腓立比书 2 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

腓立比书 2:1-30

效法基督

1所以,如果你们在基督里受到鼓励,得到爱的安慰,与圣灵相通,有慈悲和怜悯之心, 2就要同心合意,彼此相爱,灵里合一,思想一致,好让我的喜乐更充足。 3凡事不可自私自利、爱慕虚荣,要心存谦卑,看别人比自己强。 4各人不要只顾自己的事,也要为别人的需要着想。 5你们应当有基督耶稣那样的心肠。

6祂虽然本质上是上帝,

却没有紧紧抓住自己与上帝平等的地位不放,

7反而甘愿放下一切,

取了奴仆的形象,

降生为人的样子。

8祂以人的样子出现后,

就自愿卑微,顺服至死,

而且死在十字架上。

9因此,上帝将祂升为至尊,

赐给祂超乎万名之上的名,

10使一切天上的、

地上的和地底下的,

无不屈膝跪拜在耶稣的名下,

11无不口称耶稣基督是主,

将荣耀归于父上帝。

暗世明灯

12所以,我亲爱的弟兄姊妹,既然我在你们那里的时候,你们一向都很顺服;如今我不在你们那里,你们更要顺服,要战战兢兢地活出得救后应有的生命。 13因为你们立志和行事都是上帝在你们心中工作,为要成就祂美好的旨意。

14无论做什么事,都不要抱怨,也不要与人争论, 15好使你们在这个弯曲败坏的时代中无可指责、诚实无伪,做上帝纯洁无瑕的儿女,如同明光照耀在世上, 16坚守生命之道。这样,到了基督再来的时候,我可以夸口自己没有空跑一场,也没有白费功夫。 17你们的信心就是献给上帝的事奉和祭物,即使在上面浇奠我的生命,我也很喜乐,并且和你们大家一同喜乐。 18同样,你们也要喜乐,要和我一同喜乐。

保罗的得力同工

19如果主耶稣许可,我希望尽快派提摩太去你们那里,我好知道你们的近况,心里得到安慰。 20因为没有人像他那样跟我一同真正关心你们的事。 21别人都只顾自己的事,并不关心耶稣基督的事。 22但你们知道提摩太的为人,我与他情同父子,一起事奉和传扬福音。 23所以,我的案子一旦明朗了,我会立刻派他去见你们。 24我深信如果主许可,我自己很快也会去你们那里。

25另外,我觉得有必要让以巴弗提回到你们那里。他是我的弟兄、同工和战友,也是你们差遣来服侍我、供应我需用的。 26他很想念你们,并且感到不安,因为你们听说了他患病的事。 27他确实病了,几乎丧命,但上帝怜悯了他,不但怜悯他,也怜悯了我,没让我忧上加忧。 28所以,我想尽快派他回去与你们相聚,好让你们喜乐,也可以减少我的挂虑。 29你们要在主里欢欢喜喜地接待他,而且要敬重像他这样的人。 30他为了基督的工作,将生死置之度外,几乎丧命,以弥补你们服侍我的不足之处。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Afilipi 2:1-30

Kutsanzira Kudzichepetsa kwa Khristu

1Ngati muli ndi chilimbikitso chilichonse chifukwa cholumikizana ndi Khristu, ngati muli ndi chitonthozo chifukwa cha chikondi chake, ngati muli ndi mtima umodzi mwa Mzimu, ndipo ngati mumakomerana mtima ndi kuchitirana chifundo, 2tsono tsirizani chimwemwe changa pokhala amaganizo ofanana, achikondi chimodzimodzi, amodzi mu mzimu ndi acholinga chimodzinso. 3Musachite kalikonse ndi mtima odzikonda chabe kapena odzitukumula chabe. Koma khalani odzichepetsa ndipo aliyense aziona mnzake ngati womuposa iyeyo. 4Musamangofuna zokomera inu nokha koma aliyense azifuna zokomeranso ena.

5Pa ubale wanu wina ndi mnzake, mukhale ndi mtima wofanana ndi wa Khristu Yesu:

6Iyeyu, pokhala Mulungu ndithu,

sanatenge kufanana ndi Mulungu kukhala chinthu choyenera kuchigwiritsa.

