撒迦利亞書 4 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

撒迦利亞書 4:1-14

金燈臺和橄欖樹

1那位與我說話的天使又來喚醒我,像喚醒睡覺的人一樣。 2他問我:「你看見了什麼?」

我說:「我看見一個純金的燈臺,上面有一個油碗,燈臺上有七盞燈,每盞燈有七個燈芯。 3燈臺旁邊有兩棵橄欖樹,左右各一棵。」 4我問與我說話的天使:「主啊,這是什麼意思?」 5他說:「你不知道嗎?」我說:「主啊,我不知道。」

6他對我說:「這是耶和華對所羅巴伯講的話。萬軍之耶和華說,『不靠權勢,不靠才能,乃靠我的靈。 7大山啊,你算什麼?你必在所羅巴伯面前化為平地。他必搬出那塊封殿頂的石頭,伴隨著歡呼聲——願恩典、恩典歸於這殿!』」

8耶和華的話又傳給了我,說: 9所羅巴伯的手奠立這殿的根基,他的手也必完成這項工程。那時你便知道是萬軍之耶和華差遣我到你們這裡來的。 10誰敢藐視這微不足道的日子?人們看見所羅巴伯手中拿著線錘時,就必歡喜。

「這七盞燈是耶和華遍察天下的眼睛。」

11我又問天使:「燈臺左右的兩棵橄欖樹是什麼意思?」 12然後我又問道:「流出橄欖油的兩個金管旁邊的兩根橄欖枝是什麼意思?」 13他說:「你不知道嗎?」我說:「主啊,我不知道。」 14他說:「這是侍立在天下之主旁邊的兩位受膏者。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zekariya 4:1-14

Choyikapo Nyale cha Golide ndi Mitengo Iwiri ya Olivi

1Kenaka mngelo amene amayankhula nane anabwerera nandidzutsa, ngati mmene amadzutsira munthu amene ali mʼtulo. 2Anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?”

Ndinayankha kuti, “Ine ndikuona choyikapo nyale, chonse chagolide ndi mbale pamwamba pake ndi nyale zoyaka zisanu ndi ziwiri, iliyonse ili ndi zibowo zisanu ndi ziwiri zolowetsera zingwe zoyatsira. 3Ndiponso pambali pake pali mitengo ya olivi iwiri, umodzi uli kumanja kwa mbaleyo ndipo winawo kumanzere.”

4Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi nʼchiyani mbuye wanga?”

5Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?”

Ndinayankha kuti, “Ayi mbuye wanga.”

6Choncho iye anandiwuza kuti, “Mawu a Yehova kwa Zerubabeli ndi awa: ‘Osati mwa nkhondo kapena ndi mphamvu, koma ndi Mzimu wanga,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.

7“Kodi ndiwe yani, iwe phiri lamphamvu? Pamaso pa Zerubabeli udzasanduka dziko losalala. Pamenepo adzabweretsa mwala wotsiriza. Akamadzawuyika pamwamba anthu adzafuwula kuti, ‘Mulungu adalitse Nyumbayi! Mulungu adalitse Nyumbayi!’ ”

8Ndipo Yehova anayankhulanso nane kuti, 9“Manja a Zerubabeli ndiwo ayika maziko a Nyumbayi; adzatsiriza ndi manja ake omwewo. Pamenepo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye anakutuma.

10“Ndani wanyoza tsiku la zinthu zazingʼono? Anthu adzasangalala akadzaona chingwe choyezera mʼmanja mwa Zerubabeli.

(“Nyale zisanu ndi ziwirizi ndi maso a Yehova, amene amayangʼanayangʼana pa dziko lapansi.”)

11Kenaka ndinafunsa mngelo uja kuti, “Kodi mitengo ya olivi iwiri ili kumanja ndi kumanzere kwa choyikapo nyalechi ikutanthauza chiyani?”

12Ndinamufunsanso kuti, “Kodi nthambi ziwiri za mtengo wa olivi zomwe zili pambali pa mipopi yodzera mafuta iwiri yagolide zikutanthauza chiyani?”

13Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?”

Ine ndinati, “Ayi mbuye wanga.”

14Choncho iye anati, “Amenewa ndi anthu awiri amene adzozedwa kuti atumikire Ambuye pa dziko lonse lapansi.”