诗篇 110 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 110:1-7

第 110 篇

上帝和祂拣选的王

大卫的诗歌。

1耶和华对我主说:

“你坐在我的右边,

等我使你的仇敌成为你的脚凳。”

2耶和华必从锡安扩展你的王权,

你必统管你的仇敌。

3你跟仇敌作战的时候,

你的百姓必甘心跟从,

他们衣着圣洁,

如清晨的甘露。

4耶和华起了誓,永不反悔,

祂说:“你照麦基洗德的模式永远做祭司。”

5主在你身旁保护你,

祂发怒的时候,必毁灭列王。

6祂要审判列国,

使列国尸横遍野。

祂要毁灭世上的首领。

7祂要喝路旁的溪水,

祂必精神抖擞。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 110:1-7

Salimo 110

Salimo la Davide.

1Yehova akuwuza Mbuye wanga kuti,

“Khala ku dzanja langa lamanja

mpaka nditasandutsa adani ako

kukhala chopondapo mapazi ako.”

2Yehova adzakuza ndodo yamphamvu ya ufumu wako kuchokera mʼZiyoni;

udzalamulira pakati pa adani ako.

3Ankhondo ako adzakhala odzipereka

pa tsiku lako la nkhondo.

Atavala chiyero chaulemerero,

kuchokera mʼmimba ya mʼbandakucha,

udzalandira mame a unyamata wako.

4Yehova walumbira

ndipo sadzasintha maganizo ake:

“Ndiwe wansembe mpaka muyaya

monga mwa unsembe wa Melikizedeki.”

5Ambuye ali kudzanja lako lamanja;

Iye adzaponda mafumu pa tsiku la ukali wake.

6Adzaweruza anthu a mitundu ina,

adzadzaza dziko lapansi ndi mitembo ndipo adzaphwanya olamulira a pa dziko lonse lapansi.

7Iye adzamwa mu mtsinje wa mʼmbali mwa njira;

choncho adzaweramutsa mutu wake.