诗篇 10 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 10:1-18

第 10 篇

求上帝惩治恶人

1耶和华啊,你为何远远站着?

为何在我遭难时隐藏起来?

2恶人狂妄地追逼穷苦人,

愿他们落入自己所设的圈套。

3恶人夸耀自己的贪欲,

贪婪的人憎恨、咒诅耶和华。

4他们狂傲自大,心中没有上帝,

从不寻求耶和华。

5他们凡事顺利,

对你的审判不屑一顾,

对所有的仇敌嗤之以鼻。

6他们自以为可以屹立不倒,

世世代代永不遭殃。

7他们满口咒诅、谎话和恐吓之言,

舌头沾满祸害和邪恶。

8他们埋伏在村庄,

暗中监视受害者,杀害无辜。

9他们像狮子埋伏在暗处,

猎取无助的人,

用网罗拖走他们。

10不幸的人被击垮,

倒在他们的暴力下。

11他们自言自语:“上帝忘记了,

祂掩面不理这些事!”

12耶和华啊,求你起来!

上帝啊,求你举手施罚,

不要忘记无助的人!

13恶人为何轻视上帝,

以为上帝不会追究呢?

14但你已看到世人的疾苦,

随时伸出援手。

困苦无助的人投靠你,

你是孤儿的帮助。

15求你打断恶人的臂膀,

彻底追究他们的罪恶。

16耶和华永永远远是君王,

列邦必从祂的土地上灭亡。

17耶和华啊,

你知道困苦人的愿望,

你必垂听他们的呼求,

安慰他们。

18你为孤儿和受欺压的人申冤,

使渺小的世人不能再恐吓他们。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 10:1-18

Salimo 10

1Nʼchifukwa chiyani Yehova mwayima patali?

Chifukwa chiyani mukudzibisa nokha pa nthawi ya mavuto?

2Mwa kunyada kwake munthu woyipa asaka wofowoka,

amene akodwa mʼnjira zimene iye wakonza.

3Iye amatamandira zokhumba za mu mtima wake;

amadalitsa aumbombo ndi kuchitira chipongwe Yehova.

4Mwa kunyada kwake woyipa safunafuna Mulungu;

mʼmaganizo ake wonse mulibe malo a Mulungu.

5Zinthu zake zimamuyendera bwino;

iye ndi wamwano ndipo malamulo anu ali nawo kutali;

amanyogodola adani ake onse.

6Iye amadziyankhulira kuti, “Palibe chimene chidzandigwedeze.

Ndidzakhala wokondwa nthawi zonse ndipo sindidzakhala pa mavuto.”

7Mʼkamwa mwake mwadzaza matemberero, mabodza ndi zoopseza;

zovutitsa ndi zoyipa zili pansi pa lilime lake.

8Iye amabisalira anthu pafupi ndi midzi,

kuchokera pobisalapo amapha anthu osalakwa,

amayangʼanayangʼana mwachinsinsi anthu oti awawononge.

9Amabisalira anthu ngati mkango pa zitsamba.

Amabisalira kuti agwire anthu opanda mphamvu;

amagwira anthu opanda mphamvu ndi kuwakokera mu ukonde wake.

10Anthuwo amawapondaponda ndipo amakomoka;

amakhala pansi pa mphamvu zake.

11Iye amati mu mtima mwake, “Mulungu wayiwala,

wabisa nkhope yake ndipo sakuonanso.”

12Dzukani Yehova! Onetsani dzanja lanu Inu Mulungu.

Musayiwale anthu opanda mphamvu.

13Nʼchifukwa chiyani munthu woyipa amachitira chipongwe Mulungu?

Chifukwa chiyani amati mu mtima mwake,

“Iye sandiyimba mlandu?”

14Komatu Inu Mulungu, mumazindikira mavuto ndi zosautsa,

mumaganizira zochitapo kanthu.

Wovutikayo amadzipereka yekha kwa Inu pakuti

Inu ndi mthandizi wa ana amasiye.

15Thyolani dzanja la woyipitsitsa ndi la munthu woyipa;

muzengeni mlandu chifukwa cha zoyipa zake

zimene sizikanadziwika.

16Yehova ndi Mfumu kwamuyaya;

mitundu ya anthu idzawonongeka kuchoka mʼdziko lake.

17Mumamva Inu Yehova, zokhumba za osautsidwa;

mumawalimbikitsa ndipo mumamva kulira kwawo.

18Kuteteza ana amasiye ndi oponderezedwa,

ndi cholinga chakuti munthu amene ali wa dziko lapansi asaopsenso.