雅各书 3 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

雅各书 3:1-18

邪恶的舌头

1我的弟兄姊妹,不要个个当教师,因为你们知道,我们为人师表的将受到更严格的评判, 2因为我们在许多方面难免有过失。如果谁在言语上没有过失,他就是纯全的人,也能在各方面保持自制。 3我们如果把嚼环放在马嘴里,便可以使它顺服,驾驭它。 4一艘大船在遭遇暴风吹袭时,船身虽然庞大,但舵手只要操纵一个小小的舵,就能随意驾驶它。

5同样,人的舌头虽然很小,却能说夸大的话。

看啊,小火星能点燃大森林。 6舌头就是火,是我们身体上的一个充满邪恶的世界,能玷污人的全身,足以毁掉人的一生,它是从地狱点燃的火。 7自然界中的各类走兽、飞禽、爬虫、水族都可以被驯服,也已经被人类驯服了, 8但无人能驯服自己的舌头,因为舌头是个无法控制的邪恶之物,充满了致命的毒气。 9我们用舌头来赞美主和天父,也用舌头来咒诅照着上帝的形象被造的人。 10赞美和咒诅竟然从同一张嘴里发出来。我的弟兄姊妹,这是不应该的! 11同一个泉源能涌出甜苦两样水吗? 12我的弟兄姊妹,无花果树能结出橄榄吗?葡萄树能结出无花果吗?一个咸水泉必流不出甜水来。

天上的智慧

13你们当中谁是有智慧、有见识的呢?请他带着来自智慧的谦和,在善行上表现出来。 14但如果你们心怀苦毒的嫉妒和自私的野心,就不要自夸说有智慧,也不要违背真理去撒谎。 15这种智慧并非来自天上,而是从世俗、私欲和魔鬼来的。 16哪里有嫉妒和自私的野心,哪里就会有混乱和各样的恶事。

17但从天上来的智慧首先是纯洁,然后是爱好和平、温良柔顺、充满怜悯、多结善果、不存偏见、没有虚伪。 18使人和睦的人撒下和平的种子,必收获仁义的果实。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yakobo 3:1-18

Za Lilime

1Abale anga, ambiri musakhale aphunzitsi chifukwa mumadziwa kuti aphunzitsife tidzaweruzidwa mowuma kuposa anthu ena onse. 2Tonsefe timapunthwa mʼnjira zambiri. Ngati wina salakwa poyankhula, ameneyo ndi munthu wangwiro, wodziwa kuyangʼanira bwino thupi lake lonse.

3Tikayika tizitsulo mʼkamwa mwa akavalo kuti atimvere, timatha kuwongolera thupi lake lonse. 4Taonani sitima zapamadzi. Ngakhale ndi zazikulu kwambiri ndipo zimakankhidwa ndi mphepo yamphamvu, zimawongoleredwa ndi tsigiro lalingʼono kulikonse kumene woyendetsayo akufuna kupita. 5Momwemonso, lilime ndi kachiwalo kakangʼono ka thupi koma limadzitama kuti nʼkuchita zikuluzikulu. Tangoganizirani za nkhalango yayikulu imene ingapse ndi kalawi kamoto koyamba mochepa. 6Lilime nalonso ndi moto, dziko la zoyipa pakati pa ziwalo za thupi. Limawononga munthu yense wathunthu. Limayika zonse za moyo wake pa moto, ndipo moto wake ndi wochokera ku gehena.

7Mitundu yonse ya nyama, ya mbalame, ya zokwawa ndi ya zolengedwa za mʼnyanja, zikuwetedwa ndipo munthu wakhala akuziweta, 8koma palibe munthu amene angaweta lilime. Lilime ndipo silitha kupuma, ndi lodzaza ndi ululu wakupha.

9Ndi lilime lomwelo timatamanda Ambuye ndi Atate athu, komanso ndi lilime lomwelo timalalatira anthu, amene anapangidwa mʼchifanizo cha Mulungu. 10Mʼkamwa momwemo mutuluka matamando ndi kulalata. Abale anga, zisamatero ayi. 11Kodi madzi abwino ndi a mchere angatuluke pa kasupe mmodzi? 12Abale anga, kodi mtengo wa mkuyu nʼkubala mphesa, kapena mtengo wampesa nʼkubala nkhuyu? Kasupe wa madzi a mchere sangatulutsenso madzi abwino.

Mitundu Iwiri ya Nzeru

13Ndani mwa inu amene ndi wanzeru ndi womvetsa zinthu? Mulekeni aonetse ndi makhalidwe ake abwino kuti nzeru ndiye zikutsogolera kudzichepetsa kwake ndi zochita zake 14Koma ngati muli ndi mtima wakaduka ndi odzikonda, musadzitamandire kapena kukana choonadi. 15“Nzeru” zotere sizochokera kumwamba koma ndi za mʼdziko lapansi, si zauzimu koma ndi za ziwanda. 16Pakuti pamene pali kaduka ndi kudzikonda pomweponso pamakhala chisokonezo ndi zochitika zoyipa zonse.

17Koma nzeru imene imachoka kumwamba, poyamba ndi yangwiro, ndi yokonda mtendere, yoganizira za ena, yogonjera, yodzaza ndi chifundo ndi chipatso chabwino, yosakondera ndi yoona mtima. 18Anthu amtendere amene amadzala mtendere amakolola chilungamo.