约伯记 6 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约伯记 6:1-30

约伯自述无辜

1约伯回答说:

2“要是能称量我的苦难,

把我的灾殃放在秤上,

3那将比海沙还重;

所以我言语鲁莽。

4因为全能者的箭射中我,

箭毒侵蚀我的灵,

祂使恐惧列队袭来。

5野驴有草岂会叫唤?

牛有饲料岂会哞叫?

6淡食无盐岂可下咽?

蛋白有什么滋味呢?

7我碰都不想碰,

它们令我恶心。

8唯愿我的祈求蒙应允,

愿上帝成全我的冀望,

9愿祂压碎我,

伸手毁灭我。

10这样,我还能感到欣慰,

在残酷的痛苦中雀跃,

因我没有违背圣者之言。

11我有何力量可以支撑下去?

有何前景让我忍耐下去?

12我的力量岂能坚如石?

我岂是铜造之躯?

13我毫无自救之力,

已到穷途末路。

14“即使绝望者抛弃对上帝的敬畏,

也应该得到朋友的恩待。

15我的弟兄难以信赖,如同季节河,

又像变化无常的河道——

16结冰后颜色发黑,

融雪后水流涨溢;

17水流在干季时消失,

河床在烈日下干涸。

18商队偏离原路来找水喝,

结果在荒漠中死去。

19提玛的商队来找水喝,

示巴的旅客指望解渴,

20结果希望化为泡影,

到了那里大失所望。

21同样,你们帮不了我,

你们看见灾祸便害怕。

22我何尝对你们说过,

‘请你们供应我,

把你们的财产给我一份,

23从仇敌手中拯救我,

从残暴之徒手中救赎我’?

24“请多赐教,我会闭口不言;

请指出我错在何处。

25忠言何等逆耳!

但你们的指责有何根据?

26你们既视绝望者的话如风,

还要来纠正吗?

27你们甚至抽签得孤儿,

把朋友当货物卖掉。

28恳请你们看着我,

我在你们面前撒过谎吗?

29请以仁慈为怀,公正一点;

请以仁慈为怀,因我诚实无过。

30我岂会说诡诈之言?

我岂会是非不辨?

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 6:1-30

Mawu a Yobu

1Tsono Yobu anayankha kuti,

2“Achikhala mavuto anga anayezedwa,

ndipo zipsinjo zanga zonse zikanayikidwa pa sikelo!

3Ndithu, zikanalemera kupambana mchenga wa ku nyanja;

nʼchifukwa chake mawu anga akhala okhadzula.

4Mivi ya Wamphamvuzonse yandibaya,

thupi langa likumva ululu wa miviyo;

zoopsa za Mulungu zandizinga.

5Kodi bulu wakuthengo amalira akakhala ndi msipu,

nanga ngʼombe imalira ikakhala ndi chakudya?

6Kodi chakudya chosakoma nʼkuchidya chopanda mchere,

nanga choyera cha dzira chimakoma?

7Zakudya zimenezi sindifuna nʼkuzilawa komwe;

zakudya zimenezi zimabwerera kukhosi.

8“Aa, ndikanalandira chimene ndikuchipempha,

chikhala Mulungu anandipatsa chimene ndikuchiyembekezera,

9achikhala chinamukomera Mulungu kuti anditswanye,

kulola dzanja lake kuti lindimenye ndi kundiwonongeratu!

10Pamenepo ine ndikanakhalabe ndi chitonthozo ichi,

ndikanakondwa mu ululu wanga wosalekezawu

podziwa kuti sindinakane mawu a Woyerayo.

11“Kodi mphamvu zanga nʼzotani kuti ndizikhalabe ndi chiyembekezo?

Nanga zoyembekezera zanga nʼzotani kuti ndipirirebe?

12Kodi ine ndili ndi mphamvu?

Nanga thupi langa ndi lolimba ngati chitsulo?

13Kodi ndili ndi mphamvu zodzithandizira ndekha,

nanga pakuti thandizo lachotsedwa kwa ine?

14“Munthu amene ali kakasi ayenera kukhala ndi abwenzi odzipereka,

ngakhale kuti iyeyo wasiya kuopa Wamphamvuzonse.

15Koma abale anga ndi wosadalirika ngati mitsinje yowuma msanga,

ngati mitsinje imene imathamanga.

16Ali ngati mitsinje ya madzi akuda nthawi ya dzinja,

imene madzi ake amakhala ambiri chifukwa chakuchuluka kwa mvula,

17koma madziwo amasiya kuyenda nthawi yachilimwe,

ndipo nthawi yotentha madziwo amawumiratu mʼmitsinjemo.

18Anthu oyenda pa ngamira amapatukirako kufuna madzi;

iwo amangoyendayenda nʼkufera mʼchipululu.

19Anthu oyenda pa ngamira a ku Tema amafunafuna madzi,

anthu amalonda apaulendo a ku Seba amafunafuna mwa chiyembekezo.

20Amataya mtima chifukwa ankayembekezera kupeza madzi;

koma akafika kumeneko, amangokhumudwako.

21Tsono inunso mukuonetsa kuti ndinu osathandiza,

mukuona chinthu choopsa kwambiri ndipo mukuchita mantha.

22Kodi ine ndinanenapo kuti, ‘Ndiperekereni kenakake,

ndilipirireni dipo kuchokera pa chuma chanu,

23ndilanditseni mʼdzanja la mdani,

ndiwomboleni mʼdzanja la munthu wankhanza?’

24“Phunzitseni, ndipo ine ndidzakhala chete;

ndionetseni pomwe ndalakwitsa.

25Ndithu, mawu owona ndi opweteka!

Koma mawu anu otsutsa akufuna kuonetsa chiyani?

26Kodi inu mukufuna kundidzudzula pa zimene ndikunena,

ndipo mukufuna kuyesa mawu a munthu wosweka mtima ngati mphepo chabe?

27Inu mungathe kuchita maere kuti mugulitse ana amasiye

ndi kumugulitsa bwenzi lanu.

28“Koma tsopano ndichitireni chifundo pamene mukundiyangʼana.

Kodi ine ndingayankhule zabodza pamaso panu?

29Fewani mtima, musachite zosalungama;

ganiziraninso popeza chilungamo changa chikanalipobe.

30Kodi pali choyipa chilichonse pa milomo yanga?

Kodi pakamwa panga sipangathe kuzindikira kanthu koyipa?