以賽亞書 50 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以賽亞書 50:1-11

以色列的罪惡

1耶和華說:

「我休你們母親的休書在哪裡呢?

我把你們賣給了我哪一個債主呢?

你們被賣是因為你們的罪惡,

你們母親被休是因為你們的過犯。

2為什麼我來的時候一個人也不在?

為什麼我呼喚的時候沒有人回答?

是我的臂膀太短不能救贖你們嗎?

是我沒有能力拯救你們嗎?

看啊,我斥責一聲,海就乾了;

我使江河變為曠野,

魚類因無水而乾死,發出腥臭。

3我使黑暗遮蔽穹蒼,

用麻布掩蓋天空。」

主僕的順服

4主耶和華賜我教導的能力,

使我知道用什麼話幫助疲乏的人。

每天早晨,主喚醒我,

叫我像受教者那樣側耳聆聽。

5主耶和華開了我的耳朵,

我沒有悖逆,也沒有退縮。

6人打我的背,我任他打;

人拔我的鬍子,我任他拔;

人侮辱我,朝我吐唾沬,

我也不掩面。

7我並不覺得羞愧,

因為主耶和華幫助我。

我心如堅石,

知道自己必不會蒙羞。

8為我伸張正義的來了,

誰要控告我呢?

讓我們來理論吧!

誰是我的控告者呢?

讓他到我這裡來吧!

9看啊,有主耶和華幫助我,

誰能定我有罪呢?

看啊,他們都要像衣服一樣漸漸破舊,

被蛀蟲吃掉。

信靠上帝

10你們中間誰敬畏耶和華,

聽從祂僕人的話?

行在黑暗中、

沒有光的人要信靠耶和華的名,

仰賴自己的上帝。

11然而,你們自己生火、自備火把的人啊,

靠自己點燃的火光行走吧!

你們必落入悲慘的境地,

這是耶和華親手所定的。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 50:1-11

Tchimo la Israeli, Kumvera kwa Mtumiki

1Yehova akuti,

“Kalata imene ndinasudzulira amayi

anu ili kuti?

Kapena mwa anthu amene ndili nawo ngongole,

ndinakugulitsani kwa ati?

Inu munagulitsidwa ku ukapolo chifukwa cha machimo anu;

amayi anu anachotsedwa chifukwa cha kulakwa kwanu.

2Nʼchifukwa chiyani pamene ndinabwera kudzakupulumutsani panalibe munthu?

Pamene ndinayitana, nʼchifukwa chiyani panalibe wondiyankha?

Kodi dzanja langa ndi lalifupi kuti nʼkulephera kukuwombolani?

Kodi ndilibe mphamvu zokupulumutsirani?

Ndi kudzudzula kokha ndinawumitsa nyanja yayikulu,

mitsinje ndinayisandutsa chipululu;

nsomba za mʼmenemo zinawola chifukwa chosowa madzi;

ndipo zinafa ndi ludzu.

3Ndinaphimba thambo ndi mdima

ndipo chiguduli chinakhala chofunda chake.”

4Ambuye Yehova anandiphunzitsa mawu oyenera kuyankhula

kudziwa mawu olimbitsa mtima anthu ofowoka.

Mmawa mulimonse amandidzutsa,

amathwetsa khutu langa kuti ndimve monga amachitira munthu amene akuphunzira.

5Ambuye Yehova wanditsekula makutu anga,

ndipo sindinakhale munthu wowukira

ndipo sindinabwerere mʼmbuyo.

6Ndinapereka msana wanga kwa ondimenya

masaya anga ndinawapereka kwa anthu ondizula ndevu;

sindinawabisire nkhope yanga

anthu ondinyoza ndi ondilavulira.

7Popeza Ambuye Yehova amandithandiza,

sindidzachita manyazi.

Tsono ndalimba mtima ngati msangalabwi,

chifukwa ndikudziwa kuti sindidzachita manyazi.

8Wondikhalira kumbuyo ali pafupi,

ndaninso amene adzandiyimba mlandu?

Abwere kuti tionane maso ndi maso!

Mdani wanga ndi ndani?

Abweretu kuti tilimbane!

9Ambuye Yehova ndiye amene amandithandiza.

Ndaninso amene adzanditsutsa?

Onse adzatha ngati chovala

chodyedwa ndi njenjete.

10Ndani mwa inu amaopa Yehova

ndi kumvera mawu a mtumiki wake?

Aliyense woyenda mu mdima,

popanda chomuwunikira,

iye akhulupirire dzina la Yehova

ndi kudalira Mulungu wake.

11Koma tsopano inu nonse amene mumasonkha moto

ndi kuyatsa sakali za moto kufuna kuwononga anzanu,

lowani mʼmoto wanu womwewo.

Pitani mu sakali za moto zimene mwayatsa.

Ndipo ine Yehova

ndiye amene ndidzakugwetsereni mazunzowo.