歌羅西書 2 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

歌羅西書 2:1-23

1我希望你們知道,為了你們和老底嘉人,以及許多從未和我見過面的人,我是怎樣努力奮鬥的, 2為要使你們眾人心受鼓勵,聯結在愛裡,有豐富篤定的真知灼見,可以認識上帝的奧祕。這奧祕就是基督, 3一切智慧和知識都蘊藏在祂裡面。 4我講這番話是為了防止有人用花言巧語迷惑你們。 5現在,我人雖不在你們那裡,心卻和你們在一起,看到你們生活井然有序,對基督堅信不移,我很喜樂。

生活以基督為中心

6你們既然接受了基督耶穌為主,就當繼續遵從祂, 7按照你們所受的教導在祂裡面扎根成長,信心堅固,滿懷感恩。

8你們要謹慎,免得有人用空洞虛假的哲學把你們擄去。這些哲學不是出於基督,而是出於人的傳統和世俗的玄學。 9因為上帝完全的神性有形有體地蘊藏在基督裡, 10你們在基督裡得到了豐盛的生命。祂是一切執政者和掌權者的元首。

11你們也在基督裡受了非人手所行的割禮,是基督為除掉你們的罪惡本性而行的割禮。 12你們接受洗禮時已經與基督一同埋葬了,並藉著相信上帝使基督從死裡復活的大能,與基督一同復活了。 13你們從前死在過犯和未被割除的罪惡本性中,但現在上帝卻使你們與基督一同活了過來。上帝赦免了我們一切的過犯, 14撤銷了指控我們違背律法的罪狀,將它和基督一同釘在了十字架上, 15打敗了一切在靈界執政、掌權的邪惡勢力,用基督在十字架上的勝利公開羞辱牠們。

16所以,不可讓人在飲食、節期、朔日2·16 朔日」即每月初一。或安息日的事上批評你們。 17這些都不過是將來之事的影子,那真實的本體是基督。 18有些人喜歡故作謙虛,敬拜天使,沉迷於所看見的幻象,你們不要因他們而失去得獎賞的資格。他們隨從墮落的思想無故自高自大, 19沒有與身體的頭——基督聯結。全身是靠關節和筋絡維繫,從基督得到供應,按上帝的旨意漸漸成長。

20你們既然和基督一同死了,擺脫了世俗的玄學,為什麼仍像活在世俗中, 21服從「不可拿、不可嚐、不可摸」之類的規條呢? 22這些規條不過是人的戒律和說教,經不起實踐的考驗, 23看似充滿智慧,其實只不過是自創的宗教、自表謙卑、苦待己身,對於克制邪情私慾毫無用處。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Akolose 2:1-23

1Ndikufuna mudziwe kuti ndikukuvutikirani kwambiri, inuyo pamodzi ndi anzanu a ku Laodikaya, ndi ena onse amene sitinaonane maso ndi maso. 2Cholinga changa nʼchakuti alimbikitsidwe ndi kuyanjana pamodzi mʼchikondi, akhale odzaza ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndi kuti azindikire chinsinsi cha Mulungu, chimene ndi Khristu. 3Mwa Iyeyu muli chuma chonse chobisidwa cha nzeru ndi chidziwitso. 4Ndikukuwuzani zimenezi kuti wina aliyense asakunamizeni ndi kukukopani ndi mawu ake. 5Pakuti ngakhale sindili pakati panu mʼthupi, ndili nanu pamodzi mu mzimu, ndipo ndikukondwa kuona kuti mukulongosola bwino zonse ndiponso kuti chikhulupiriro chanu mwa Khristu ndi chokhazikika ndithu.

Za Moyo Weniweni mwa Khristu

6Tsono popeza munavomereza Khristu Yesu kukhala Ambuye anu, mupitirire kukhala mwa Iyeyo. 7Mukhale ozikika mizu mwa Iye, ndipo moyo wanu umangike pa Iye. Mulimbike mʼchikhulupiriro monga momwe munaphunzirira, ndipo kuyamika kwanu kusefukire.

8Musalole kuti wina aliyense akutengeni ukapolo ndi mʼnzeru zachinyengo zolongosola zinthu zozama, zomwe zimachokera ku miyambo ya anthu ndi ku maganizo awo okhudza za dziko lapansi osati kwa Khristu.

9Pakuti mʼthupi la Khristu mumakhala umulungu wonse wathunthu. 10Ndipo inunso ndinu athunthu mwa Khristu. Iye ndiye mtsogoleri wa pamwamba pa maufumu onse ndi maulamuliro wonse. 11Mwa Iye inunso munachita mdulidwe mʼthupi lanu, osati mdulidwe ochitidwa ndi manja a anthu ayi, koma ochitidwa ndi Khristu pamene anavula khalidwe lanu lauchimo lija. 12Mu ubatizo, munayikidwa mʼmanda pamodzi ndi Khristu ndi kuukitsidwa naye pamodzi, pokhulupirira mphamvu za Mulungu amene anamuukitsa kwa akufa.

13Pamene munali akufa chifukwa cha machimo anu ndi osachita mdulidwe mʼmitima mwanu, Mulungu anakupatsani moyo mwa Khristu. Iye anatikhululukira machimo athu onse. 14Anafafaniza kalata ya ngongole yathu, pomwe panali milandu yotitsutsa ife. Iye anayichotsa, nayikhomera pa mtanda. 15Ndipo atalanda zida maufumu ndi maulamuliro, Iye anawachititsa manyazi powayendetsa pamaso pa anthu onse atawagonjetsa ndi mtanda.

Ufulu Wathu

16Nʼchifukwa chake musalole wina aliyense kukuzengani mlandu chifukwa cha zimene mumadya kapena kumwa, kapena za masiku achikondwerero cha chipembedzo, za chikondwerero cha mwezi watsopano, kapena za tsiku la Sabata. 17Zimenezi ndi chithunzithunzi chabe cha zinthu zimene zikubwera, koma choonadi chenicheni chikupezeka mwa Khristu. 18Musalole kuti wina aliyense amene amakonda kudzichepetsa mwachiphamaso ndi kumapembedza angelo akulepheretseni kukalandira mphotho. Munthu woteroyu amayankhulanso mwatsatanetsatane zinthu zimene akuti anaziona mʼmasomphenya. Anthuwa ndi odzitukumula ndi fundo zopanda pake zochokera mʼmaganizo mwawo amene si auzimu. 19Iwo sakulumikizananso ndi mutu, kumene kumachokera thupi lonse, logwirizidwa ndi kumangiriridwa pamodzi ndi mʼmitsempha yake ndi mnofu, limene limakula monga mmene Mulungu afunira kuti likulire.

20Popeza munafa pamodzi ndi Khristu kusiyana nayo miyambo ya dziko lapansi lino, nʼchifukwa chiyani mukukhalanso ngati a dziko lapansi lino? Bwanji mukumvera malamulo monga awa: 21“Usagwire chakuti,” “Usalawe chakuti,” “Usakhudze chakuti?” 22Malamulo amenewa amakhudza zinthu zimene zimatha zikamagwiritsidwa ntchito, ndipo malamulo ndi zophunzitsa za anthu chabe. 23Ndithu malamulo oterewa amaoneka ngati anzeru, pakuti amalamulira anthu ambiri pa zachipembedzo ndi pa zakudzichepetsa kwa chiphamaso, ndi pa zakuzunza thupi lawo, koma alibe mphamvu zoletsa kuchita zofuna za thupilo.