彼得前書 5 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

彼得前書 5:1-14

勸勉長老

1我是基督受苦的見證人,將分享以後所顯明的榮耀。我以長老的身分勸你們中間作長老的: 2務要牧養上帝託付給你們的羊群,按著上帝的旨意甘心樂意地照顧他們,不是出於勉強,不是為了謀利,而是出於熱誠。 3不要辖制託付給你們的羊群,而是要做群羊的榜樣。 4等到大牧長顯現的時候,你們必得到永不衰殘的榮耀冠冕。

5你們年輕的要順服年長的,大家都要存謙卑的心彼此服侍。因為上帝阻擋驕傲的人,恩待謙卑的人。 6所以你們要在上帝大能的手下謙卑,時候到了,祂必擢升你們。 7你們要把一切憂慮卸給上帝,因為祂眷顧你們。

8你們務要謹慎,警醒,因為你們的仇敵魔鬼好像咆哮的獅子四處遊走,尋找可以吞吃的獵物。 9你們要以堅固的信心抵擋牠,要知道世界各地的弟兄姊妹在遭受同樣的苦難。 10你們忍受短暫的苦難之後,廣施恩典、在基督裡呼召你們享受祂永遠榮耀的上帝必親自復興你們,使你們剛強、篤定、堅立。 11願權能歸給祂,直到永永遠遠。阿們!

問候

12在忠心的弟兄西拉的幫助下,我簡單地寫了這封信勸勉你們,並證明這是上帝真實的恩典。你們務要在這恩典上站穩。

13巴比倫和你們一同蒙揀選的教會問候你們,我的兒子馬可也問候你們。 14你們要以愛心彼此親吻問候。

願平安歸給你們所有在基督裡的人!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Petro 5:1-14

Akulu Ampingo ndi Anyamata mu Mpingo

1Ine ndikupempha akulu a mpingo amene ali pakati panu, monga inenso mkulu mnzawo, mboni ya zowawa za Khristu ndiponso amene ndidzalandira nawo ulemerero umene uti udzaonetsedwe. 2Wetani gulu la Mulungu limene lili mʼmanja mwanu, muziliyangʼanira. Muzichita osati mowumirizidwa, koma mwakufuna kwanu, monga momwe Mulungu akufunira kuti mutero. Musachite chifukwa chadyera la ndalama, koma ndi mtima ofuna kutumikira. 3Musakhale ngati mafumu pa amene mukuwayangʼanira, koma mukhale chitsanzo kwa gululo. 4Ndipo Mʼbusa wamkulu akadzaonekera, mudzalandira chipewa cha ulemerero chosafota.

5Momwemonso, inu anyamata gonjerani amene ndi akulu. Inu nonse mukhale odzichepetsa kuti mutumikirane, chifukwa,

“Mulungu amatsutsana nawo odzikuza,

koma amapereka chisomo kwa odzichepetsa.”

6Choncho, mudzichepetse pamaso pa Mulungu wamphamvu, kuti pa nthawi yake adzakukwezeni. 7Tayani pa Iye nkhawa zanu zonse chifukwa ndiye amakusamalani.

8Khalani odziretsa ndi atcheru. Mdani wanu mdierekezi amayendayenda monga mkango wobangula kufunafuna wina kuti amumeze. 9Mukaneni iye, ndipo mukhazikike mʼchikhulupiriro, chifukwa mukudziwa kuti abale anzanu pa dziko lonse lapansi nawonso akumva zowawa zomwezi.

10Ndipo Mulungu wachisomo chonse, amene anakuyitanani ku ulemerero wake wamuyaya mwa Khristu, mutamva zowawa pa kanthawi, adzakukonzaninso ndi kukulimbitsani pa maziko olimba. 11Kwa Iye kukhale mphamvu mpaka muyaya, Ameni.

Mawu Otsiriza

12Mothandizidwa ndi Sila, amene ndi mʼbale wokhulupirika, ndakulemberani mwachidule kukulimbikitsani ndi kuchita umboni kuti ichi ndi chisomo choona cha Mulungu. 13Imani mwamphamvu mʼchisomochi. Mlongo wanu amene ali ku Babuloni, wosankhidwa pamodzi nanu akupereka moni, nayenso Marko, mwana wanga, akupereka moni. 14Mupatsane moni ndi mpsopsono wachikondi. Mtendere ukhale ndi inu nonse amene muli mwa Khristu.