耶利米书 14 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

耶利米书 14:1-22

预言旱灾

1耶和华告诉耶利米有关旱灾的事:

2犹大充满悲泣,

她的城邑衰败,

人人坐在地上痛哭,

耶路撒冷哀鸣四起。

3贵族派仆人去水池打水,

仆人去那里发现没有水,

就带着空瓶垂头丧气、

羞愧难当地回去了。

4天不下雨,

土地干裂,

农夫沮丧地抱着头。

5因为没有草,

田野的母鹿抛弃了刚生下来的小鹿;

6因为没有草,

野驴站在光秃的山头上像豺狼一样喘气,双目无神。”

7耶和华啊,虽然我们的罪控告我们,

我们屡屡叛逆得罪你,

求你为了自己的尊名而拯救我们。

8以色列的盼望和患难时的救主啊,

你为什么在这里像一个异乡人,

像一个只住一夜的旅客呢?

9你为什么像一个受惊的人,

像一个无力救人的勇士呢?

耶和华啊,你一直都在我们中间,

我们属于你的名下,

求你不要抛弃我们。

10论到这些百姓,耶和华这样说:

“他们喜欢流浪,

不约束自己的脚步,

因此耶和华不喜欢他们。

现在祂要清算他们的罪恶,

追讨他们的罪。”

11耶和华对我说:“你不要为这百姓祷告。 12他们禁食,我也不会听他们的呼求;他们献上燔祭和素祭,我也不会悦纳。我要用战争、饥荒和瘟疫灭绝他们。” 13我说:“主耶和华啊!众先知不停地告诉他们不会有战争,也不会遭遇饥荒,说耶和华必在这地方赐给他们永久的平安。”

14耶和华对我说:“那些先知奉我的名说假预言,我并没有差派他们,没有委任他们,也没有对他们说话。他们对你们说的预言是假异象,是占卜,是凭空捏造。 15我没有差派他们,他们却奉我的名说这地方必没有战争和饥荒。他们必死于战争和饥荒。这是耶和华说的。 16至于听他们说预言的人以及那些人的妻子儿女,必因饥荒和战争而暴尸耶路撒冷街头。因为我要使他们受到应得的报应。

17耶利米,你要对他们说,

‘让我昼夜泪眼汪汪吧,

因为我的同胞遭受重创,

遍体鳞伤。

18我走到田间,

眼前是具具被杀的尸体;

我进入城里,

见饥荒肆虐,

祭司和先知也流亡异乡14:18 祭司和先知也流亡异乡”或译“连祭司和先知也浑浑噩噩,不知道自己做什么”。。’”

19耶和华啊,你完全丢弃犹大了吗?

你厌恶锡安吗?

你为什么把我们打得伤痕累累,以致无法医治?

我们期待平安,却没有平安;

渴望得到医治,却饱受惊吓。

20耶和华啊,我们承认自己和我们祖先的罪,

我们都得罪了你。

21为了你的尊名,

求你不要厌恶我们,

不要让你荣耀的宝座蒙羞。

求你顾念你与我们立的约,

不要废除它。

22在列国供奉的偶像中,

谁能赐下雨水呢?

天能自降甘霖吗?

我们的上帝耶和华啊,

难道不是只有你能行这些事吗?

是你赐雨水降甘霖,

所以我们仰望你。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 14:1-22

Chilala, Njala, Lupanga

1Awa ndi mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya onena za chilala:

2“Yuda akulira,

mizinda yake ikuvutika;

anthu ake adzigwetsa pansi mwachisoni,

kulira kwa Yerusalemu kwakula.

3Anthu awo wolemekezeka akutuma antchito awo kuti akatunge madzi.

Apita ku zitsime

osapezako madzi.

Choncho amabwerera ndi mitsuko yopanda madzi.

Amanyazi ndi othedwa nzeru

adziphimba kumaso.

4Popeza pansi pawumiratu

chifukwa kulibe madzi,

alimi ali ndi manyazi

ndipo amphimba nkhope zawo.

5Ngakhale mbawala yayikazi

ikusiya mwana wake wakhanda ku thengo

chifukwa kulibe msipu.

6Mbidzi zikuyima pa zitunda zopanda kanthu

nʼkumapuma wefuwefu ngati nkhandwe;

maso awo achita chidima

chifukwa chosowa msipu.”

