约书亚记 17 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约书亚记 17:1-18

1以下是约瑟的长子玛拿西支派分到的土地:玛拿西的长子、基列的父亲玛吉是个战士,因此分到了基列巴珊两地。 2玛拿西其他的子孙也按宗族分到了土地,他们属于亚比以谢希勒亚斯列示剑希弗示米大宗族。这些男子按宗族都是约瑟的儿子玛拿西的后代。 3玛拿西的玄孙、玛吉的曾孙、基列的孙子、希弗的儿子西罗非哈没有儿子,只有五个女儿,名叫玛拉挪阿曷拉密迦得撒4她们来见祭司以利亚撒的儿子约书亚和各首领,说:“耶和华曾经吩咐摩西在我们亲族中分给我们产业。”约书亚便照耶和华的吩咐,让她们在叔伯中也分到产业。 5除了约旦河东的基列巴珊两地以外,玛拿西人还分到十块土地, 6因为在玛拿西的后代中,女性也分到了产业。玛拿西其他的子孙分到基列地区。

7玛拿西支派分到的产业从亚设开始,到示剑东面的密米他,再向南到隐·他普亚人居住的地方。 8他普亚地属于玛拿西,但在玛拿西边界上的他普亚城属于以法莲的子孙。 9边界继续向南到加拿河,在河南侧玛拿西境内的城邑都归以法莲玛拿西的边界沿着加拿河北侧直到地中海。 10这样,南面归以法莲,北面归玛拿西,西部边界是地中海,北接亚设,东邻以萨迦11以萨迦亚设境内,玛拿西拥有伯·善以伯莲多珥隐·多珥他纳米吉多及其附近的乡村。 12可是,玛拿西人没能把这些城邑的迦南人赶走,因为他们执意不肯离开。 13以色列人国势强盛的时候,就让迦南人服劳役,但始终没有把他们完全赶走。

14约瑟的子孙对约书亚说:“耶和华赐福给我们,使我们人口众多,为什么你只让我们抽一支签,分一份产业呢?” 15约书亚对他们说:“如果你们人口众多,认为以法莲山区窄小,你们可以到比利洗人和利乏音人居住的地方开辟林区。” 16他们答道:“那些地方不够我们住,何况住在伯·善一带和耶斯列平原的迦南人都有铁战车。” 17约书亚约瑟的子孙以法莲人和玛拿西人说:“你们人口众多,势力强大,不应只得一签之地, 18山区也要分给你们,虽然全是森林,但可以开辟土地,使整个地区归你们。虽然迦南人强盛,有铁战车,但你们能够赶走他们。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 17:1-18

1Gawo lina la dzikolo linapatsidwa kwa mabanja ena a fuko la Manase, mwana woyamba kubadwa wa Yosefe. Makiri anali mwana woyamba kubadwa wa Manase ndiponso kholo la anthu okhala ku Giliyadi. Popeza kuti iye anali munthu wankhondo, analandira Giliyadi ndi Basani. 2Mabanja ena otsala a fuko la Manase amene analandira dziko ndi awa: Abiezeri, Heleki, Asirieli, Sekemu, Heferi ndi Semida. Izi ndi zidzukulu zina zazimuna za Manase mwana wa Yosefe ndiponso eni mbumba.

3Panali Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri mwana wa Manase. Iyeyu analibe ana aamuna koma aakazi okhaokha ndipo mayina awo ndi awa: Mahila, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza. 4Iwo anapita kwa Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni, ndi atsogoleri ndipo anati: “Yehova analamula Mose kuti ife ndi alongo athu atipatse cholowa chathu.” Choncho iwowo pamodzi ndi abale a abambo awo anawapatsa dera lina la dzikolo kuti likhale monga mwa lamulo la Yehova. 5Choncho kuwonjezera pa mayiko a Giliyadi ndi Basani kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Manase analandiranso magawo khumi 6chifukwa ana aakazi a fuko la Manase analandira cholowa chawo pakati pa ana aamuna. Dziko la Giliyadi linali dziko la zidzukulu zonse za Manase.

7Malire a dziko la Manase anayambira ku Aseri, ndipo anakafika ku Mikimetati kummawa kwa Sekemu. Tsono malire anapita kummwera kuloza kwa anthu a ku Eni-Tapuwa. 8(Manase anatenga dziko la Tapuwa, koma mzinda wa Tapuwawo, umene unali mʼmalire mwa Manase unali wa fuko la Efereimu). 9Ndipo malire ake anapitirira kummwera mpaka ku mtsinje wa ku Kana. Mizinda ya kummwera kwa mtsinjewo inali ya fuko la Efereimu ngakhale kuti inali mʼdziko la Manase. Malire a fuko la Manase anapita kumpoto kwa mtsinje wa Kana ndi kukathera ku Nyanja. 10Dziko la kummwera linali la Efereimu ndipo la kumpoto linali la Manase. Dziko la Manase linafika ku nyanja ndipo linachita malire ndi Aseri, kumpoto ndiponso Isakara, kummawa.

11Mʼdziko la Isakara ndi Aseri, Manase analinso ndi mizinda ya Beti-Seani ndi Ibuleamu pamodzi ndi midzi yawo yozungulira. Panalinso Akanaani amene ankakhala ku Dori, Endori, Taanaki ndi Megido pamodzi ndi mizinda yozungulira (wachitatu pa mʼndandandawu ndi Nafati Dori).

12Komabe anthu a fuko la Manase sanathe kuwapirikitsa anthu okhala mʼmizinda imeneyi. Choncho Akanaani anakhalabe mʼmizindayi. 13Ngakhale Aisraeli anali a mphamvu mʼdzikomo, sanapirikitse Akanaani onse koma anangowasandutsa kukhala akapolo.

14Anthu a fuko la Yosefe anati kwa Yoswa, “Chifukwa chiyani mwatipatsa gawo limodzi lokha la dziko kuti likhale cholowa chathu? Ife tilipo anthu ambiri popeza Yehova watidalitsa kwambiri.”

15Yoswa anayankha kuti, “Ngati muli ambiri ndipo dziko la ku mapiri la Efereimu lakucheperani kwambiri, lowani ku nkhalango mudule mitengo, mudzikonzere malo akuti mukhalemo, mʼdziko la Aperezi ndi Arefai.”

16Tsono zidzukulu za Yosefe zinati, “Dziko la ku mapiri ndi losatikwaniradi, komanso Akanaani onse amene akukhala ku chigwa pamodzi ndi amene akukhala ku Beti-Seani ndi madera awo ndiponso amene ali ku chigwa cha Yezireeli ali ndi magaleta azitsulo.”

17Koma Yoswa anawuza zidzukulu za Yosefe, za fuko la Efereimu ndi za fuko la Manase kuti, “Inu mulipodi ambiri ndiponso amphamvu. Simulandira gawo limodzi lokha, 18dziko la ku mapiri lidzakhalanso lanu. Ngakhale kuti ndi nkhalango yokhayokha koma inu mudzadula mitengo yake ndipo lidzakhala lanu mpaka kumapeto. Ngakhale kuti Akanaani ali ndi magaleta azitsulo ndiponso kuti iwo ndi amphamvu, koma inu mudzawapirikitsa.”