俄巴底亞書 1 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

俄巴底亞書 1:1-21

1俄巴底亞看到的異象。

耶和華懲罰以東

論到以東

主耶和華這樣說:

「我們從耶和華那裡聽到消息,

有位使者被派到各國,說,

『來!我們去攻打以東吧!』」

2耶和華對以東說:

「我要讓你成為列國中最弱小的國家,

使你飽受藐視。

3你住在懸崖峭壁間,

住在高山上,

自以為誰也不能把你拉下來,

但你的驕傲欺騙了你。

4即使你如鷹高飛,

在星辰間築巢,

我也必把你拉下來。

這是耶和華說的。

5「盜賊深夜洗劫你的家,

不會洗劫一空;

人們摘葡萄,不會摘光;

但你會被徹底毀滅!

6以掃1·6 以掃」又名「以東」。要被洗劫一空,

他藏的珍寶要被搜去。

7你的盟友將你逐出家園;

你的朋友欺騙你,戰勝你;

你的知己設陷阱害你,

你卻懵然不知。」

8耶和華說:「到那天,

我要毀滅以東的智者,

除掉以掃山上的明哲。

9提幔的勇士必驚慌失措,

以掃山上的人盡遭殺戮。

懲罰以東的原因

10「因你曾殘暴地對待同胞兄弟雅各

你必蒙羞,永遭毀滅。

11外族人掠奪雅各的財物,

攻入耶路撒冷抽籤分贓時,

你竟然袖手旁觀,

就像他們的同夥一樣。

12你的親族遭難之日,

你不該幸災樂禍;

猶大人被滅的日子,

你不該興高采烈;

他們遭難的日子,

你不該口出狂言;

13我子民遭難的日子,

你不該闖進他們的城;

他們遭難的日子,

你不該幸災樂禍;

他們遭難的日子,

你不該趁火打劫;

14你不該站在路口截殺那些逃亡者;

他們遭難的日子,

你不該把倖存者交給仇敵。

15「耶和華懲罰萬國的日子近了。

必按你的所作所為報應你,

你的惡行必落到自己頭上。

16你們猶大人在我的聖山上怎樣飽飲憤怒,

萬國也要照樣飲,

且要大口吞下,

直到他們完全消逝。

以色列的復興

17「然而,錫安山必成為避難所,

成為聖地。

雅各家必得到自己的產業。

18雅各家將成為火,

約瑟家將成為烈焰,

以掃家將成為碎稭,

被火焚燒、吞噬,無一人逃脫。

這是耶和華說的。

19「南地的人將佔領以掃山;

丘陵的人將佔領非利士

奪取以法蓮撒瑪利亞

便雅憫人將佔領基列

20被擄的以色列人將返回家園,

佔領遠至撒勒法一帶的土地;

耶路撒冷被擄到西法拉的人將佔領南地各城。

21拯救者必登上錫安山,

統治以掃山,

耶和華必做王掌權。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Obadiya 1:1-21

Masomphenya a Obadiya

1Masomphenya a Obadiya.

Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti,

Tamva uthenga wochokera kwa Yehova:

Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti,

“Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”

2“Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina;

udzanyozedwa kwambiri.

3Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa,

iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe

ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali,

iwe amene umanena mu mtima mwako kuti,

‘Ndani anganditsitse pansi?’

4Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga

ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi,

ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,”

akutero Yehova.

5“Anthu akuba akanabwera kwa iwe,

kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku,

aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe!

Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha?

Ngati anthu othyola mphesa akanafika,

kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?

6Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse,

chuma chake chobisika chidzabedwa!

7Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire;

abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa;

amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha,

koma iwe sudzazindikira zimenezi.”

8Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo,

kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu,

anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?

9Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha,

ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau

adzaphedwa pa nkhondo.

10Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo,

udzakhala wamanyazi;

adzakuwononga mpaka muyaya.

11Pamene adani

ankamulanda chuma chake

pamene alendo analowa pa zipata zake

ndi kuchita maere pa Yerusalemu,

pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.

12Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako

pa nthawi ya tsoka lake,

kapena kunyogodola Ayuda

chifukwa cha chiwonongeko chawo,

kapena kuwaseka pa nthawi ya

mavuto awo.

13Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga

pa nthawi ya masautso awo,

kapena kuwanyogodola

pa tsiku la tsoka lawo,

kapena kulanda chuma chawo

pa nthawi ya masautso awo.

14Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu

kuti uphe Ayuda othawa,

kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka

pa nthawi ya mavuto awo.”

15“Tsiku la Yehova layandikira

limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu.

Adzakuchitira zomwe unawachitira ena;

zochita zako zidzakubwerera wekha.

16Iwe unamwa pa phiri langa loyera,

koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza;

iwo adzamwa ndi kudzandira

ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.

17Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso;

phirilo lidzakhala lopatulika,

ndipo nyumba ya Yakobo

idzalandira cholowa chake.

18Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto

ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto;

nyumba ya Esau idzasanduka chiputu,

ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza.

Sipadzakhala anthu opulumuka

kuchokera mʼnyumba ya Esau.”

Yehova wayankhula.

19Anthu ochokera ku Negevi adzakhala

ku mapiri a Esau,

ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri

adzatenga dziko la Afilisti.

Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya,

ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.

20Aisraeli amene ali ku ukapolo

adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati;

a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi

adzalandira mizinda ya ku Negevi.

21Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni

ndipo adzalamulira mapiri a Esau.

Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.