列王紀下 4 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

列王紀下 4:1-44

以利沙幫助窮寡婦

1有一個先知的妻子哀求以利沙說:「你僕人——我丈夫怎樣敬畏耶和華,你是知道的。如今他去世了,債主來取我的兩個孩子做奴隸。」 2以利沙問她:「我該怎樣幫你呢?告訴我,你家裡有什麼?」婦人答道:「婢女家什麼也沒有,只有一瓶油。」 3以利沙說:「你去向所有的鄰居借空器皿,要儘量多借一些。 4然後回家關上門,你和你兒子在屋裡把那瓶油倒在所有借來的器皿中,裝滿的放在一邊。」 5於是,婦人辭別以利沙,回去後把自己和兒子關在屋裡,兒子遞給她器皿,她就倒油。 6器皿都裝滿了,她對兒子說:「再拿個器皿給我。」兒子說:「已經沒有了。」這時,油止住了。 7婦人將經過告訴上帝的僕人,上帝的僕人對她說:「你去把油賣了還債,你們母子可以用剩下的錢度日。」

以利沙和書念婦人

8一天,以利沙路過書念,那裡一位富有的婦人挽留他吃飯。此後以利沙每次路過那裡,總到她家裡吃飯。 9那婦人對丈夫說:「我看常路過我們這裡的這位是上帝聖潔的僕人。他常路過我們這裡, 10不如我們在房頂上給他蓋一間小屋,裡面放床、桌子、椅子和燈。這樣,他來我們家時,可以在那裡休息。」

11一天,以利沙又到了那裡,便在那間小屋裡休息。 12以利沙吩咐僕人基哈西去請書念的婦人。她來了,站在以利沙面前。 13以利沙吩咐基哈西說:「你對她說,『你為我們費了不少心,我們該為你做些什麼呢?要不要我們在王或元帥面前為你說些好話呢?』」她答道:「我在本族中安居無事。」 14以利沙基哈西:「我們能為她做什麼呢?」基哈西說:「她沒有兒子,丈夫也已經老了。」 15以利沙說:「你再去請她來。」她來了,站在門口。 16以利沙對她說:「明年這時候,你必抱一個兒子。」她說:「上帝的僕人,我主啊,不要騙我。」 17那婦人果然懷了孕,在第二年的那時候生了一個兒子,應驗了以利沙對她說的話。

18孩子漸漸長大。一天,他到收割的人那裡找他父親。 19突然,他對他父親喊道:「我的頭啊!我的頭啊!」他父親見狀,立刻吩咐僕人抱他到他母親那裡。 20僕人把他抱起來,送到他母親那裡。孩子坐在母親的膝上,到中午就死了。 21他母親上樓把他放在上帝僕人的床上,關上門出來。 22她叫來丈夫,對他說:「請你預備一個僕人和一頭驢,我好趕快去見上帝的僕人,然後返回來。」 23她丈夫說:「今天不是朔日4·23 朔日」即每月初一。,也不是安息日,你為什麼要去見他?」婦人說:「平安無事。」 24她騎上驢,對僕人說:「快走吧!我不吩咐你,就不要慢下來。」

25她就去迦密山見上帝的僕人。上帝的僕人遠遠望見她,就對僕人基哈西說:「你看,書念的婦人來了! 26你跑去迎接她,問問她和她的丈夫與孩子都好嗎。」

婦人對以利沙的僕人說:「一切都好。」

27可是,她上山見到上帝的僕人後,就抱住他的腳。基哈西想要推開她,但上帝的僕人說:「由她吧!因為她心裡非常痛苦。耶和華沒有告訴我發生了什麼事。」 28婦人說:「我何嘗向我主求過兒子呢?我不是對你說不要騙我嗎?」 29以利沙吩咐基哈西:「你要束上腰帶,拿著我的杖去她家。路上不論遇見誰,都不要問候他。有人問候你,也不要作答。去把我的杖放在孩子臉上。」 30孩子的母親說:「我憑永活的耶和華和你的性命起誓,你若不同去,我決不離開你。」於是,以利沙跟她同去。 31基哈西先趕到,把杖放在孩子臉上,可是孩子一點動靜也沒有。他就回去找以利沙,路上碰見他,便說:「孩子還沒醒過來。」