7Koma anadzichepetsa kotheratu

nakhala ndi khalidwe ngati la kapolo

ndi kukhala munthu ngati anthu ena onse.

8Ndipo pokhala munthu choncho

anadzichepetsa yekha

ndipo anamvera mpaka imfa yake,

imfa yake ya pamtanda!

9Choncho Mulungu anamukweza Iye kukhala wapamwamba kwambiri,

ndipo anamupatsa dzina loposa dzina lina lililonse

10kuti pakumva dzina la Yesu, bondo lililonse limugwadire,

kumwamba ndi pa dziko lapansi ndi pansi pa dziko,

11ndipo lilime lililonse livomereze kuti Yesu Khristu ndi Ambuye

kuchitira ulemu Mulungu Atate.

Kuwala monga Nyenyezi

12Tsono, abwenzi anga okondedwa, monga mwakhala omvera nthawi zonse, osati pamene ndinali nanu pokha, koma tsopano koposa pamene ndili kutali. Pitirizani kugwira ntchito ya chipulumutso chanu mwa mantha ndi kunjenjemera, 13pakuti ndi Mulungu amene amagwira ntchito mwa inu kuti mufune ndi kuchita zimene zimamukondweretsa Iyeyo.

14Muzichita zonse mosawiringula kapena mosatsutsapo, 15kuti mukhale wopanda cholakwa ndi angwiro, ana a Mulungu wopanda cholakwika mu mʼbado uno wachinyengo ndi wosocheretsa. Mukatero mudzawala pakati pawo ngati nyenyezi zakumwamba 16powawuza mawu amoyo. Ndipo ine ndidzatha kunyadira pa tsiku la Khristu kuti sindinathamange kapena kugwira ntchito pachabe. 17Koma ngakhale ndikuthiridwa ngati nsembe ya chakumwa yoperekedwa pa nsembe ndi pa utumiki wochokera mʼchikhulupiriro chanu, ndine wokondwa ndi wosangalala pamodzi ndi inu nonse. 18Chomwechonso, inu khalani okondwa ndi osangalala nane pamodzi.

Timoteyo ndi Epafrodito

19Ngati Ambuye Yesu alola, ndikukhulupirira kuti ndidzamutuma Timoteyo msanga kwanuko, kuti mwina ndingadzasangalale ndikadzamva za moyo wanu. 20Ndilibenso wina monga iyeyu amene ali ndi chidwi chenicheni pa za moyo wanu. 21Pakuti aliyense amangofuna zokomera iye yekha osati zokomera Yesu Khristu. 22Koma inu mukudziwa kuti Timoteyo wadzionetsa yekha, chifukwa watumikira ndi ine pa ntchito ya Uthenga Wabwino monga mwana ndi abambo ake. 23Choncho ndikuyembekezera kumutuma msanga ndikangodziwa mmene zinthu zanga ziyendere. 24Ndipo ndikukhulupirira kuti Ambuye akalola ine mwini ndidzafikanso kwanuko posachedwapa.

25Koma ndikuganiza kuti nʼkofunika kuti ndikutumizireni mʼbale wanga Epafrodito, mtumiki mnzanga ndi msilikali mnzanga, amenenso ndi mtumiki wanu amene munamutumiza kuti adzandithandize pa zosowa zanga. 26Pakuti akukulakalakani nonsenu ndipo akusauka mu mtima chifukwa munamva kuti akudwala. 27Zoonadi ankadwala ndipo anatsala pangʼono kumwalira. Koma Mulungu anamuchitira chifundo, ndipo sanangomuchitira chifundo iye yekhayu komanso ine, kuti chisoni changa chisachuluke. 28Choncho khumbo langa lofulumiza kumutumiza lakula, kuti pamene mumuonenso musangalale komanso kuti nkhawa yanga ichepe. 29Mulandireni mwa Ambuye ndi chimwemwe chachikulu, ndipo anthu onga iyeyu muziwachitira ulemu. 30Iyeyu anatsala pangʼono kufa chifukwa cha ntchito ya Khristu, anayika moyo pa chiswe kuti akwaniritse thandizo limene inu simukanatha.