约书亚记 23 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约书亚记 23:1-16

约书亚的诀别之言

1此后很长时间,耶和华使以色列人四境太平,没有战事。约书亚年事已高, 2他召来了以色列的长老、族长、审判官和官长,对他们说:“我已经老了, 3你们都亲眼看见你们的上帝耶和华怎样为了你们而对付列邦,亲自为你们争战。 4约旦河到地中海的这片土地,无论是已征服的还是没有征服的,我已经用抽签的方式分给你们各支派作产业。 5你们的上帝耶和华必把列邦从你们面前赶出去,使他们离开你们。这样,你们就可以承受他们的土地,正如你们的上帝耶和华的应许。 6所以,你们应当刚强,谨遵摩西律法书上所记载的一切,不可有半点偏离。 7不可与你们中间剩下的异族混杂,不可提他们的神明或凭它们起誓,不可供奉、祭拜他们的神明。 8你们要一如既往地倚靠你们的上帝耶和华, 9因为祂为你们赶走了强大的外族人,至今无人敌得过你们。 10你们一个人能打败他们一千人,因为你们的上帝耶和华照着祂的应许为你们争战。 11所以你们要特别谨慎,爱你们的上帝耶和华。 12如果你们悖逆,跟你们当中剩下的异族人联合,通婚往来, 13毫无疑问,你们的上帝耶和华必不再为你们赶走他们。相反,他们还要成为设在你们当中的圈套和陷阱,你们的肉中刺、眼中钉,直到你们在你们的上帝耶和华所赐给你们的这块美好的土地上灭亡。

14“我快要走完人世的路程了。你们深知你们的上帝耶和华赐给你们的一切美好应许没有一句落空,都已经应验了。 15正如你们的上帝耶和华已成就祂应许给你们的一切福气,如果你们违背祂,祂必照样降各样灾祸给你们,直到把你们从祂所赐的这美好土地上毁灭。 16你们如果违背你们的上帝耶和华吩咐你们遵守的约,去供奉、祭拜别的神明,祂必向你们发怒,使你们在祂所赐的这美好土地上迅速灭亡。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 23:1-16

Kutsanzika kwa Yoswa

1Panapita nthawi yayitali kuchokera pamene Yehova anakhazikitsa mtendere pakati pa Aisraeli ndi adani awo owazungulira. Nthawi imeneyi nʼkuti Yoswa atakalamba, ali ndi zaka zambiri. 2Yoswayo anayitanitsa Aisraeli onse pamodzi ndi akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi oyangʼanira anthu antchito ndipo anawawuza kuti, “Ine ndakalamba ndipo ndili ndi zaka zambiri. 3Inu mwaona zonse zimene Yehova Mulungu wanu wachita kwa mitundu yonseyi chifukwa cha inu. Ndi Yehova Mulungu wanu amene anakumenyerani nkhondo. 4Tsono onani! Mitundu ya anthu otsalawa ndayipereka kwa mafuko anu pamodzi ndi mitundu ya anthu ya pakati pa Yorodani ndi Nyanja Yayikulu ya kumadzulo imene ndinayigonjetsa. 5Yehova Mulungu wanu ndiye adzawathamangitsa pamaso panu. Mudzatenga dziko lawo monga Yehova anakulonjezerani.

6“Choncho khalani amphamvu, ndipo samalani kuti mumvere zonse zimene zalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose. Musapatuke pa malamulo onse amene alembedwamo. 7Musagwirizane ndi mitundu ya anthu imene yatsala pakati panu. Musatchule mayina a milungu yawo kapena kuyitchula polumbira. Musayitumikire kapena kuyigwadira. 8Koma mukuyenera kugwiritsa Yehova Mulungu wanu, monga mwachitira mpaka lero lino.

9“Yehova wapirikitsa patsogolo panu mitundu ya anthu ikuluikulu ndi yolimba. Mpaka lero palibe amene watha kulimbana nanu. 10Aliyense wa inu atha kuthamangitsa anthu 1,000 chifukwa Yehova Mulungu wanu ndiye amakumenyerani nkhondo, monga momwe analonjezera. 11Choncho samalitsani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu.

12“Koma ngati mubwerera mʼmbuyo ndi kuphatikizana ndi mitundu yotsalayi imene ili pakati panu ndi kumakwatirana nayo, 13pamenepo mudziwe kuti Yehova, Mulungu wanu, sadzapirikitsa mitundu imeneyi pamaso panu, koma idzakhala ngati msampha kwa inu kapenanso khwekhwe lokukolani. Idzakhala ngati zikwapu pa msana panu kapenanso ngati minga mʼmaso mwanu mpaka mutatha psiti mʼdziko labwinoli limene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.

14“Aliyense wa inu akudziwa mu mtima mwake komanso mʼmoyo mwake kuti zabwino zonse zimene Yehova Mulungu wanu anakulonjezani zachitika. Palibe lonjezo ndi limodzi lomwe limene silinakwaniritsidwe. 15Monga momwe Yehova Mulungu wanu wakuchitirani zabwino zonse zimene ananena kuti adzachita, Yehovayo angathenso kukuchitirani zoyipa zonse zimene waopseza, mpaka kukuchotsani mʼdziko lokoma limene anakupatsani. 16Ngati muphwanya pangano la Yehova Mulungu wanu, limene anakulamulirani nʼkumapita kukatumikira milungu ina ndi kuyigwadira, Yehova adzakukwiyirani, ndiye mudzachotsedwa mʼdziko labwinoli limene Yehova wakupatsani.”