32以利沙進了屋子,看見孩子死了,躺在床上, 33就關上門,向耶和華祈禱。 34禱告後,他上床伏在孩子身上,口對口,眼對眼,手對手,孩子的身體漸漸變暖了。 35然後,以利沙起來在房內來回走了一趟,又上床伏在孩子身上。孩子打了七個噴嚏,便睜開了眼睛。 36以利沙基哈西請那婦人來。婦人來了,以利沙對她說:「把你兒子抱走吧。」 37婦人進來,在以利沙腳前下拜,然後抱起兒子出去了。

用麵粉解毒

38以利沙回到吉甲,那裡正鬧饑荒。一群先知坐在他面前,他吩咐僕人把一口大鍋放在火上給他們煮湯。 39有個先知到田間摘野菜,看見一棵野瓜藤,便摘了一兜野瓜回來,切碎了放進鍋裡,卻不知道那是什麼瓜。 40湯煮好後倒出來給眾人喝,他們剛喝了一點,就叫道:「上帝的僕人啊,湯裡有毒!」他們都不敢喝了。 41以利沙說:「拿點麵粉來。」他把麵粉撒在鍋裡,說:「倒出來給眾人喝吧。」於是,湯裡沒有毒了。

用二十個餅餵飽百人

42巴力·沙利沙來了一個人,他帶了二十個用初熟大麥做的餅和一些麥穗送給上帝的僕人。上帝的僕人說:「分給眾人吃吧。」 43僕人說:「這些怎麼夠一百人吃呢?」以利沙說:「你只管分給眾人吃。因為耶和華說,『眾人都能吃飽,並且還會剩下。』」 44於是,僕人將食物擺在眾人面前,他們都吃飽了,果然還有剩餘,正如耶和華所言。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 4:1-44

Mafuta a Mkazi Wamasiye

1Mkazi wa mmodzi mwa ana a aneneri anafuwula kwa Elisa kuti, “Mtumiki wanu, mwamuna wanga wamwalira ndipo inu mukudziwa kuti ankaopa Yehova. Koma tsopano munthu amene mwamuna wanga anakongolako zinthu zake, akubwera kudzatenga ana anga awiri aamuna kuti akhale akapolo ake.”

2Elisa anayankha mayiyo kuti, “Kodi ufuna ndikuchitire chiyani? Tandiwuza uli ndi chiyani mʼnyumba mwako?”

Mayiyo anayankha kuti, “Mdzakazi wanu alibe kanthu kalikonse koma timafuta pangʼono chabe.”

3Elisa anati, “Pita kabwereke mitsuko yonse yopanda kanthu kwa anzako. Usakabwereke mitsuko yochepa. 4Kenaka ukalowe mʼnyumba mwako ndi kudzitsekera iwe ndi ana ako. Mukakatero mukakhuthulire mafuta mʼmitsuko yonseyo, ndipo mtsuko uliwonse ukadzaza muzikawuyika pambali.”

5Mayi uja anachoka kwa Elisa nakadzitsekera ndi ana ake. Anthu anabweretsa mitsuko kwa iye ndipo ankathiramo mafuta. 6Mitsuko yonse itadzaza, mayiyo anawuza mwana wake kuti, “Bweretsa mtsuko wina.”

Koma iye anayankha kuti, “Mitsuko yonse yatha.” Pamenepo mafuta analeka kutuluka.

7Mayiyo anapita nakamuwuza munthu wa Mulungu amene anamuyankha kuti, “Pita, kagulitse mafutawo ndipo ukabweze ngongole ija. Ndalama zotsalazo zikakhale zako ndi ana ako.”

Elisa Aukitsa Mwana wa Mayi wa ku Sunemu

8Tsiku lina Elisa anapita ku Sunemu. Kumeneko kunkakhala mayi wina wachuma amene anawumiriza Elisa kuti adye chakudya. Choncho nthawi iliyonse imene Elisa amadutsa kumeneko, ankayima ndi kudya. 9Mayiyo anawuza mwamuna wake kuti, “Taonani, ine ndikudziwa kuti munthu amene amadutsa pano nthawi zambiriyu ndi munthu woyera wa Mulungu. 10Tiyeni timumangire kachipinda kakangʼono pa denga la nyumbayi ndi kumuyikiramo bedi ndi tebulo, mpando ndi nyale. Akabwera kuno azikhala mʼmenemo.”

