尼希米记 4 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

尼希米记 4:1-23

尼希米战胜阻力

1参巴拉听说我们正在重建城墙,非常愤怒,就嘲笑犹太人, 2当着他的同僚和撒玛利亚军兵的面说:“这群弱小的犹太人在做什么呢?要重建城墙吗?要献祭吗?要在一日之间建好吗?要用废墟中烧过的石头来建造吗?”

3他身旁的多比雅说:“他们建的石墙,一只狐狸上去就能踩倒!”

4我祷告说:“我们的上帝啊,求你垂听,因为我们正在被人耻笑。求你使他们对我们的凌辱归到他们自己头上,使他们被掳到外邦。 5不要遮掩他们的恶行,也不要从你面前涂抹他们的罪恶,因为他们在这些建造的人面前惹你发怒。”

6众人全心做工,把整个城墙连接起来,高达原来的一半。

7参巴拉多比雅阿拉伯人、亚扪人和亚实突人听说耶路撒冷的城墙正在重建、缺口正在填补,非常愤怒, 8便一起图谋袭击耶路撒冷,使城内混乱。 9但我们向我们的上帝祷告,并设立守卫昼夜防备他们。

10犹大人说:“工人已经筋疲力尽,还有太多瓦砾有待清理,我们自己无法重建城墙。” 11我们的敌人说:“我们要趁他们不知不觉,进入他们中间杀死他们,阻止他们的工作。” 12靠近敌人居住的犹太人十次来告诉我们,说敌人会从各方来袭击我们4:12 本节希伯来文意义不明。13于是,我按宗族派人手持刀剑、长矛和弓箭守卫在城墙后面低洼的空地上。 14我察看形势后,起来对贵族、官员和其他民众说:“不要怕他们!要记住,主伟大而可畏。要为你们的兄弟、儿女、妻子和家园而战。”

15敌人听说我们知道了他们的阴谋,上帝已破坏他们的诡计,就没有来。我们回到城墙那里,继续各人的工作。 16从那时起,我的仆人一半继续修筑城墙,一半身穿盔甲,手持长矛、盾牌和弓箭负责守卫。官长都站在修筑城墙的所有犹大人后面。 17搬运工人一手工作,一手拿兵器。 18修筑城墙的人工作的时候都腰间配剑。吹号的人在我旁边, 19我对贵族、官员和其余的民众说:“这工程浩大,范围广阔,我们在城墙上相隔很远, 20因此你们一听见号角声,就要聚到我那里。我们的上帝必为我们争战!”

21这样,从黎明直到星星出现,我们的人一半工作,一半手持兵器守卫。 22那时,我又吩咐众人各带仆人在耶路撒冷住宿。他们夜间可以帮我们守卫,白天帮我们工作。 23我和我的兄弟、仆人及跟从我的守卫都衣不解带,刀不离身4:23 刀不离身”或译“出去打水时也带着刀”。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nehemiya 4:1-23

Adani a Nehemiya pa Ntchito Yake

1Sanibalati atamva kuti tikumanganso khoma anapsa mtima nayamba kuseka ndi kunyogodola Ayuda kwambiri. 2Ndipo anayankhula pamaso pa abale ake ndi asilikali a Samariya kuti, “Kodi Ayuda ofowokawa akuchita chiyani? Kodi iwo nʼkumanganso khoma? Kodi adzaperekanso nsembe? Kodi adzatsiriza ntchitoyi tsiku limodzi? Kodi adzachita kutenga miyala yakale ija ndi mmene inapseramo?”

3Tobiya wa ku Amoni, amene anali naye anati, “Chimene akumangacho ngati nkhandwe itakwerapo, itha kugwetsa khoma lawolo!”

4Tsono ndinayamba kupemphera kuti, “Timvereni, Inu Mulungu wathu, mmene akutinyozera. Mulole kuti mawu awo onyoza awabwerere, ndipo atengedwe ukapolo ku dziko lachilendo. 5Musawakhululukire mphulupulu zawo kapena kufafaniza machimo awo pamaso panu popeza aputa ukali wanu pamaso pa anthu omanga khoma.”