7Anthu akuti, “Ngakhale machimo athu akutitsutsa,

koma Inu Yehova chitanipo kanthu chifukwa cha dzina lanu.

Pakuti kusakhulupirika kwathu nʼkwakukulu;

ife takuchimwirani.

8Inu Yehova amene Aisraeli amakukhulupirirani

ndi amene mumawapulumutsa pa nthawi ya masautso,

chifukwa chiyani mukukhala ngati mlendo mʼdziko muno?

Chifukwa chiyani muli ngati wapaulendo amene akungogona tsiku limodzi?

9Chifukwa chiyani muli ngati munthu amene wadzidzimutsidwa,

kapena ngati wankhondo amene alibe mphamvu yopulumutsa?

Komabe Inu Yehova, muli pakati pathu,

ndipo tikudziwika ndi dzina lanu;

musatitaye ife!”

10Zimene Yehova akunena za anthuwa ndi izi:

“Iwo amakonda kuyendayenda kwambiri;

samatha kudziretsa.

Nʼchifukwa chake Ine Yehova sindingawalandire,

ndipo tsopano ndidzakumbukira zoyipa zawo

ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo.”

11Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Usawapempherere anthu awa kuti zinthu ziwayendere bwino. 12Ngakhale asale zakudya, Ine sindidzamva kulira kwawo; ngakhale apereke nsembe zopsereza ndi chopereka cha chakudya, sindidzazilandira. Mʼmalo mwake, ndidzawapha ndi lupanga, njala ndi mliri.”

13Koma ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova, aneneri amawawuza anthuwo kuti, sadzaphedwa ndi lupanga kapena kuvutika ndi njala. Koma kuti Inu mudzawapatsa mtendere wokhawokha pamalo pano.”

14Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ndi zabodza kuti aneneriwa akunenera mʼdzina langa. Ine sindinawatume kapena kuwasankha kapenanso kuyankhula nawo. Iwo amakuwuzani zinthu zabodza zomwe amati anaziona mʼmasomphenya, kapena pogwiritsa ntchito mawula achabechabe. Zimene amayankhula ndi zongopeka mʼmutu mwawo. 15Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti aneneri amenewa akulosera mʼdzina langa pamene Ine sindinawatume. Iwo amati simudzafa pa nkhondo kapena ndi njala mʼdziko muno. Koma tsono ndi iwowo, aneneriwa amene adzafe pa nkhondo kapena ndi njala. 16Ndipo anthu amene anawaloserawo adzaponyedwa mʼmisewu ya mu Yerusalemu atafa ndi njala ndi lupanga. Sipadzapezeka wowayika mʼmanda popeza iwowo, akazi awo, ana awo aamuna, onse adzakhala atafa. Ine ndidzawagwetsera chilango chowayenera.

17“Awuze mawu awa:

“ ‘Maso anga akugwetsa misozi kosalekeza

usana ndi usiku;

chifukwa anthu anga okondedwa

apwetekeka kwambiri,

akanthidwa kwambiri.

18Ndikapita kuthengo,

ndikuona amene aphedwa ndi lupanga;

ndikapita mu mzinda,

ndikuona amene asakazidwa ndi njala.

Ngakhale aneneri pamodzi

ndi ansembe onse atengedwa.’ ”

19Kodi anthu a ku Yuda mwawakana kwathunthu?

Kodi mtima wanu wanyansidwa nawo anthu a ku Ziyoni?

Chifukwa chiyani mwatikantha chotere

kuti sitingathenso kuchira?

Ife tinayembekezera mtendere

koma palibe chabwino chomwe chabwera,

tinayembekezera kuchira

koma panali kuopsezedwa kokhakokha.

20Inu Yehova, ife tikuvomereza kuyipa kwathu

ndiponso kulakwa kwa makolo athu;

ndithu ife tinakuchimwiranidi.

21Musatikane kuopa kuti dzina lanu linganyozedwe;

musanyoze mpando wanu waufumu waulemerero.

Kumbukirani pangano lanu ndi ife

ndipo musachiphwanye.

22Mwa milungu yachabechabe ya anthu a mitundu ina,

kodi pali mulungu amene angagwetse mvula?

Ife chikhulupiriro chathu chili pa Inu,

popeza Inu nokha ndinu Yehova Mulungu wathu

amene mukhoza kuchita zimenezi.