启示录 22 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

启示录 22:1-21

1天使让我看城内街道当中一道流淌着生命水的河,清澈如水晶,从上帝和羔羊的宝座那里流出。 2河两岸有结十二种果子的生命树,每个月都结果子,叶子能医治万民。 3再也没有咒诅,因为城里有上帝和羔羊的宝座,祂的奴仆都要事奉祂。 4他们必见上帝的面,上帝的名字必印在他们的额上。 5再没有黑夜,也不需要灯光和阳光,因为主上帝必做他们的光。他们要执掌王权直到永永远远。

基督的再来

6天使对我说:“这些话真实可靠。赐圣灵感动众先知的主上帝已差遣祂的天使,将那些快要发生的事指示给祂的奴仆们。”

7“看啊,我快要来了。遵行这书中预言的人有福了!”

8以上都是我约翰亲眼看见、亲耳听见的事。当我听见、看见这些事后,就俯伏敬拜将这一切指示给我的天使。 9天使对我说:“千万不可!我与你、你的众先知弟兄和那些遵行这书上话语的人同是上帝的奴仆,你要敬拜上帝。”

10他又对我说:“不可封住这卷书上的预言,因为时候快到了。 11不义的,让他继续不义;污秽的,让他继续污秽;公义的,让他保持公义;圣洁的,让他保持圣洁。”

12“看啊,我快要来了,到时候我要按各人的行为施行赏罚。 13我是阿拉法,我是俄梅加;我是首先的,我是末后的;我是开始,我是终结。 14那些洗净自己衣裳的人有福了!他们有权吃生命树的果子,也可以从城门进入城中。 15那些如同恶犬的败类、行邪术的、淫乱的、杀人的、拜偶像的和一切喜欢弄虚作假的,都要被拒之城外。 16我耶稣差遣我的天使到众教会,向你们证明这些事。我是大卫的根,也是大卫的后裔,又是明亮的晨星。”

17圣灵和新娘都说:“来吧!”听见的也要说:“来吧!”口渴的,让他来吧!愿意的,让他白白享用生命水吧!

警告

18我郑重警告所有听见这书上预言的人:如果谁在这书上增添什么,上帝必将这书上所记载的灾祸加在他身上; 19如果有人从这预言书上删减什么,上帝必使他无份于这书上所记载的生命树和圣城。

20那位证明这些事的说:“是的,我快要来了。”阿们!主耶稣啊,我愿你来!

21愿主耶稣的恩典与众圣徒同在。阿们!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 22:1-21

Mtsinje Wamoyo

1Ndipo mngeloyo anandionetsa mtsinje wamadzi amoyo, oyera ngati mwala wa krustalo ukutuluka ku mpando waufumu wa Mulungu ndi wa Mwana Wankhosa, 2Ukuyenda pakati pa msewu waukulu wa mu mzindawo. Mbali iliyonse ya mtsinjewo kunali mtengo wamoyo, utabala zipatso khumi ndi ziwiri. Kubereka zipatso mwezi uliwonse. Ndipo masamba a mtengowo ndi mankhwala wochiritsa anthu a mitundu ina. 3Sipadzakhalanso temberero lililonse. Mpando waufumu wa Mulungu ndi wa Mwana Wankhosa udzakhala mu mzindawo, ndipo atumiki ake adzamutumikira. 4Iwo adzaona nkhope yake ndipo dzina lake lidzalembedwa pa mphumi zawo. 5Sipadzakhalanso usiku. Sadzafuna kuwala kwa nyale kapena kwa dzuwa pakuti Ambuye Mulungu adzakhala kuwala kwawo. Ndipo adzalamulira kwamuyaya.

6Mngeloyo anandiwuza kuti, “Mawu awa ndi okhulupirika ndi owona. Ambuye Mulungu wa mizimu ya aneneri anatumiza mngelo wake kudzaonetsa atumiki ake zinthu zimene ziyenera kuchitika posachedwapa.”

Yesu Akubweranso

7“Taonani, ndikubwera posachedwa! Wodala ndi amene asunga mawu oneneratu za kutsogolo a mʼbuku ili.”

8Ine Yohane, ndine amene ndinamva ndi kuona zinthu izi. Ndipo pamene ndinamva ndi kuona izi ndinagwa pansi kuti ndipembedze mngelo amene amandionetsa zimenezi. 9Koma mngeloyo anandiwuza kuti, “Usatero ayi! Ine ndine wotumikira monga iwe pamodzi ndi abale ako aneneri ndi onse amene amasunga mawu a mʼbuku pembedzani Mulungu.”

10Kenaka anandiwuza kuti, “Usabise mawu onena zamʼtsogolo a mʼbuku ili chifukwa nthawi yayandikira. 11Wochita zoyipa apitirire kuchita zoyipazo; wochita zonyansa apitirire kuchita zonyansazo; wochita zabwino apitirire kuchita zabwinozo; ndipo woyera mtima apitirire kukhala woyera mtima.”

Mawu Otsiriza: Kuyitanidwa ndi Chenjezo

12“Taonani, ndikubwera posachedwa! Ndikubwera ndi mphotho zanga kuti ndidzapereke kwa aliyense malinga ndi zimene anachita. 13Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza, Chiyambi ndi Chimaliziro ndine.

14“Odala amene achapa mikanjo yawo, kuti akhale ndi ufulu wopita ku mtengo wamoyo ndi kuti akalowe mʼzipata za mu mzindawo. 15Kunja kuli agalu, amatsenga, achiwerewere, akupha anthu, opembedza mafano ndi aliyense amene amakonda bodza ndi kulichita.

16“Ine Yesu, ndatuma mngelo wanga kuti achitire umboni uwu ku mipingo. Ine ndine Muzu ndi Chipatso cha Davide ndipo ndine Nthanda Yonyezimira.”

17Mzimu Woyera ndi mkwatibwi akuti, “Bwerani!” Ndipo amene akumva anena kuti Bwerani! Iye amene ali ndi ludzu abwere, ndipo aliyense amene afuna alandire mphatso yaulere ya madzi amoyo.

18Ndikuchenjeza aliyense amene akumva mawu onena zamʼtsogolo a mʼbukuli kuti, “Ngati wina awonjezerapo kalikonse, Mulungu adzamuwonjezera miliri imene yalembedwa mʼbuku ili. 19Ndipo wina akachotsapo mawu onena zamʼtsogolo a mʼbuku ili, Mulungu adzachotsa gawo lake pa mtengo wamoyo ndi la mu mzinda woyera zimene zanenedwa mʼbuku ili.”

20Iye amene akuchitira umboni pa zinthu izi akuti, “Inde, Ine ndikubwera posachedwa.”

Ameni. Bwerani Ambuye Yesu.

21Chisomo cha Ambuye Yesu chikhale ndi anthu onse. Ameni.