民數記 13 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

民數記 13:1-33

打探迦南

1耶和華對摩西說: 2「你要派十二位首領,每個支派一位,去打探我要賜給以色列人的迦南。」 3摩西就按耶和華的吩咐,從巴蘭曠野派出了十二位首領。 4他們的名字如下:呂便支派撒刻的兒子沙姆亞5西緬支派何利的兒子沙法6猶大支派耶孚尼的兒子迦勒7以薩迦支派約色的兒子以迦8以法蓮支派的兒子何西阿9便雅憫支派拉孚的兒子帕提10西布倫支派梭底的兒子迦疊11約瑟的子孫、瑪拿西支派穌西的兒子迦底12支派基瑪利的兒子亞米利13亞設支派米迦勒的兒子西帖14拿弗他利支派縛西的兒子拿比15迦得支派瑪基的兒子臼利16以上是摩西派去打探迦南的人,他稱的兒子何西阿約書亞

17摩西派他們去打探迦南,並囑咐說:「你們先去南地,然後再進山區, 18打探那地方,看看那裡的居民是強是弱,是多是少; 19那地方是好是壞,人們住的是堅固的城池還是不設防的營地; 20土地是肥沃還是貧瘠,有沒有樹木。儘量帶些當地的果子回來。」當時是葡萄初熟的季節。

21於是,他們從曠野一直打探到哈馬口附近的利合22他們經南地到達希伯崙希伯崙城比埃及鎖安城還要早建七年,那裡住著亞衲人的子孫亞希幔示篩撻買23他們來到以實各谷,在那裡砍下一根葡萄枝,上面有一串葡萄,由兩個人用杠子抬著,又採了一些石榴和無花果。 24因為他們在那裡砍了一串葡萄,所以就稱那地方為以實各13·24 以實各」意思是「一串」。谷。

25過了四十天,他們打探完畢,返回營地。 26他們來到巴蘭曠野的加低斯摩西亞倫以色列全體會眾彙報,把當地的果子給大家看。 27他們對摩西說:「我們照你的指示打探了那地方,果然是奶蜜之鄉,這些都是那裡的果子。 28但那裡的居民很強悍,城邑又大又堅固。我們在那裡還見到亞衲人的子孫。 29亞瑪力人住在南地,人、耶布斯人和亞摩利人住在山區,迦南人住在海邊和約旦河沿岸。」 30迦勒讓站在摩西面前的民眾安靜,然後說:「我們立刻去佔領那地方吧!我們必能取勝。」 31跟他一起去打探的人卻說:「我們不能去攻打那些人,他們比我們強大。」 32他們還危言聳聽,說:「我們去打探的地方是吞吃居民之地,我們看見的人個個身材高大。 33我們在那裡看見了亞衲人的子孫,他們是巨人的後裔,我們跟他們相比就像蚱蜢,他們看我們也像蚱蜢。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 13:1-33

Kukazonda Kanaani

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Tuma anthu kuti akazonde dziko la Kanaani limene ndikupereka kwa Aisraeli. Kuchokera pa fuko lililonse utume munthu mmodzi amene ndi mtsogoleri wawo.”

3Monga mwa mawu a Yehova, Mose anawatuma kuchokera ku chipululu cha Parani. Onsewo anali atsogoleri a Aisraeli. 4Mayina awo ndi awa:

kuchokera ku fuko la Rubeni, Samuwa mwana wa Zakuri;

5kuchokera ku fuko la Simeoni, Safati mwana wa Hori;

6kuchokera ku fuko la Yuda, Kalebe mwana wa Yefune;

7kuchokera ku fuko la Isakara, Igala mwana wa Yosefe;

8kuchokera ku fuko la Efereimu, Hoseya mwana wa Nuni;

9kuchokera ku fuko la Benjamini, Paliti mwana wa Rafu;

10kuchokera ku fuko la Zebuloni, Gadieli mwana wa Sodi;

11kuchokera ku fuko la Manase (fuko la Yosefe), Gadi mwana wa Susi;

12kuchokera ku fuko la Dani, Amieli mwana wa Gemali;

13kuchokera ku fuko la Aseri, Seturi mwana wa Mikayeli;

14kuchokera ku fuko la Nafutali, Naabi mwana wa Vofisi;

15kuchokera ku fuko la Gadi, Geuweli mwana wa Maki.

