提摩太後書 4 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

提摩太後書 4:1-22

務要傳道

1在上帝和審判活人死人的基督耶穌面前,我憑基督的顯現和祂的國鄭重囑咐你: 2無論時機好壞,都要堅持傳道,以百般的忍耐和教導督責人、警戒人、勉勵人。 3因為有一天,人們會厭倦純正的教導,耳朵發癢,尋找許多迎合他們私慾的老師。 4他們掩耳不聽真理,反而偏向無稽之談。 5然而,你要謹慎行事,不怕吃苦,專心傳道,盡忠職守。

6我的生命如同奉獻在祭壇上的酒正傾倒出來,我離世的日子快要到了。 7那美好的仗,我打過了;當跑的路,我跑完了;所信的道,我持守住了。 8從此,有公義的冠冕為我預備,按公義審判的主會在祂來的那一天把它賜給我,不但會賜給我,也會賜給所有愛慕祂顯現的人。

最後的囑咐

9請你儘快到我這裡來, 10因為底馬貪愛世界,離棄我跑到帖撒羅尼迦去了。革勒士去了加拉太提多去了撻馬太11只剩下路加一人在我身邊。你要把馬可一起帶來,因為他在傳道的工作上對我很有幫助。 12至於推基古,我派他到以弗所去了。 13你來的時候,要把我在特羅亞時留在加布的外衣帶來,也要帶來那些書卷,特別是那些羊皮卷。

14銅匠亞歷山大做了許多惡事害我,主必按他的所作所為報應他。 15你也要提防他,因為他極力反對我們所傳的道。

16我第一次在法庭申辯的時候,沒有人幫助我,眾人都離棄了我,但願他們不會因此而獲罪。 17然而主站在我身旁加給我力量,使我可以把福音清楚地傳給外族人。主把我從獅子口裡救了出來。 18主必救我脫離一切兇險,帶我進入祂的天國。願榮耀歸給上帝,直到永永遠遠。阿們!

問候

19請代我問候百基拉亞居拉,也問候阿尼色弗一家。 20以拉都留在了哥林多,我把生病的特羅非摩留在了米利都21你要儘快在冬天之前趕到這裡來。友布羅布田利奴革勞底亞和眾弟兄姊妹都問候你。

22願主與你的靈同在!願恩典與你們同在!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Timoteyo 4:1-22

1Pamaso pa Mulungu ndi pamaso pa Khristu Yesu, amene adzaweruza amoyo ndi akufa omwe pamene adzaonekera ndi ufumu wake, ndikukulamula kuti: 2Lalikira Mawu; khala wokonzeka pa nthawi yake, ngakhale pamene si pa nthawi yake. Konza zolakwa zawo, dzudzula ndipo limbikitsa moleza mtima kwambiri ndi malangizo osamalitsa. 3Pakuti idzafika nthawi imene anthu adzakana chiphunzitso choona. Mʼmalo mwake, chifukwa chokhumba kumva zowakomera zokha, adzasonkhanitsa aphunzitsi ambiri omawawuza zimene iwo akufuna kumva. 4Sadzafuna kumva choona koma adzafuna kumva nthano chabe. 5Koma iwe, khala tcheru nthawi zonse, pirira mʼzovuta, gwira ntchito ya mlaliki, gwira ntchito zonse za utumiki wako.

6Pakuti moyo wanga wayamba kale kuthiridwa ngati nsembe, ndipo nthawi yakwana yoti ndinyamuke ulendo wanga. 7Ndamenya nkhondo yabwino, ndatsiriza bwino mpikisano wa liwiro ndipo ndasunga chikhulupiriro. 8Tsopano mphotho yanga ikundidikira imene ndi chipewa cha chilungamo, imene Ambuye, woweruza wolungama, adzandipatsa pa tsiku lijalo, osati ine ndekha komanso onse amene akufunitsitsa kubwera kwake.

Ndemanga ya Paulo

9Uyesetse kubwera kuno msanga. 10Paja Dema anandisiya chifukwa chokonda dziko lapansi lino, ndipo anapita ku Tesalonika. Kresike anapita ku Galatiya ndipo Tito anapita ku Dalimatiya. 11Ndatsala ndi Luka yekha basi. Mutenge Marko ndipo ubwere naye kuno, chifukwa amandithandiza mu utumiki wanga. 12Ndatumiza Tukiko ku Efeso. 13Pobwera, unditengere chofunda pamwamba chimene ndinachisiya kwa Kupro ku Trowa. Unditengerenso mabuku anga, makamaka aja azikopawa.

14Alekisandro, mmisiri wa zitsulo anandichitira zoyipa kwambiri. Ambuye adzamubwezera pa zimene anachita. 15Iwenso ukhale naye tcheru chifukwa anatsutsa kwambiri uthenga wathu.

16Podziteteza koyamba pa mlandu wanga, panalibe ndi mmodzi yemwe amene anandithandiza, koma aliyense anandithawa. Mulungu awakhululukire. 17Koma Ambuye anayima nane limodzi, ndipo anandipatsa mphamvu, kuti kudzera mwa ine, uthenga ulalikidwe kwambiri, ndikuti anthu a mitundu ina amve. Ndipo ndinalanditsidwa mʼkamwa mwa mkango. 18Ambuye adzandilanditsa ku chilichonse chofuna kundichita choyipa ndipo adzandisamalira bwino mpaka kundilowetsa chonse mu ufumu wake wakumwamba. Kwa Iye kukhale ulemerero mpaka muyaya.

Mawu Otsiriza

19Pereka moni kwa Prisila ndi Akura pamodzi ndi banja lonse la Onesiforo. 20Erasto anatsalira ku Korinto. Trofimo ndinamusiya akudwala ku Mileto. 21Uyesetse kubwera kuno nthawi yozizira isanafike. Eubulo akupereka moni, ndiponso Pude, Lino, Klaudiya ndi abale onse nawonso akupereka moni.

22Ambuye akhale ndi mzimu wako. Chisomo chikhale ndi inu nonse.