6Choncho ife tinamangabe khomalo kufikira lonse litafika theka la msinkhu wake, chifukwa chakuti anthu anagwira ntchitoyo ndi mtima wawo wonse.

7Koma pamene Sanibalati, Tobiya, Aarabu, Aamoni ndi anthu a ku Asidodi anamva kuti ntchito yokonzanso makoma a Yerusalemu ikupitirirabe ndipo kuti mipata ikutsekedwa, anapsa mtima kwambiri. 8Tsono onse anapangana za chiwembu kuti abwere ndi kudzathira nkhondo anthu a ku Yerusalemu ndi kuyambitsa mapokoso pakati pawo. 9Koma ife tinapemphera kwa Mulungu wathu ndipo tinayika alonda otiteteza kwa adaniwo usiku ndi usana.

10Pa nthawi yomweyi anthu a ku Yuda anati, “Mphamvu za anthu onyamula zinyalala zikutha ndipo pali zinyalala zambiri. Choncho ife sititha kumanga khomali.”

11Adani athunso anati, “Iwo asanadziwe izi, kapena kutiona, tidzakhala tili pakati pawo ndipo tidzawapha ndi kuyimitsa ntchitoyo.”

12Ndipo Ayuda amene ankhala pafupi ndi adani athuwo anabwera kakhumi konse kuchokera konse kumene ankakhala kudzatiwuza kuti tibwereko ku ntchito.

13Choncho kumbuyo kwa khoma, cha mʼmunsi mwake komanso malo amene anali asanathe ndinayikamo anthu mʼmabanja atatenga malupanga, mikondo ndi mauta awo. 14Popeza anthu ankachita mantha, tsono ndinawawuza anthu olemekezeka, akuluakulu ndiponso anthu onse kuti, “Musawaope. Kumbukirani kuti Ambuye ndi wamkulu ndipo ndi woopsa. Choncho menyerani nkhondo abale anu, ana aamuna ndi aakazi, akazi anu ndi nyumba zanu.”

15Adani athu atamva kuti ife tadziwa za chiwembu chawo, anadziwanso kuti Yehova walepheretsa zimene ankafuna kutichita. Choncho tinabwerera aliyense ku ntchito yake yomanga khoma.

16Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo mwake, theka la antchito anga linkagwira ntchito, pamene theka linalo limatenga mikondo, zishango, mauta ndi kuvala malaya azitsulo. Akuluakulu ankalimbikitsa Ayuda onse 17amene ankamanga khoma. Anthu onyamula zinyalala aja ankagwira ntchito ndi dzanja limodzi, dzanja linali atanyamula chida chankhondo. 18Mʼmisiri aliyense ankamangirira lupanga lake mʼchiwuno mwake akamagwira ntchito. Koma munthu woyimba lipenga anali pambali panga nthawi zonse.

19Ndipo ine ndinati kwa anthu olemekezeka ndi anthu ena onse, “Ntchitoyi ndi yayikulu ndipo ili padera lalikulu ndipo ifeyo takhala motayanatayana kwambiri pa khoma. 20Tsono kulikonse kumene muliko, mukamva kulira kwa lipenga bwerani mudzasonkhane kumene kuli ine kuno. Mulungu wathu adzatimenyera nkhondo.”

21Choncho enafe tinapitiriza kugwira ntchito, pamene theka lina linkanyamula mikondo kuyambira mʼbandakucha mpaka nyenyezi zitaoneka. 22Pa nthawi imeneyo ndinawuzanso anthuwo kuti, “Aliyense pamodzi ndi wantchito wake agone mu Yerusalemu kuti tikhale ndi otilondera usiku ndi kuti masana tizigwira ntchito.” 23Choncho ine, anzanga, antchito anga, ndi anthu otiteteza amene ankanditsata panalibe ndi mmodzi yemwe anavula zovala zake pogona. Aliyense anasunga chida chake chankhondo pambali pake.