都交給了我們。 37我們遵照我們的上帝耶和華的吩咐,沒有侵犯亞捫人的土地,即雅博河一帶和山區的城邑。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 2:1-37

Kuyendayenda Mʼchipululu

1Kenaka tinabwerera ndi kuyamba ulendo wolowera ku chipululu motsatira njira ya ku Nyanja Yofiira, monga mmene Yehova anatilamulira. Kwa nthawi yayitali tinayendayenda cha ku dziko la mapiri la Seiri.

2Ndipo Yehova anati kwa ine, 3“Mwazungulira mokwanira dziko la mapiri, tsopano tembenukirani kumpoto. 4Apatse anthu malamulo awa: ‘Muli pafupi kudutsa mʼchigawo cha abale anu adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Iwowa adzachita nanu mantha koma musamale kwambiri. 5Musayambane nawo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo ngakhale poti mungoyika phazi. Ndamupatsa Esau dziko lamapiri la Seiri kuti likhale lakelake. 6Inu muyenera kuwalipira ndi siliva pa chakudya chimene mudye ndi madzi amene mumwe.’ ”

7Yehova Mulungu wanu wakudalitsani mʼntchito zonse za manja anu. Iye wakuyangʼanirani pa ulendo wanu wodutsa mʼchipululu chachikulu. Yehova Mulungu wanu wakhala nanu mʼzaka makumi anayi, ndipo simunasowe kalikonse.

8Choncho tinapitiriza ulendo modutsa abale athu, adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Tinapatukira njira ya ku Araba imene imachokera ku Elati ndi Ezioni Geberi ndipo tinayenda njira ya ku chipululu cha Mowabu.

9Ndipo Yehova anati kwa ine, “Musawavutitse Amowabu kapena kuwaputa kuti muchite nawo nkhondo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo. Ndinapereka Ari kwa adzukulu a Loti ngati chuma chawo.”

10(Aemi, anthu amphamvu ndi ochuluka komanso ataliatali ngati Aanaki amakhala kumeneko. 11Ngati Aanaki, nawonso ankawayesa kuti anali Arefai, koma Amowabu ankawatcha iwo Aemi. 12Ahori amakhala ku Seiri koma adzukulu a Esau anawapirikitsa. Iwo anawononga Ahori pamaso pawo nawakhalira pamalo pawo monga Aisraeli anachitira mʼdziko limene Yehova anawapatsa ngati chuma chawo).

13Ndipo Yehova anati, “Tsopano nyamukani ndipo muwoloke Chigwa cha Zeredi.” Choncho tinawoloka chigwacho.

14Panapita zaka 38 kuchokera pa nthawi imene tinachoka ku Kadesi Barinea mpaka pamene tinawoloka Chigwa cha Zeredi. Pa nthawi imeneyi nʼkuti mʼbado wonse wa anthu ankhondowo utawonongeka ku msasa monga Yehova anawalumbirira. 15Dzanja la Yehova linatsutsana nawo mpaka wonse anathera ku msasa.

16Tsono atafa munthu wotsiriza mwa anthu ankhondowo, 17Yehova anati kwa ine, 18“Lero mudutsa malire a Mowabu ku Ari podzera ku Ari. 19Mukafika kwa Aamoni, musawavutitse kapena kuwaputa, popeza sindidzakupatsani gawo lililonse la dziko la Aamoni. Ine ndalipereka dzikoli ngati chuma kwa adzukulu a Loti.”

20(Ilinso ankaliyesa dziko la Arefai amene ankakhala kumeneko. Koma Aamoni ankawatcha iwo Azamuzumi. 21Iwo anali anthu amphamvu ndiponso ochuluka, ataliatali ngati Aanaki. Yehova anawawononga ndi kuwachotsa pamaso pa Aamoni, amene anawapirikitsa nawakhalira pa malo pawo. 22Yehova anachitanso chimodzimodzi ndi adzukulu a Esau omwe anakhazikika ku Seiri atawononga Ahori powachotsa pamaso pawo. Iwo anawapirikitsa Ahoriwo ndi kuwakhalira pamalo pawo mpaka lero. 23Ndipo za Aavi omwe ankakhala mʼmidzi yofika mpaka ku Gaza, anagonjetsedwa ndi Akafitori wochokera ku Akafitori nakhala pamalo pawo).

Kugonjetsedwa kwa Sihoni Mfumu ya ku Hesiboni

24“Tsopano nyamukani, muwoloke khwawa la Arinoni. Taona ndapereka mʼmanja mwako Sihoni Mwamori mfumu ya Hesiboni ndi dziko lake lonse. Yambapo kutenga chuma chake ndi kumenyana naye nkhondo. 25Lero lomwe lino ndidzayamba kuyika chiopsezo ndi mantha pa mitundu yonse pansi pa thambo kuti akuope. Iwowo adzamva zambiri yako ndipo adzanjenjemera ndi kuwawidwa mtima chifukwa cha iwe.”

26Ine ndinatuma amithenga kuchokera ku chipululu cha Kedemoti kupita kwa Sihoni mfumu ya Hesiboni kukanena mawu ofuna mtendere ndipo ndinati, 27“Tiloleni tidutse mʼdziko mwanu. Ife tidzangodutsa ndi msewu waukulu, ndipo sitidzapatukira kumanja kapena kumanzere. 28Mutigulitse chakudya kuti tidye ndi madzi kuti timwe pa mtengo wa siliva. Mungotilola kuti tidutse, tikuyenda pansi 29monga mmene anatichitira adzukulu a Esau okhala ku Seiri ndi Amowabu okhala ku Ari mpaka titawoloka Yorodani kufika ku dziko limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa.” 30Koma Sihoni mfumu ya Hesiboni sanalole kuti tidutse. Popeza Yehova Mulungu wanu analimbitsa mzimu wake, nawumitsa mtima wake kuti amupereke mʼmanja mwanu monga wachitira lero lino.

31Yehova anati kwa ine, “Taona ndayamba kumupereka Sihoni ndi dziko lake kwa iwe. Tsopano yamba kugonjetsa ndi kulanda dziko lake.”

32Sihoni ndi ankhondo ake atabwera kudzakumana nafe mwankhondo pa Yahazi, 33Yehova Mulungu anamupereka iye kwa ife ndipo tinankantha, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse lankhondo. 34Pa nthawi imeneyi tinamulanda mizinda yake yonse ndi kuyiwononga kwathunthu, amuna, akazi ndi ana. Palibe amene anapulumuka. 35Koma ziweto ndi zinthu zonse zimene tinalanda mʼmizinda imene tinagonjetsayo, tinazitenga kukhala zathu. 36Kuchokera ku Aroeri mʼmphepete mwa mtsinje wa Arinoni ndi ku mzinda wa ku mtsinjeko mpaka kukafika ku Giliyadi, panalibe ndi mzinda ndi umodzi omwe umene unatikanika kuwugonjetsa. Yehova Mulungu wathu anatipatsa onsewo. 37Molingana ndi lamulo la Yehova Mulungu wathu, simunalowerere dziko lililonse la Aamoni, ngakhale dera lonse la ku mtsinje wa Yaboki kapena dera lozungulira dera la ku mizinda ya ku mapiri.