以賽亞書 2 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以賽亞書 2:1-22

主必統治萬邦

1亞摩斯的兒子以賽亞看到以下有關猶大耶路撒冷的異象。

2在末後的日子,耶和華殿所在的山必聳立,

高過群山,超過萬嶺,

萬族都要湧向它。

3眾民都必來,說:

「來吧!讓我們登耶和華的山,

雅各之上帝的殿。

祂必將祂的路指示給我們,

使我們走祂的道。」

因為訓誨必出於錫安

耶和華的話語必來自耶路撒冷

4祂必在各國施行審判,

為列邦平息紛爭。

他們必將刀劍打成犁頭,

把矛槍製成鐮刀。

國與國不再刀兵相見,

人們不用再學習戰事。

5雅各家啊,來吧!

讓我們走在耶和華的光中。

耶和華審判的日子

6耶和華啊,你離棄了你的子民——雅各的後裔,

因為他們當中充滿了東方的惡俗,

非利士人一樣占卜,

跟外族人同流合污。

7他們境內金銀遍地,

財寶無窮;

他們境內馬匹充裕,

戰車無數。

8他們境內偶像林立,

他們跪拜自己用手所造的物品,

跪拜自己用指頭所造之物。

9他們必遭羞辱和貶抑。

耶和華啊,

求你不要赦免他們。

10要躲進岩穴,藏入地洞,

逃避耶和華的憤怒和威榮!

11到那日,狂妄的人將被挫敗,

驕傲的人將遭貶抑;

唯獨耶和華將受尊崇。

12因為萬軍之耶和華已定了日子,

要懲罰一切驕傲狂妄和自高自大的人,

使他們淪為卑賤;

13祂必毀滅黎巴嫩高大的香柏樹和巴珊的橡樹,

14毀滅一切崇山峻嶺,

15毀滅高聳的城樓和堅固的城牆,

16毀滅他施的商船和一切華美的船隻。

17到那日,狂妄的人必被挫敗,

驕傲的人必遭貶抑,

唯獨耶和華受尊崇。

18偶像必被徹底剷除。

19耶和華使大地震動的時候,

眾人躲進岩穴,藏入地洞,

逃避祂的憤怒和威榮。

20到那日,眾人必把造來敬拜的金銀偶像丟給田鼠和蝙蝠。

21耶和華使大地震動的時候,

眾人必躲進山洞和岩縫,

逃避祂的憤怒和威榮。

22不要再倚靠世人,

他們的生命不過是一口氣,

他們有什麼值得稱道的呢?

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 2:1-22

Phiri la Yehova

1Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:

2Mʼmasiku otsiriza,

phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa

kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse,

lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse,

ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.

3Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti,

“Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova,

ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo.

Iye adzatiphunzitsa njira zake,

ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.”

Malangizo adzachokera ku Ziyoni,

mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.

4Iye adzaweruza pakati pa mayiko,

ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri.

Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu

ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera.

Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina,

kapena kuphunziranso za nkhondo.

5Inu nyumba ya Yakobo, bwerani,

tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.

Tsiku la Yehova

6Inu Yehova mwawakana anthu anu,

nyumba ya Yakobo.

Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa;

amawombeza mawula ngati Afilisti,

ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.

7Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide;

ndipo chuma chawo ndi chosatha.

Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo;

ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.

8Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano;

iwo amapembedza ntchito ya manja awo,

amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.

9Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa

ndi kutsitsidwa.

Inu Yehova musawakhululukire.

10Lowani mʼmatanthwe,

bisalani mʼmaenje,

kuthawa kuopsa kwa Yehova

ndi ulemerero wa ufumu wake!

11Kudzikuza kwa anthu kudzatha,

ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa;

Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.

12Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku

limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama,

ndipo adzagonjetsa

onse amphamvu,

13tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali,

ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,

14tsiku la mapiri onse ataliatali

ndiponso la zitunda zonse zazitali,

15tsiku la nsanja zonse zazitali

ndiponso malinga onse olimba,

16tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi

ndiponso la mabwato onse okongola.

17Kudzikuza kwa munthu kudzatha

ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa,

Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,

18ndipo mafano onse adzatheratu.

19Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe

ndi mʼmaenje a nthaka,

kuthawa mkwiyo wa Yehova,

ndiponso ulemerero wa ufumu wake,

pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.

20Tsiku limenelo anthu adzatayira

mfuko ndi mileme

mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide,

amene anawapanga kuti aziwapembedza.

21Adzathawira mʼmapanga a matanthwe

ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka

kuthawa mkwiyo wa Yehova

ndiponso ulemerero wa ufumu wake,

pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.

22Lekani kudalira munthu,

amene moyo wake sukhalira kutha.

Iye angathandize bwanji wina aliyense?