11Tsiku lina pamene Elisa anafika ku Sunemu, iye anakalowa mʼchipinda chake chija nagona mʼmenemo. 12Iye anati kwa mtumiki wake Gehazi, “Muyitane Msunemuyu.” Ndipo anapita kukamuyitana mayiyo, ndipo anabwera nayima pamaso pa Elisa. 13Elisa anati kwa Gehazi, “Muwuze mayiyo kuti, ‘Wavutika potichitira zonsezi. Nanga tsopano ifeyo tikuchitire chiyani? Kodi ukufuna kuti tikadziwitse mfumu kapena mtsogoleri wa ankhondo zimene watichitirazi?’ ”

Mayiyo anayankha kuti, “Ine ndimakhala mwamtendere pakati pa abale anga.”

14Elisa anafunsanso Gehazi kuti, “Kodi tingamuchitire chiyani?”

Gehazi anati, “Ndithu, mayiyu alibe mwana ndipo mwamuna wake ndi wokalamba.”

15Pamenepo Elisa anati, “Muyitane.” Choncho Gehazi anamuyitana, ndipo iye anabwera nayima pa khomo. 16Elisa anati kwa mayiyo, “Nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, udzakhala utanyamula mwana wamwamuna mʼmanja mwako.”

Mayiyo anatsutsa zimenezi nanena kuti, “Ayi mbuye wanga. Inu munthu wa Mulungu, musanamize mdzakazi wanu!”

17Koma mayi uja anakhala woyembekezera, ndipo chaka chotsatiracho, nthawi ngati yomweyo anabereka mwana wamwamuna monga momwe Elisa anamuwuzira.

18Mwana uja anakula, ndipo tsiku lina anapita kwa abambo ake amene anali ndi anthu odula tirigu. 19Mwanayo anafuwula kwa abambo ake kuti, “Mayo! Mutu wanga ine! Mayo! Mutu wanga ine!”

Abambo akewo anawuza wantchito wake kuti, “Munyamule ndi kukamupereka kwa amayi ake.” 20Wantchito uja atamunyamula ndi kumupereka kwa amayi ake. Mwanayo anakhala pa miyendo ya amayi akeyo mpaka masana, ndipo pambuyo pake anamwalira. 21Mayiyo ananyamula mwanayo nakamugoneka pa bedi la munthu wa Mulungu uja. Kenaka anatseka chitseko iye nʼkuchokapo.

22Iye anayitanitsa mwamuna wake namuwuza kuti, “Tumizireni wantchito mmodzi ndi bulu mmodzi kuti ndipite mofulumira kwa munthu wa Mulungu nʼkubwererako.”

23Mwamuna wakeyo anafunsa kuti, “Chifukwa chiyani ukupita kwa iyeyo lero? Lero si tsiku la Chikondwerero cha Mwezi Watsopano kapena tsiku la Sabata.”

Mayiyo anayankha kuti, “Zonse zili bwino.”

24Mayiyo anamangirira chishalo pa bulu ndipo anawuza wantchito wake kuti, “Yendetsa bulu mofulumira. Usachepetse liwiro pokhapokha nditakuwuza.” 25Choncho ananyamuka nakafika kwa munthu wa Mulungu uja ku Phiri la Karimeli.

Munthu wa Mulungu ataona mayiyo patali, anawuza mtumiki wake Gehazi kuti, “Taona! Msunemu uyo! 26Thamanga msanga ukakumane naye ndipo ukamufunse kuti, ‘Kodi muli bwino? Kodi mwamuna wanu ali bwino? Kodi mwana wanu ali bwino?’ ”

Mayiyo anayankha kuti, “Zonse zili bwino.”

27Atafika kwa munthu wa Mulunguyo pa phiripo, mayiyo anagwira mapazi a Elisa. Gehazi anabwera kuti amukankhe, koma munthu wa Mulungu anati, “Musiye! Iyeyu ali pa mavuto aakulu, koma Yehova wandibisira zimenezi ndipo sanandiwuze chifukwa chake.”

