尼希米记 6 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

尼希米记 6:1-19

敌人阴谋阻挠重建

1参巴拉多比雅阿拉伯基善和我们其余的敌人听说我已修完城墙,没有留下任何缺口——那时我还没有为城门安上门扇—— 2参巴拉基善就派人告诉我说:“来,我们在阿挪平原的一个村庄见面吧。”其实他们想要害我。 3我派人回复他们说:“我正在做一件大工程,不能下去见你们。我怎能停止工作下去见你们呢?” 4他们四次派人来告诉我,每次我都这样拒绝了。 5参巴拉第五次派人送来一封未封口的信, 6上面写着:“各国都在谣传,基善也说,你和犹太人计划谋反,因而才修建城墙,据说你要做他们的王。 7你还派先知在耶路撒冷指着你预言说,‘犹大有王了。’如今王必听到这些传闻。所以你还是来与我们一同商议吧。” 8我就派人答复他说:“你所说的并非事实,是你心里捏造的。” 9因为他们想恐吓我们,以为我们会吓得手发软,无法完成工程。但上帝啊,求你使我的手有力量!

10我到米希达别的孙子、第来雅的儿子示玛雅的家中,那时他正闭门不出。他对我说:“我们在上帝的殿里会面,要关上殿门,因为他们要来杀你,要在夜间杀你。” 11但我回答说:“像我这样的人岂能逃跑?岂能进入殿里保命?我决不进去。” 12我察觉上帝并没有差派他,他是被多比雅参巴拉收买才说预言攻击我的。 13他们收买他是为了恐吓我,使我依从他去犯罪,好毁坏我的名声、羞辱我。 14我的上帝啊,求你按照他们的行为报应多比雅参巴拉、女先知挪亚底及其他恐吓我的先知。

工程竣工

15以禄月6:15 以禄月”即希伯来历的六月,阳历是八月中旬到九月中旬。二十五日城墙竣工,前后用了五十二天。 16我们的敌人和周围各国听说后,都感到惧怕和气馁,因为他们知道这工作是在上帝的帮助下完成的。 17在那些日子,多比雅犹大贵族之间多有书信来往。 18犹大有很多人与多比雅结盟,因为他是亚拉的儿子示迦尼的女婿,他儿子约哈难又娶了比利迦的儿子米书兰的女儿为妻。 19他们常告诉我有关多比雅的善行,并把我的话告诉他。多比雅不断写信恐吓我。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nehemiya 6:1-19

Adani Apitiriza Kutsutsa ndi Kuopseza Nehemiya

1Pamenepo Sanibalati, Tobiya, Gesemu Mwarabu ndi adani athu anamva kuti ndatsiriza ntchito yomanganso khoma ndi kuti palibe mpata umene watsala ngakhale kuti pa nthawi imeneyi ndinali ndisanayike zitseko pa zipata. 2Sanibalati ndi Gesemu, ananditumizira uthenga uwu: “Bwerani tidzakumane pa mudzi wina ku chigwa cha Ono.”

Koma iwo anakonzekera kuti akandichite chiwembu kumeneko. 3Choncho ine ndinatuma amithenga ndi yankho ili: “Ine ndikugwira ntchito yayikulu kuno ndipo sindingathe kubwera kumeneko. Kodi ntchito iyime pofuna kuti ndibwere kumeneko?” 4Ananditumizira uthenga umodzimodzi omwewu kanayi ndipo ndinawayankha chimodzimodzi.

5Tsono kachisanu, Sanibalati anatumiza wantchito wake ndi kalata yosamata. 6Mu kalatamo munali mawu akuti,

“Pali mphekesera pakati pa mitundu ya anthu, ndiponso Gesemu akunena zomwezo kuti inu ndi Ayuda onse mufuna kuwukira boma. Nʼchifukwa chake mukumanga khoma. Mphekeserazo zikutinso inu mukufuna kudzakhala mfumu yawo. 7Mwayikanso kale aneneri amene adzalengeza za iwe mu Yerusalemu kuti ‘Mu Yuda muli mfumu!’ Tsono nkhani iyi imveka ndithu kwa mfumu. Choncho bwerani kuti tidzakambirane.”

8Ine ndinatumiza yankho ili: “Pa zimene mukunenazo, palibe chimene chinachitikapo. Inu mukungozipeka mʼmutu mwanu.”

9Apa adani athu onsewa ankangofuna kutiopseza. Iwo ankaganiza kuti “Tichita mantha ndi kuleka kugwira ntchito.”

Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu ndilimbitseni mtima.”

10Tsiku lina ndinapita ku nyumba ya Semaya mwana wa Delaya mwana wa Mehatabeli. Tsono anandiwuza kuti, “Tiyeni tikakumanire ku Nyumba ya Mulungu. Tikabisale mʼmenemo ndi kutseka zitseko chifukwa akubwera kudzakuphani. Ndithu usiku uno akubwera kudzakuphani.”

11Koma ndinayankha kuti, “Kodi munthu ngati ine nʼkuthawa? Kapena munthu wofanana ndi ine nʼkupita ku Nyumba ya Mulungu kuti apulumutse moyo wake? Ayi, ine sindipita!” 12Ndinazindikira kuti Mulungu sanamutume koma kuti anayankhula mawu oloserawa motsutsana nane chifukwa Tobiya ndi Sanibalati anamulemba ntchitoyi. 13Iye analembedwa ntchitoyi ndi cholinga choti ine ndichite mantha, ndithawe. Ndikanatero ndiye kuti ndikanachimwira Yehova ndiponso iwowo akanandiyipitsira mbiri yanga ndi kumandinyoza.

14Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu wanga, kumbukirani Tobiya ndi Sanibalati chifukwa cha zimene achita. Kumbukiraninso mneneri wamkazi Nowadiya ndi aneneri amene akhala akufuna kundiopseza.”

Kutsiriza kwa Khoma

15Ndipo khoma linatsirizidwa kumanga pa tsiku la 25 la mwezi wa Eluli. Linamangidwa pa masiku okwana 52. 16Adani athu onse atamva izi, mitundu yonse ya anthu yozungulira inachita mantha ndi kuchita manyazi. Iwo anazindikira kuti ntchitoyo inachitika ndi thandizo la Mulungu wathu.

17Komanso masiku amenewo anthu olemekezeka a ku Yuda ankalemberana naye makalata ambiri ndi Tobiyayo, 18pakuti anthu ambiri a ku Yuda anali atalumbira kale kuti adzagwira naye ntchito popeza anali mkamwini wa Sekaniya mwana wa Ara, ndipo mwana wake Yehohanani anakwatira mwana wamkazi wa Mesulamu mwana wa Berekiya. 19Kuwonjezera apo, anthu ankasimba za ntchito zake zabwino ine ndili pomwepo ndipo anakamuwululira mawu anga. Choncho Tobiyayo ankatumiza makalata ondiopseza.