16Amenewa ndiwo mayina a anthu amene Mose anawatuma kukazonda dzikolo. (Hoseya mwana wa Nuni, Mose anamupatsa dzina loti Yoswa).

17Mose atawatuma kuti akazonde Kanaani anati, “Mupite kudzera ku Negevi, mukapitirire mpaka ku dziko la mapiri. 18Mukaone dzikolo kuti ndi lotani ndi anthu okhala mʼmenemo ngati ndi amphamvu kapena ofowoka, ochepa kapena ambiri. 19Nanga dziko limene akukhalako ndi lotani? Ndi labwino kapena loyipa? Mizinda imene akukhalamo ndi yotani? Kodi ilibe malinga kapena ndi ya malinga? 20Nthaka yake ndi yotani? Yachonde kapena yopanda chonde? Kodi dzikolo lili ndi mitengo kapena lilibe mitengo? Mukayesetse kubweretsako zipatso za mʼdzikomo.” (Inali nthawi yamphesa zoyamba kupsa).

21Choncho anapita kukazonda dzikolo kuchokera ku chipululu cha Zini mpaka ku Rehobu, mopenyana ndi Lebo Hamati. 22Anapita kudzera ku Negevi ndi kukafika ku Hebroni, kumene Ahimani, Sesai ndi Talimai, ana a Anaki ankakhala. (Anamanga Hebroni zaka zisanu ndi ziwiri asanamange Zowani ku Igupto). 23Atafika ku chigwa cha Esikolo, anadulako nthambi ya mpesa ya phava limodzi la mphesa ndipo anthu awiri ananyamulizana, natenganso makangadza ndi nkhuyu. 24Malo amenewo anawatcha chigwa cha Esikolo chifukwa cha phava la mphesa limene Aisraeli anadula kumeneko. 25Patapita masiku makumi anayi, anthu aja anabwerako kokazonda dziko lija.

Kufotokoza Zomwe Anakaona

26Ndipo atabwerako anapita kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa Aisraeli onse ku Kadesi mʼchipululu cha Parani. Kumeneko anafotokozera anthu onse nawaonetsanso zipatso za mʼdzikolo. 27Anthuwo anafotokozera Mose kuti, “Tinapita ku dziko komwe munatituma. Dzikolo ndi loyenda mkaka ndi uchi ndipo zipatso zake ndi izi. 28Koma anthu amene amakhala mʼdzikomo ndi amphamvu, mizinda yawo ndi ya malinga aakulu kwambiri. Tinaonanso Aanaki kumeneko. 29Aamaleki amakhala ku Negevi, Ahiti, Ayebusi ndi Aamori amakhala mʼdziko la mapiri ndipo Akanaani amakhala pafupi ndi nyanja, mʼmbali mwa Yorodani.”

30Koma Kalebe anawakhalitsa chete anthuwo pamaso pa Mose, ndipo anati, “Tiyeni tipite ndithu ndi kutenga dzikolo, pakuti tingathe kulitenga.”

31Koma anthu aja amene anapita naye anati, “Sitingathe kulimbana ndi anthuwo popeza ndi amphamvu kuposa ifeyo.” 32Choncho anthuwo anafalitsa pakati pa Aisraeli mbiri yoyipa ya dziko lomwe anakalionalo. Iwo anati, “Dziko limene tinapita kukalizonda limawononga anthu okhala mʼmenemo. Ndipo anthu onse amene tinakawaona kumeneko ndi ataliatali. 33Kumeneko tinaona Anefili (ana a Aanaki ochokera kwa Nefili). Ifeyo timangodziona ngati ziwala mʼmaso mwawo, ndipo kwa iwo timaonekadi motero ndithu.”