彌迦書 5 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

彌迦書 5:1-15

耶和華的應許

1耶路撒冷的居民5·1 耶路撒冷的居民」希伯來文是「被圍攻的女子」。啊,

現在你們要調集軍隊!

敵人正四面圍攻我們,

要用杖擊打以色列首領的臉頰。

2以法他伯利恆啊,

你在猶大各城中毫不起眼,

但將有一位從你那裡出來,

為我統治以色列

祂的根源自亙古,來自太初。

3耶和華要將以色列人交給他們的敵人,

直到那臨盆的婦人生下兒子。

那時,祂流亡的弟兄將重返他們的以色列同胞那裡。

4祂要挺身而起,

倚靠耶和華的能力,

奉祂上帝耶和華的威名牧養祂的群羊。

他們將安然居住,

因為那時祂必受尊崇,直達地極。

5祂必給他們帶來平安!

亞述人侵略我們的國土、踐踏我們的宮殿時,

我們將選立七位牧者和八位首領抗擊他們。

6他們要用刀劍統治亞述,統治寧錄地區。

亞述人侵入我們國境、踐踏我們疆土時,

祂必拯救我們。

7雅各餘剩的子孫將在萬民中像從耶和華那裡降下的雨露,

又像灑在草上的甘霖。

他們不依靠人,

不冀望於世人。

8在各國各民中,

雅各餘剩的子孫猶如林間百獸中的獅子,

又像闖入羊群的猛獅,

將獵物撲倒撕碎,

無人能搭救。

9願你們伸手戰勝仇敵!

願你們的仇敵都被剷除!

10耶和華說:

「到那日,

我要消滅你們的戰馬,

毀壞你們的戰車。

11我要摧毀你們境內的城邑,

拆除你們所有的堡壘。

12我要除掉你們手中的巫術,

使你們那裡不再有占卜的。

13我要從你們中間除去雕刻的神像和神柱,

使你們不再跪拜自己所造的。

14我要從你們中間剷除亞舍拉神像,

毀滅你們的偶像。

15我要在烈怒中報應那些不聽從我的國家。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 5:1-15

Wolamulira Wochokera ku Betelehemu

1Iwe mzinda wa anthu ankhondo, sonkhanitsa anthu ako ankhondo,

pakuti anthu atizungulira kuti alimbane nafe.

Adzakantha ndi ndodo pa chibwano

cha wolamulira wa Israeli.

2“Koma iwe Betelehemu Efurata,

ngakhale uli wonyozeka pakati pa mafuko a Yuda,

mwa iwe mudzatuluka

munthu amene adzalamulira Israeli,

amene chiyambi chake nʼchakalekale,

nʼchamasiku amakedzana.”

3Nʼchifukwa chake Israeli adzasiyidwa

mpaka pa nthawi imene mayi amene ali woyembekezera adzachire.

Ndipo abale ake onse otsalira adzabwerera

kudzakhala pamodzi ndi Aisraeli.

4Iye adzalimbika, ndipo adzaweta nkhosa zake

mwa mphamvu ya Yehova,

mu ulemerero wa dzina la Yehova Mulungu wake.

Ndipo iwo adzakhala mu mtendere,

pakuti ukulu wake udzakhala ponseponse pa dziko lapansi.

5Ndipo Iye adzakhala mtendere wawo.

Chipulumutso ndi Chiwonongeko

Asiriya akadzalowa mʼdziko lathu

ndi kuyamba kuthira nkhondo malo athu otetezedwa,

tidzawadzutsira abusa asanu ndi awiri,

ngakhalenso atsogoleri asanu ndi atatu.

6Iwo adzagonjetsa dziko la Asiriya ndi lupanga,

dziko la Nimurodi adzalilamulira mwankhondo.

Adzatipulumutsa kwa Asiriya

akadzafika mʼmalire a mʼdziko lathu

kudzatithira nkhondo.

7Otsalira a Yakobo adzakhala

pakati pa mitundu yambiri ya anthu

ngati mame ochokera kwa Yehova,

ngati mvumbi pa udzu,

omwe sulamulidwa ndi munthu

kapena kudikira lamulo la anthu.

8Otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu ya anthu,

mʼgulu la anthu a mitundu yambiri,

ngati mkango pakati pa nyama za mʼnkhalango.

Ngati mwana wa mkango pakati pa gulu la nkhosa,

amene pozidutsa amazidya ndi kuzikhadzula,

ndipo palibe angathe kuzilanditsa.

9Mudzagonjetsa adani anu,

ndipo adani anu onse adzawonongeka.

10Yehova akuti,

“Tsiku limenelo ndidzawononga akavalo anu onse

ndi kuphwasula magaleta anu.

11Ndidzawononga mizinda ya mʼdziko mwanu

ndi kugwetsa malinga anu onse.

12Ndidzawononga ufiti wanu

ndipo sikudzakhalanso anthu owombeza mawula.

13Ndidzawononga mafano anu osema

pamodzi ndi miyala yanu yopatulika imene ili pakati panu;

simudzagwadiranso zinthu zopanga

ndi manja anu.

14Ndidzazula mitengo ya mafano a Asera imene ili pakati panu,

ndipo ndidzawononga mizinda yanu.

15Ndidzayilanga mwaukali ndi mokwiya

mitundu imene sinandimvere Ine.”