彼得前书 3 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

彼得前书 3:1-22

夫妻之道

1-2照样,做妻子的要顺服丈夫。这样,即使丈夫不信从真道,也会因为看见妻子贞洁和敬虔的品行而被无声地感化。 3你们不要注重外表的妆饰,像编头发、戴金饰或穿华丽的衣服, 4要以温柔、娴静这些永不褪色的内在美为妆饰,这是上帝所看重的。 5从前那些仰赖上帝的圣洁妇女,都是以这些来妆饰自己,并顺服自己的丈夫, 6正如撒拉顺服亚伯拉罕,称他为主人。所以,如果你们做对的事,不怕恐吓,就是撒拉的女儿。

7你们做丈夫的也一样,要按情理3:7 按情理”希腊文是“按知识”。与妻子共同生活,因为她们比你们软弱。要敬重她们,因为她们和你们一同承受上帝施恩赐下的生命。这样,你们的祷告就可以畅通无阻了。

要为义受苦

8总而言之,你们要同心合意,互相关怀,彼此相爱,仁慈谦虚。 9不要以恶报恶,以辱骂还辱骂,反要祝福对方,这是你们蒙召的目的,好叫你们得到祝福。 10因为圣经上说:

“若有人热爱生命,

渴望幸福,

就要舌头不出恶言,

嘴唇不说诡诈的话。

11要弃恶行善,竭力追求和睦。

12因为主的眼睛看顾义人,

祂的耳朵垂听他们的祈求。

但主必严惩作恶之人。”

13如果你们热心行善,有谁会害你们呢? 14就算你们为义受苦,也是有福的。不要害怕别人的恐吓3:14 不要害怕别人的恐吓”或译“不要怕别人所怕的”。,也不要惊慌, 15要心里尊基督为主。如果有人问起你们心中的盼望,你们要随时准备答复, 16但态度要温和恭敬,存无愧的良心。这样,那些对你们因信基督而有的好品行妄加诬蔑的人会自觉羞愧。 17如果上帝的旨意是要你们因行善而受苦,这也总比你们因作恶而受苦强。

18因为基督也曾一次为罪受苦,以无罪之身代替不义之人,为要领你们到上帝面前。祂的肉体虽被处死,但祂借着圣灵复活了。 19祂还借着圣灵向那些监狱中的灵魂传道, 20他们就是从前在挪亚造方舟、上帝耐心等候人们悔改的时代中那些不肯信的人。当时进入方舟,从洪水中得救的人很少,只有八个人。 21这水代表的洗礼现在借着耶稣基督的复活也拯救了你们。这洗礼要表明的不是除掉肉体的污秽,而是求在上帝面前有无愧的良心。 22基督已经升到天上,坐在上帝的右边,众天使、掌权的、有能力的都服从了祂。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Petro 3:1-22

Akazi ndi Amuna

1Momwemonso, akazi inu gonjerani amuna anu kuti ngati ena a iwo sakhulupirira Mawu a Mulungu, akopeke ndi makhalidwe a akazi awo ndipo sipadzafunikanso mawu 2pamene aona moyo wanu wachiyero ndi moyo woopa Mulungu. 3Kudzikongoletsa kwanu kusakhale kwa maonekedwe akunja, monga kuluka tsitsi ndi kuvala zokometsera zagolide ndi zovala zamberewere. 4Mʼmalo mwake kudzikongoletsa kwanu kukhale kwa munthu wa mʼkatimo, kukongola kosatha kwa mtima ofatsa ndi mzimu wachete, zimene ndi za mtengowapatali pamaso pa Mulungu. 5Pakuti umo ndi mmene akazi oyera mtima akale amene anali ndi chiyembekezo pa Mulungu anadzikongoletsera. Iwo ankagonjera amuna awo, 6monga Sara, amene anamvera Abrahamu namutcha iye mbuye wake. Akazi inu ndinu ana ake ngati muchita zoyenera, ndipo musaope choopsa chilichonse.

7Momwemonso amuna inu, khalani mwanzeru ndi akazi anu, ndipo muwachitire ulemu monga anzanu ofowoka ndiponso olandira nanu pamodzi mphatso ya moyo wosatha, kuti pasakhale kanthu kotsekereza mapemphero anu.

Kumva Zowawa Chifukwa cha Chilungamo

8Potsiriza, nonse khalani a mtima umodzi, omverana chisoni. Kondanani monga abale, muchitirane chifundo ndi kudzichepetsa. 9Wina akakuchitirani choyipa musabwezere pochitanso choyipa, kapena kubwezera chipongwe akakuchitirani chipongwe, koma muwadalitse. Munayitanidwa kuti mulandire mdalitso. 10Pakuti,

“Iye amene angakonde moyo

ndi kuona masiku abwino,

aletse lilime lake kuyankhula zoyipa,

ndiponso milomo yake kunena mabodza.

11Apewe zoyipa, ndipo azichita zabwino.

Afunefune mtendere ndi kuyesetsa kuwupeza.

12Pakuti Ambuye amayangʼanira bwino anthu olungama

ndipo amatchera khutu ku mapemphero awo.

Koma Ambuye sawayangʼana bwino amene amachita zoyipa.”

13Ndani angakuchitireni zoyipa ngati muchita changu kuchita zabwino? 14Koma ngakhale mumve zowawa chifukwa cha chilungamo, ndinu odala. “Musaope anthu, musachite mantha.” 15Koma lemekezani Khristu mʼmitima mwanu ngati Ambuye wanu. Khalani okonzeka nthawi zonse kuyankha aliyense amene akufunsani za chiyembekezo chimene muli nacho. 16Koma chitani zimenezi mofatsa ndi mwaulemu, mukhale ndi chikumbumtima chosakutsutsani, kuti anthu ena akanena zoyipa za makhalidwe anu abwino mwa Khristu, achite okha manyazi ndi chipongwe chawocho. 17Nʼkwabwino ngati ndi chifuniro cha Mulungu kumva zowawa chifukwa chochita zabwino kusiyana ndi kumva zowawa chifukwa chochita zoyipa. 18Pakuti Khristu anafa chifukwa cha machimo kamodzi kokha kufera onse, wolungama kufera osalungama, kuti akufikitseni kwa Mulungu. Anaphedwa ku thupi koma anapatsidwa moyo mu mzimu. 19Ndipo ali ngati mzimu chomwecho anapita ndi kukalalikira mizimu imene inali mʼndende, 20ya anthu amene sanamvere Mulungu atadikira moleza mtima pa nthawi imene Nowa ankapanga chombo. Mʼchombo chija anthu owerengeka okha, asanu ndi atatu, ndiwo anapulumutsidwa ku madzi. 21Madziwo akufanizira ubatizo umene lero ukukupulumutsaninso, osati chifukwa chochotsa litsiro la mʼthupi koma chifukwa cha chikumbumtima choona pamaso pa Mulungu. Umakupulumutsani chifukwa cha kuuka kwa Yesu Khristu, 22amene anapita kumwamba ndipo ali kudzanja lamanja la Mulungu komwe angelo ndi maulamuliro ndi amphamvu amamvera Iye.