以弗所書 2 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以弗所書 2:1-22

靠恩典、憑信心

1你們從前死在過犯和罪惡之中。 2那時,你們隨從今世的風俗,順服在空中掌權的魔鬼,就是如今在一切叛逆上帝之人心中運行的邪靈。 3我們以前也在他們當中隨從罪惡的本性2·3 罪惡的本性」希臘文是「肉體」。,放縱肉體和心中的私慾,與其他人一樣本是惹上帝發怒的人。

4然而上帝有豐富的憐憫,祂深愛我們, 5儘管我們死在過犯之中,祂仍然使我們和基督一同活了過來。你們得救是因為上帝的恩典。 6在基督耶穌裡,上帝使我們與基督一同復活,一同坐在天上, 7好藉著祂在基督耶穌裡向我們所施的恩慈,向後世顯明祂無可比擬的豐富恩典。 8你們得救是靠恩典,憑信心。這不是出於你們自己,而是上帝的禮物; 9也不是由於你們的行為,以免有人自誇。 10我們是上帝的傑作,是在基督耶穌裡創造的,為要叫我們做祂預先安排給我們的美善之事。

在基督裡合而為一

11因此,你們要記住,從前按照肉體來說你們是外族人,那些肉體上受過人手所行割禮的以色列人稱你們為「沒有受過割禮的」。 12那時,你們與基督無關,又不是以色列人,在上帝應許的諸約上是局外人,你們活在世上沒有盼望,沒有上帝。 13但你們這些從前遠離上帝的人,如今在基督耶穌裡,靠著祂所流的血已經被帶到上帝面前。 14因為基督耶穌親自給我們帶來了和平,以自己的身體拆毀了以色列人和外族人之間充滿敵意的隔牆,使雙方合而為一, 15並廢除了以誡命和規條為內容的律法制度。祂這樣做是為了在自己裡面把雙方造成一個新人,成就和平, 16並藉著十字架消滅彼此間的敵意,使雙方藉著一個身體與上帝和好。 17祂來傳揚這平安的福音給你們這些離上帝很遠的外族人,也給我們這些離上帝很近的以色列人。 18我們雙方都是靠著祂在同一位聖靈的引導下來到父上帝面前。

19從此,你們不再是外人或過客,你們與眾聖徒一樣是天國的子民,是上帝家裡的人了。 20你們已被建立在眾使徒和先知們的基礎上,基督耶穌自己是房角石。 21整座建築的各部分都靠祂巧妙地連接在一起,逐漸成為主的聖殿。 22你們也靠著祂被建造在一起,成為上帝藉著聖靈居住的地方。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aefeso 2:1-22

Amene anali Akufa Alandira Moyo

1Kunena za inu, kale munali akufa chifukwa cha zolakwa zanu ndi machimo anu, 2mmene inu munkakhalamo pamene munkatsatira njira za dziko lapansi ndi za ulamuliro waufumu wa mlengalenga, mzimu umene ukugwira ntchito tsopano mwa amene samvera. 3Nthawi ina tonsefe tinalinso ndi moyo wonga wawo, tinkachitanso zilizonse zimene matupi ndi maganizo athu ankafuna. Mwachibadwa chathu, tinali oyenera chilango monga anthu ena onse. 4Koma chifukwa cha chikondi chake chachikulu pa ife, Mulungu amene ndi olemera mʼchifundo, 5anatipanga kukhala amoyo ndi Khristu ngakhale pamene ife tinali akufa mu zolakwa zathu. Koma tinapulumutsidwa mwachisomo. 6Ndipo Mulungu anatiukitsa pamodzi ndi Khristu ndi kutikhazika pamodzi ndi Iye mmwamba mwa Khristu Yesu, 7ndi cholinga chakuti mʼnthawi imene ikubwera, Iyeyo adzaonetse chuma choposa cha chisomo chake, choonetsedwa mwa kukoma mtima kwake kwa ife mwa Khristu Yesu. 8Pakuti mwapulumutsidwa mwachisomo, kudzera mʼchikhulupiriro ndipo izi sizochokera mwa inu eni, koma ndi mphatso ya Mulungu, 9osati ndi ntchito, kuti wina aliyense asadzitamandire. 10Pakuti ndife ntchito ya Mulungu, olengedwa mwa Khristu Yesu kuti tichite ntchito zabwino, zimene Mulungu anazikonzeratu kale kuti tizichite.

Umodzi mwa Khristu

11Chifukwa chake kumbukirani kuti poyamba inu amene munali anthu a mitundu ina mwachibadwa ndipo munkatchedwa “osachita mdulidwe” ndi amene amadzitcha okha “a mdulidwe” (zimene zinachitika mʼthupi ndi manja a anthu). 12Kumbukirani kuti nthawi imene inu munali wopanda Khristu, simunkawerengedwa ngati nzika za Israeli ndipo munali alendo pa pangano la lonjezo, wopanda chiyembekezo ndi opanda Mulungu mʼdziko lapansi. 13Koma tsopano mwa Khristu Yesu, inu amene nthawi ina munali kutali, mwabweretsedwa pafupi kudzera mʼmagazi a Khristu.

14Pakuti Iye mwini ndiye mtendere wathu, amene anachita kuti awiri akhale mmodzi ndipo anagumula chotchinga, khoma la udani lotilekanitsa, 15pothetsa mʼthupi lake lamulo pamodzi ndi zolamulira zake ndi malangizo. Cholinga chake chinali chakuti alenge mwa Iye mwini, munthu mmodzi watsopano kuchokera kwa abwino, motero nʼkupanga mtendere, 16ndi kuyanjanitsa onse awiriwa mʼthupi lake kwa Mulungu, kudzera pa mtanda, umene Iye anaphapo udani wawo. 17Iye anabwera ndipo analalikira mtendere kwa inu amene munali kutali ndi mtendere ndiponso kwa iwonso amene anali pafupi. 18Pakuti mwa Iye, ife tonse titha kufika kwa Atate mwa Mzimu mmodzi.

19Kotero kuti, inu sindinunso alendo ndi adani, koma nzika pamodzi ndi anthu a Mulungu ndiponso a mʼbanja la Mulungu. 20Ndinu okhazikika pa maziko a atumwi ndi a aneneri, pamodzi ndi Khristu Yesu mwini ngati mwala wa pa ngodya. 21Mwa Iyeyo, nyumba yonse yalumikizidwa pamodzi ndipo yakwezedwa kukhala Nyumba yoyera mwa Ambuye. 22Ndipo mwa Iye, inunso mukamangidwa pamodzi ndi ena onse kukhala nyumba yokhalamo imene Mulungu amakhala mwa Mzimu wake.