28Tsono mayiyo anati, “Mbuye wanga, kodi ine ndinakupemphani mwana? Kodi sindinakuwuzeni kuti musandinamize?”

29Elisa anawuza Gehazi kuti, “Manga lamba mʼchiwuno mwako, tenga ndodo yanga mʼdzanja lako ndipo thamanga. Ngati ukumana ndi munthu wina aliyense, usamupatse moni, ndipo ngati wina akupatsa moni, usayankhe. Ukagoneke ndodo yanga pa nkhope ya mwanayo.”

30Koma mayi wake wa mwana uja anati, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu nomwe, ineyo sindidzakusiyani.” Choncho Elisa ananyamuka natsatira mayiyo.

31Gehazi anatsogola nakagoneka ndodoyo pa nkhope ya mwanayo, koma sipanamveke mawu kapena kugwedezeka kuonetsa kuti ali moyo. Choncho Gehazi anabwerera kukakumana ndi Elisa ndipo anamuwuza kuti, “Mwanayo sanatsitsimuke.”

32Ndipo Elisa atafika ku nyumbako, taonani, mwanayo anali wakufa atamugoneka pa bedi lake. 33Elisa analowa mʼnyumbamo natseka chitseko. Anali awiri okha mʼchipindamo ndipo iye anapemphera kwa Yehova. 34Kenaka anakwera pa bedi ndi kumugonera mwanayo, pakamwa pake panakhudzana ndi pakamwa pa mwanayo, maso ake anakhudzana ndi maso a mwanayo, ndipo manja ake anakhudzana ndi manja a mwanayo. Pamene ankadzitambalitsa yekha pa mwanayo, thupi la mwanayo linayamba kufunda. 35Elisa anatembenuka nayenda uku ndi uku kamodzi mʼchipindamo ndipo kenaka anakweranso pa bedi nagoneranso mwanayo. Mwanayo anayetsemula kasanu ndi kawiri ndipo anatsekula maso ake.

36Elisa anayitana Gehazi ndipo anati, “Muyitane Msunemuyo.” Ndipo anaterodi. Mayiyo atabwera, Elisa anati, “Tenga mwana wako.” 37Mayiyo analowa, nagwada pa mapazi a Elisa, naweramitsa mutu wake pansi. Kenaka ananyamula mwana wake natuluka.

Imfa mu Mʼphika

38Elisa anabwerera ku Giligala ndipo ku dera limenelo kunali njala. Elisa akukumana ndi ana a aneneri, anati kwa mtumiki wake, “Ika mʼphika waukulu pa moto ndipo uwaphikire chakudya anthu awa.”

39Mmodzi mwa ana aneneriwo anapita kuthengo kukafuna ndiwo ndipo anakapeza mpesa wakuthengo. Iye anathyolako zipatso zake nadzaza nsalu yake. Atabwerera, anazidula zipatsozo naziyika mu mʼphika, ngakhale kuti panalibe amene ankazidziwa. 40Anawapakulira anthu chakudyacho, koma atayamba kudya, anthuwo anafuwula kuti, “Inu munthu wa Mulungu muli imfa mu mʼphikamu!” Ndipo sakanatha kudya chakudyacho.

41Elisa anati, “Bweretsani ufa.” Iye anathira ufa mu mʼphikamo ndipo anati, “Perekani chakudyachi kwa anthu kuti adye.” Ndipo mu mʼphikamo munalibenso zoopsa.

Kudyetsa Anthu 100

42Munthu wina wochokera ku Baala-Salisa anabwera atamutengera munthu wa Mulungu malofu a barele makumi awiri opangidwa kuchokera ku zokolola zoyamba kucha, pamodzinso ndi ngala zatsopano za tirigu. Elisa anati kwa munthuyo, “Apatse anthu kuti adye.”

43Mtumiki wake anafunsa kuti, “Kodi ndikachigawe motani chakudyachi kwa anthu 100?”

Koma Elisa anamuwuzanso kuti, “Apatse anthu adye. Pakuti izi ndi zimene Yehova akunena kuti, ‘Iwo adzadya chakudyachi ndipo china chidzatsalako.’ ” 44Tsono iye anachipereka kwa anthuwo ndipo anadya china nʼkutsalako, molingana ndi mawu a Yehova.